1 Petro 3 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Petro 3:1-22

Akazi ndi Amuna

1Momwemonso, akazi inu gonjerani amuna anu kuti ngati ena a iwo sakhulupirira Mawu a Mulungu, akopeke ndi makhalidwe a akazi awo ndipo sipadzafunikanso mawu 2pamene aona moyo wanu wachiyero ndi moyo woopa Mulungu. 3Kudzikongoletsa kwanu kusakhale kwa maonekedwe akunja, monga kuluka tsitsi ndi kuvala zokometsera zagolide ndi zovala zamberewere. 4Mʼmalo mwake kudzikongoletsa kwanu kukhale kwa munthu wa mʼkatimo, kukongola kosatha kwa mtima ofatsa ndi mzimu wachete, zimene ndi za mtengowapatali pamaso pa Mulungu. 5Pakuti umo ndi mmene akazi oyera mtima akale amene anali ndi chiyembekezo pa Mulungu anadzikongoletsera. Iwo ankagonjera amuna awo, 6monga Sara, amene anamvera Abrahamu namutcha iye mbuye wake. Akazi inu ndinu ana ake ngati muchita zoyenera, ndipo musaope choopsa chilichonse.

7Momwemonso amuna inu, khalani mwanzeru ndi akazi anu, ndipo muwachitire ulemu monga anzanu ofowoka ndiponso olandira nanu pamodzi mphatso ya moyo wosatha, kuti pasakhale kanthu kotsekereza mapemphero anu.

Kumva Zowawa Chifukwa cha Chilungamo

8Potsiriza, nonse khalani a mtima umodzi, omverana chisoni. Kondanani monga abale, muchitirane chifundo ndi kudzichepetsa. 9Wina akakuchitirani choyipa musabwezere pochitanso choyipa, kapena kubwezera chipongwe akakuchitirani chipongwe, koma muwadalitse. Munayitanidwa kuti mulandire mdalitso. 10Pakuti,

“Iye amene angakonde moyo

ndi kuona masiku abwino,

aletse lilime lake kuyankhula zoyipa,

ndiponso milomo yake kunena mabodza.

11Apewe zoyipa, ndipo azichita zabwino.

Afunefune mtendere ndi kuyesetsa kuwupeza.

12Pakuti Ambuye amayangʼanira bwino anthu olungama

ndipo amatchera khutu ku mapemphero awo.

Koma Ambuye sawayangʼana bwino amene amachita zoyipa.”

13Ndani angakuchitireni zoyipa ngati muchita changu kuchita zabwino? 14Koma ngakhale mumve zowawa chifukwa cha chilungamo, ndinu odala. “Musaope anthu, musachite mantha.” 15Koma lemekezani Khristu mʼmitima mwanu ngati Ambuye wanu. Khalani okonzeka nthawi zonse kuyankha aliyense amene akufunsani za chiyembekezo chimene muli nacho. 16Koma chitani zimenezi mofatsa ndi mwaulemu, mukhale ndi chikumbumtima chosakutsutsani, kuti anthu ena akanena zoyipa za makhalidwe anu abwino mwa Khristu, achite okha manyazi ndi chipongwe chawocho. 17Nʼkwabwino ngati ndi chifuniro cha Mulungu kumva zowawa chifukwa chochita zabwino kusiyana ndi kumva zowawa chifukwa chochita zoyipa. 18Pakuti Khristu anafa chifukwa cha machimo kamodzi kokha kufera onse, wolungama kufera osalungama, kuti akufikitseni kwa Mulungu. Anaphedwa ku thupi koma anapatsidwa moyo mu mzimu. 19Ndipo ali ngati mzimu chomwecho anapita ndi kukalalikira mizimu imene inali mʼndende, 20ya anthu amene sanamvere Mulungu atadikira moleza mtima pa nthawi imene Nowa ankapanga chombo. Mʼchombo chija anthu owerengeka okha, asanu ndi atatu, ndiwo anapulumutsidwa ku madzi. 21Madziwo akufanizira ubatizo umene lero ukukupulumutsaninso, osati chifukwa chochotsa litsiro la mʼthupi koma chifukwa cha chikumbumtima choona pamaso pa Mulungu. Umakupulumutsani chifukwa cha kuuka kwa Yesu Khristu, 22amene anapita kumwamba ndipo ali kudzanja lamanja la Mulungu komwe angelo ndi maulamuliro ndi amphamvu amamvera Iye.

