1 Petro 2 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Petro 2:1-25

1Choncho, lekani zoyipa zonse, chinyengo chilichonse, chiphamaso, nsanje ndi kusinjirira kulikonse. 2Monga makanda obadwa kumene amalirira mkaka, inunso muzilakalaka mkaka weniweni wauzimu, kuti mukule ndi kukufikitsani ku chipulumutso chanu, 3pakuti tsopano mwalawadi kuti Ambuye ndi wabwino.

Mwala wa Moyo ndi Anthu Osankhidwa

4Pamene mukubwera kwa Iye, amene ndi Mwala wa moyo, umene anthu anawukana, koma Mulungu anawusankha kuti ndi wa mtengowapatali, 5inunso, mukhale ngati miyala ya moyo yoti Mulungu amangire nyumba yake yauzimu kuti mukhale ansembe opatulika, opereka nsembe zauzimu zovomerezeka ndi Mulungu mwa Yesu Khristu. 6Pakuti mʼMalemba mwalembedwa kuti,

“Taonani, ndikuyika mwala wa maziko mu Ziyoni,

wosankhika ndi wamtengowapatali.

Amene akhulupirira Iye

sadzachititsidwa manyazi.”

7Tsono kwa inu okhulupirira, mwalawo ndi wamtengowapatali. Koma kwa amene sakhulupirira,

“Mwala umene amisiri anawukana

wasanduka mwala wa maziko,

8ndi

“Mwala wopunthwitsa anthu

ndiponso thanthwe limene limagwetsa anthu.”

Iwo amapunthwa chifukwa samvera uthenga, pakuti ichi ndiye chinali chifuniro cha Mulungu pa iwo.

9Koma inu ndinu anthu osankhidwa ndi Mulungu, ansembe achifumu, mtundu woyera mtima, anthu ake enieni a Mulungu, munasankhidwa kuti mulalikire za ntchito zamphamvu za Iye amene anakuyitanani kuti mutuluke mu mdima ndi kulowa mʼkuwunika kwake kodabwitsa. 10Kale simunali anthu ake, koma tsopano ndinu anthu a Mulungu. Kale simunalandire chifundo, koma tsopano mwalandira chifundo.

11Okondedwa, ndikukupemphani, ngati alendo pansi pano, pewani zilakolako za uchimo, zimene zimachita nkhondo ndi moyo wanu. 12Khalani moyo wabwino pakati pa anthu osapembedza kuti ngakhale atakusinjirirani kuti mumachita zoyipa, iwowo akaona ntchito zanu zabwino, adzalemekeza Mulungu pa tsiku lomwe Iye adzatiyendere.

Kugonjera Olamulira

13Gonjerani maulamuliro onse chifukwa cha Ambuye. Kaya ndi mfumu, imvereni chifukwa ili ndi ulamuliro waukulu, 14kaya ndi mabwanamkubwa, pakuti watumidwa ndi mfumu kuti alange onse amene amachita zoyipa ndi kuyamikira onse amene amachita zabwino. 15Pakuti Mulungu akufuna kuti pochita ntchito zabwino muthetse kuyankhula mosazindikira ndi mopusa. 16Mukhale monga mfulu, koma musagwiritse ntchito ufulu wanuwo ngati chophimbira zoyipa; mukhale monga atumiki a Mulungu. 17Chitirani ulemu aliyense, kondani abale okhulupirira, wopani Mulungu, ndipo chitirani mfumu ulemu.

Akapolo

18Inu akapolo, gonjerani ambuye anu ndi kuwachitira ulemu, osati kwa iwo okha amene ndi abwino ndi omvetsa zinthu, komanso kwa amene ndi ankhanza. 19Pakuti ndi chinthu chokoma ngati munthu apirira mu zowawa zimene sizinamuyenera chifukwa chodziwa kuti Mulungu alipo. 20Kodi pali choti akuyamikireni ngati mupirira pomenyedwa chifukwa choti mwalakwa? Koma ngati mumva zowawa chifukwa chochita zabwino ndi kupirira, mwachita choyamikika pamaso pa Mulungu. 21Munayitanidwa kudzachita zimenezi, chifukwa Khristu anamva zowawa chifukwa cha inu, anakusiyirani chitsanzo, kuti inu mutsatire mʼmapazi ake.

22“Iye sanachite tchimo

kapena kunena bodza.”

23Pamene anthu ankamuchita chipongwe, Iye sanabwezere chipongwe, pamene Iye ankamva zowawa, sanaopseze. Mʼmalo mwake, anadzipereka kwa Mulungu amene amaweruza molungama. 24Iye mwini anasenza machimo athu mʼthupi lake pa mtanda, kuti ife tife kutchimo ndi kukhala ndi moyo potsata chilungamo, ndipo ndi mabala ake munachiritsidwa. 25Pakuti munali monga nkhosa zosochera, koma tsopano mwabwerera kwa mʼbusa ndi woyangʼanira miyoyo yanu.

Persian Contemporary Bible

اول پطرس 2:1-25

1بنابراين، وجود خود را از كينه و دشمنی، فريب و دورويی، حسادت و بدگويی، پاک سازيد. 2‏-3شما كه مهر و محبت خداوند را در زندگی خود چشيده‌ايد، مانند يک كودک نوزاد، مشتاق شير روحانی خالص باشيد، تا با خوردن آن، در نجاتی كه به دست آورده‌ايد، رشد نماييد.

