1 Petro 2 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Petro 2:1-25

1Choncho, lekani zoyipa zonse, chinyengo chilichonse, chiphamaso, nsanje ndi kusinjirira kulikonse. 2Monga makanda obadwa kumene amalirira mkaka, inunso muzilakalaka mkaka weniweni wauzimu, kuti mukule ndi kukufikitsani ku chipulumutso chanu, 3pakuti tsopano mwalawadi kuti Ambuye ndi wabwino.

Mwala wa Moyo ndi Anthu Osankhidwa

4Pamene mukubwera kwa Iye, amene ndi Mwala wa moyo, umene anthu anawukana, koma Mulungu anawusankha kuti ndi wa mtengowapatali, 5inunso, mukhale ngati miyala ya moyo yoti Mulungu amangire nyumba yake yauzimu kuti mukhale ansembe opatulika, opereka nsembe zauzimu zovomerezeka ndi Mulungu mwa Yesu Khristu. 6Pakuti mʼMalemba mwalembedwa kuti,

“Taonani, ndikuyika mwala wa maziko mu Ziyoni,

wosankhika ndi wamtengowapatali.

Amene akhulupirira Iye

sadzachititsidwa manyazi.”

7Tsono kwa inu okhulupirira, mwalawo ndi wamtengowapatali. Koma kwa amene sakhulupirira,

“Mwala umene amisiri anawukana

wasanduka mwala wa maziko,

8ndi

“Mwala wopunthwitsa anthu

ndiponso thanthwe limene limagwetsa anthu.”

Iwo amapunthwa chifukwa samvera uthenga, pakuti ichi ndiye chinali chifuniro cha Mulungu pa iwo.

9Koma inu ndinu anthu osankhidwa ndi Mulungu, ansembe achifumu, mtundu woyera mtima, anthu ake enieni a Mulungu, munasankhidwa kuti mulalikire za ntchito zamphamvu za Iye amene anakuyitanani kuti mutuluke mu mdima ndi kulowa mʼkuwunika kwake kodabwitsa. 10Kale simunali anthu ake, koma tsopano ndinu anthu a Mulungu. Kale simunalandire chifundo, koma tsopano mwalandira chifundo.

11Okondedwa, ndikukupemphani, ngati alendo pansi pano, pewani zilakolako za uchimo, zimene zimachita nkhondo ndi moyo wanu. 12Khalani moyo wabwino pakati pa anthu osapembedza kuti ngakhale atakusinjirirani kuti mumachita zoyipa, iwowo akaona ntchito zanu zabwino, adzalemekeza Mulungu pa tsiku lomwe Iye adzatiyendere.

Kugonjera Olamulira

13Gonjerani maulamuliro onse chifukwa cha Ambuye. Kaya ndi mfumu, imvereni chifukwa ili ndi ulamuliro waukulu, 14kaya ndi mabwanamkubwa, pakuti watumidwa ndi mfumu kuti alange onse amene amachita zoyipa ndi kuyamikira onse amene amachita zabwino. 15Pakuti Mulungu akufuna kuti pochita ntchito zabwino muthetse kuyankhula mosazindikira ndi mopusa. 16Mukhale monga mfulu, koma musagwiritse ntchito ufulu wanuwo ngati chophimbira zoyipa; mukhale monga atumiki a Mulungu. 17Chitirani ulemu aliyense, kondani abale okhulupirira, wopani Mulungu, ndipo chitirani mfumu ulemu.

Akapolo

18Inu akapolo, gonjerani ambuye anu ndi kuwachitira ulemu, osati kwa iwo okha amene ndi abwino ndi omvetsa zinthu, komanso kwa amene ndi ankhanza. 19Pakuti ndi chinthu chokoma ngati munthu apirira mu zowawa zimene sizinamuyenera chifukwa chodziwa kuti Mulungu alipo. 20Kodi pali choti akuyamikireni ngati mupirira pomenyedwa chifukwa choti mwalakwa? Koma ngati mumva zowawa chifukwa chochita zabwino ndi kupirira, mwachita choyamikika pamaso pa Mulungu. 21Munayitanidwa kudzachita zimenezi, chifukwa Khristu anamva zowawa chifukwa cha inu, anakusiyirani chitsanzo, kuti inu mutsatire mʼmapazi ake.

22“Iye sanachite tchimo

kapena kunena bodza.”

23Pamene anthu ankamuchita chipongwe, Iye sanabwezere chipongwe, pamene Iye ankamva zowawa, sanaopseze. Mʼmalo mwake, anadzipereka kwa Mulungu amene amaweruza molungama. 24Iye mwini anasenza machimo athu mʼthupi lake pa mtanda, kuti ife tife kutchimo ndi kukhala ndi moyo potsata chilungamo, ndipo ndi mabala ake munachiritsidwa. 25Pakuti munali monga nkhosa zosochera, koma tsopano mwabwerera kwa mʼbusa ndi woyangʼanira miyoyo yanu.