Persian Contemporary Bible

اول پطرس 3:1‏-22

كلامی چند به زنان

1‏-2و اما شما ای زنان، مطيع شوهران خود باشيد تا چنانچه بعضی از ايشان نيز به انجيل ايمان نياورده باشند، با ديدن رفتار شما ايمان بياورند؛ زيرا رفتار خوب و توأم با احترام يک زن، بهتر از سخنان او دربارهٔ مسيح، در دل شوهر اثر می‌گذارد. 3برای زيبايی، به آرايش ظاهری نظير جواهرات و لباسهای زيبا و آرايش گيسوان، توسل نجوييد، 4بلكه بگذاريد باطن و سيرت شما زيبا باشد. باطن خود را با زيبايی پايدار يعنی با روحيهٔ آرام و ملايم زينت دهيد كه مورد پسند خداست. 5اين گونه خصايل، در گذشته در زنان مقدس ديده می‌شد. ايشان به خدا ايمان داشتند و مطيع شوهران خود بودند. 6سارا همسر ابراهيم نيز چنين بود. او از شوهرش اطاعت می‌كرد و به او چون سرپرست خانواده احترام می‌گذاشت. شما نيز اگر دختران آن بانوی بزرگوار باشيد و راه خوب او را در پيش گيريد، ديگر ترس و نگرانی نخواهيد داشت از اينكه ممكن است شوهرانتان از شما برنجند.

كلامی چند به شوهران

7و شما ای شوهران، رفتارتان با همسرانتان بايد با ملاحظه و توأم با احترام باشد، چون ايشان ظريفتر از شما هستند. در ضمن، فراموش نكنيد كه ايشان شريک زندگی روحانی و بركات الهی شما می‌باشند. بنابراين، اگر با ايشان آن گونه كه شايسته است، رفتار نكنيد، دعاهايتان مستجاب نخواهد شد.

كلامی چند به همه مسيحيان

8اين چند كلمه را نيز خطاب به همهٔ شما می‌نويسم: مانند اعضای يک خانواده، نسبت به يكديگر همدرد و مهربان و فروتن باشيد و يكديگر را از صميم قلب دوست بداريد. 9اگر كسی به شما بدی كرد، به او بدی نكنيد، و اگر كسی به شما دشنام داد، به او دشنام ندهيد؛ بلكه برای ايشان دعای خير و بركت كنيد، زيرا ما بايد با ديگران مهربان باشيم؛ آنگاه خدا ما را بركت خواهد داد.

10اگر طالب يک زندگی خوب و خوش می‌باشيد، از سخنان بد و دروغ بپرهيزيد.

11از بدی دوری كنيد و به همه نيكی نماييد. بكوشيد تا با همهٔ مردم در صلح و صفا زندگی كنيد.

12زيرا خداوند نسبت به نيكوكاران نظر لطف دارد و به دعای ايشان گوش می‌دهد، اما از بدكاران روگردان است.

رنج و زحمت به خاطر نيکوکاری

13معمولاً كسی به سبب نيكوكاری خود مورد آزار و اذيت قرار نمی‌گيرد؛ 14اما حتی اگر شما مورد جور و ستم واقع می‌شويد، خوشا به حال شما، زيرا خداوند به شما اجر خواهد داد. پس نگران نباشيد، 15بلكه با خاطری آسوده، خود را به خداوندتان مسيح بسپاريد؛ و اگر كسی علت اين اعتماد و ايمان را جويا شد، حاضر باشيد تا با كمال ادب و احترام به او توضيح دهيد.

16بدون توجه به توهين و بدگويی مردم، آنچه را كه راست و درست است انجام دهيد؛ زيرا وقتی به درستكاری شما پی بردند، از كار خود شرمنده خواهند شد. 17اگر خواست خدا اينست كه زحمت ببينيد، بهتر است برای نيكوكاری رنج و زحمت بكشيد تا برای بدكاری.

18مسيح نيز زحمت ديد. او خود از هر گناهی مبرّا بود، اما يک بار جان خود را در راه ما گناهكاران فدا كرد تا ما را به حضور خدا بياورد. زمانی كه بدن مسيح در قبر گذاشته شد، روح او زنده ماند؛ 19و اين روح او بود كه نزد ارواح محبوس رفت و پيروزی خود را به آنان بشارت داد، 20يعنی به روح كسانی كه در قديم، در زمان نوح، از خدا نافرمانی كرده بودند، گرچه خدا وقتی كه نوح مشغول ساختن كشتی بود، صبورانه منتظر توبهٔ ايشان بود. با اين حال، فقط هشت نفر از آن طوفان وحشتناک نجات پيدا كردند و غرق نشدند. 21اكنون اين طوفان، غسل تعميد را در نظر ما مجسم می‌كند. وقتی تعميد می‌گيريم، نشان می‌دهيم كه بوسيلهٔ زنده شدن مسيح، از مرگ و هلاكت نجات يافته‌ايم. هدف از غسل تعميد، نظافت و شستشوی بدن نيست، بلكه با تعميد يافتن در واقع به سوی خدا باز می‌گرديم و از او می‌خواهيم كه دلهايمان را از گناه پاک سازد. 22اكنون مسيح در آسمان است و در مقامی رفيع، در دست راست خدا نشسته است و تمام فرشتگان و قدرتهای آسمان در برابر او تعظيم می‌كنند و تحت فرمان او می‌باشند.