سنگهای زنده برای خانه خدا

4می‌دانيد كه مسيح، آن سنگ زنده‌ای است كه خدا مقرر فرموده تا عمارت روحانی خود را بر آن بنا كند. گرچه انسانها دست رد به سينه او زدند. اما او نزد خدا عزيز و مكرم است. پس به سوی او بياييد، 5تا شما نيز مانند سنگهای زنده در دست خدا، در بنای آن عمارت و عبادتگاه روحانی به کار رويد. مهمتر اينكه شما در اين عبادتگاه، كاهن مقدس نيز می‌باشيد. پس قربانیهای مقبول و مورد پسند خدا را توسط عيسی مسيح تقديم كنيد. 6در كتاب آسمانی آمده است كه خدا مسيح را خواهد فرستاد تا در خانهٔ او، سنگ زاويهٔ گرانبها باشد، و هر كه به او ايمان بياورد، نوميد و پشيمان نشود.

7اين «سنگ» برای شما كه ايمان داريد، بسيار گرانبهاست، اما برای بی‌ايمانان همان سنگی است كه درباره‌اش گفته شده: «سنگی كه معماران دور افكندند، سنگ اصلی ساختمان گرديد.» 8همچنين، در كتاب آسمانی آمده است: «او سنگی است كه پای بعضی به آن می‌خورد و می‌افتند، و تخته سنگی است كه بعضی از آن سقوط می‌كنند.» حقشان است كه بيفتند و سقوط كنند، زيرا از كلام خدا اطاعت نمی‌نمايند.

9اما شما مانند آنان نيستيد. شما برگزيدگان خدا، و كاهنان پادشاهمان عيسی، و قوم مقدس و خاص خدا می‌باشيد، تا به اين ترتيب به ديگران نشان دهيد كه خدا چگونه شما را از تاريكی به نور عجيب خود دعوت نموده است. 10زمانی شما هيچ هويت نداشتيد، اما اكنون فرزندان خدا می‌باشيد؛ زمانی از رحمت و مهربانی خدا بی‌بهره بوديد، اما حال، مورد لطف و رحمت او قرار گرفته‌ايد.

11برادران عزيز، شما در اين دنيا رهگذری بيش نيستيد، و خانهٔ اصلی شما در آسمان است. از این رو، خواهش می‌كنم خود را از لذات گناه‌آلود اين دنيا دور نگاه داريد. شما برای اين قبيل اميال و هوسها ساخته نشده‌ايد؛ به همين دليل است كه آنها با روح و جان شما در جنگ و جدالند. 12مراقب رفتار خود نزد اطرافيان بی‌ايمانتان باشيد؛ چه، در اين صورت، حتی اگر ايشان شما را متهم به بدكاری نمايند، اما در زمان بازگشت مسيح، خدا را به سبب كارهای نيكتان، تمجيد خواهند كرد.

رفتار مسيحی در اجتماع

13‏-14به خاطر خداوند، از مقامات كشور اطاعت نماييد، خواه از رهبر مملكت، و خواه از مأمورين دولت كه از سوی رهبر منصوب شده‌اند تا خلافكاران را مجازات كنند و درستكاران را پاداش دهند.

15خواست خدا اينست كه شما درستكار باشيد تا به اين ترتيب دهان اشخاص نادانی را كه از شما ايراد می‌گيرند ببنديد. 16درست است كه شما از قيد و بند احكام مذهبی آزاد شده‌ايد، اما اين به آن معنی نيست كه می‌توانيد به هر كار نادرستی دست بزنيد، بلكه آزادی خود را بايد برای اجرای خواست خدا به کار ببريد.

17به همه احترام كنيد؛ ايمانداران را دوست بداريد؛ از خدا بترسيد؛ به رهبران مملكت احترام بگذاريد.

سرمشق از مسيح

18شما خدمتكاران، بايد مطيع اربابان خود باشيد و به ايشان احترام كامل بگذاريد، نه فقط به اربابان مهربان و با ملاحظه، بلكه به آنانی نيز كه سختگير و تندخو هستند. 19اگر به خاطر انجام ارادهٔ خدا، به ناحق متحمل رنج و زحمت شويد، خدا شما را اجر خواهد داد. 20اگر به سبب اعمال بد و نادرست مجازات شويد، چه افتخاری دارد؟ اما اگر به سبب درستكاری و نيكوكاری، رنج و زحمت ببينيد و بدون شكايت آن را تحمل نماييد، آنگاه خدا را خشنود ساخته‌ايد.

21اين رنج و زحمت، جزئی از خدمتی است كه خدا به شما محول كرده است. سرمشق شما مسيح است كه در راه شما زحمت كشيد. پس راه او را ادامه دهيد. 22هرگز از او گناهی سر نزد، و دروغی از دهان او بيرون نيامد. 23وقتی به او ناسزا می‌گفتند، پاسخی نمی‌داد؛ و زمانی كه او را عذاب می‌دادند، تهديد به انتقام نمی‌كرد، بلكه زندگی خود را به خدايی واگذار كرد كه داور عادل و با انصاف می‌باشد. 24او بر روی صليب، بار گناهان ما را بر دوش گرفت تا ما بتوانيم از چنگ گناه رهايی يافته، زندگی پاكی داشته باشيم. زخمهای او نيز دوای دردهای ما گرديد. 25شما مانند گوسفندانی بوديد كه راهشان را گم كرده‌اند. اما اكنون نزد شبانتان بازگشته‌ايد، شبانی كه نگهبان جان شماست و شما را از خطرات حفظ می‌كند.