Habrit Hakhadasha/Haderekh

אגרתו הראשונה של פטרוס השליח 2:1-25

1לפיכך, הפסיקו לעשות מעשים רעים! אל תרמו, אל תקנאו, אל תרכלו ואל תוציאו דיבה. 2‏-3אכן, אם אתם באמת מעריכים את טוב־לבו של האדון, חדלו לכם מהרשע, וכתינוקות רכים המשתוקקים לחלב אמם השתוקקו לחלב רוחני טהור, שיעזור לכם לגדול ולהגיע לבגרות רוחנית ולישועה מושלמת.

4בואו אל המשיח שהוא אבן־פינה חיה! בני־האדם זלזלו בו, אך לאלוהים שבחר בו להיות מעל הכול, יקר המשיח מכל!

5עתה נעשיתם אבנים חיות, ואלוהים בונה בכם את משכנו הרוחני. במשכנו זה אתם כוהניו הקדושים, ובשם ישוע המשיח עליכם להקריב לו זבחים שימצאו־חן בעיניו. 6בקשר לכך אומר לנו אלוהים בכתבי־הקודש:2‏.6 ב 6 ישעיהו כח 16

”הנני יוסד בציון אבן פינה,

אבן בוחן ויקרה,

המאמין בה לא יבוש“.2‏.6 ב 6 כלשונו: הנני יסד בציון אבן, אבן בוחן פינת יקרת מוסד, המאמין לא יחיש.

7לכם, המאמינים, אבן זאת יקרה מאוד, אך לאלה שאינם מאמינים:

”האבן שמאסו הבונים

הייתה לראש פינה, 2‏.7 ב 7 תהלים קיח 22

8לאבן נגף וצור מכשול“.2‏.8 ב 8 ישעיהו ח 14

אכן, אלה שאינם מאמינים ייכשלו, שכן לא יקשיבו לדבר אלוהים, וכך יקבלו את העונש שמיועד להם.

9אולם אתם שונים מהם; אתם נבחרתם על־ידי אלוהים עצמו לממלכת כוהנים, לעם קדוש ומיוחד, כדי שתראו לבני־האדם כיצד הוציאכם אלוהים מהחשכה והביאכם אל אורו הנפלא. 10בעבר התכחש אלוהים אליכם, אך עתה עם אלוהים אתם! בעבר לא הכרתם את טוב לבו של אלוהים; עתה טוב־לבו זה שינה את חייכם לחלוטין.

11אחים יקרים ואהובים, אני מתחנן לפניכם, אנא, התנהגו בעולם הזה כזרים, מעין תושבים ארעיים, ואל תיכנעו לפיתויי העולם הזה שמתגרים בנפשותיכם.

12הקפידו על התנהגות טובה עם שכניכם הלא־מאמינים. התנהגו איתם בצדק וביושר כדי שיראו את מעשיכם הטובים, וכך, למרות חשדותיהם הנוכחיים, בבוא המשיח הם יפארו את שמו על־שום מעשיכם הטובים.

13היכנעו לכל שלטון אנושי למען אדוננו, בין אם למלך כראש המדינה, 14ובין אם לנציגים אשר שלח להעניש את עושי הרע ולשבח את עושי הטוב. 15אלוהים רוצה שתעשו אך ורק את הטוב, כדי שמעשיכם הטובים ישתיקו את הלא־מאמינים אשר, מתוך טיפשות וחוסר דעת, מחפשים סיבה לדבר נגדכם ונגד הבשורה. 16אתם אמנם חופשיים, אך הנכם עבדים לאלוהים, אז אל תנצלו את היותכם חופשיים כתירוץ לעשות את הרע. 17כבדו את כל בני האדם; אהבו את המאמינים, כבדו את השלטונות, והתייחסו ביראה אל אלוהים.

18עבדים, כבדו את אדוניכם, ועשו כל מה שיאמרו לכם – לא רק אם הם טובי־לב וענווים, אלא גם אם הם קפדנים ואכזרים. 19אם אתם נענשים חינם על מעשה טוב שעשיתם, הללו את אלוהים! 20אחרי הכול, אם נענשתם על מעשה רע שעשיתם, לא מגיע לכם פרס; אך אם אתם נענשים וסובלים בגלל מעשיכם הטובים, מוצא הדבר חן בעיני אלוהים.

21אלוהים יעד לכם סבל זה, שהרי גם המשיח סבל למענכם והשאיר לכם דוגמה ללכת בעקבותיו. 22המשיח לא חטא מעולם, לא רימה, 23לא השיב למקללים אותו ולא איים לנקום במעניו; הוא הפקיד את עצמו בידי האלוהים ששופט בצדק. 24המשיח נשא בגופו את חטאינו, כדי שנמות לגבי החטא ונחיה כדי לעשות מעשי צדקה. הכאב והסבל שנשא המשיח ריפאו אותנו! 25בעבר טעיתם כצאן ההולכות לאיבוד, אך עתה שבתם אל הרועה הטוב ששומר על נפשותיכם.