Yakobo 1 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yakobo 1:1-27

1Yakobo, mtumiki wa Mulungu ndi wa Ambuye Yesu Khristu,

kulembera mafuko khumi ndi awiri obalalikana ku mayiko osiyanasiyana.

Landirani moni.

Masautso ndi Mayesero

2Abale, muchiyese ngati chimwemwe chenicheni nthawi zonse pamene mukukumana ndi mayesero amitundumitundu. 3Inu mukudziwa kuti kuyesedwa kwa chikhulupiriro chanu kumabweretsa chipiriro. 4Chipiriro chiyenera kugwira ntchito yake kuti mukhale okhwima ndi angwiro, osasowa kanthu kalikonse. 5Ngati wina pakati panu akusowa nzeru, apemphe kwa Mulungu amene amapereka kwa onse mwaulere ndi mosatonzera, ndipo adzapatsidwa. 6Koma pamene mupempha, muyenera kukhulupirira osakayika, chifukwa amene amakayika ali ngati mafunde pa nyanja amene amawinduka nakankhika ndi mphepo. 7Munthu wotere asayembekezere kulandira kalikonse kuchokera kwa Ambuye. 8Iyeyu ndi munthu wa mitima iwiri, wosakhazikika pa zimene akuchita.

9Abale omwe ndi anthu wamba anyadire pamene akwezedwa. 10Koma olemera anyadire pamene atsitsidwa, chifukwa adzatha ngati duwa lakuthengo. 11Pakuti dzuwa limatuluka nʼkutentha kwake, ndipo limafotetsa zomera. Duwa lake limathothoka ndipo kukongola kwake kumatheratu. Momwemonso munthu wachuma adzazimirira ngakhale atamachitabe malonda ake.

12Wodala ndi munthu amene amapirira mʼmayesero, chifukwa akapambana adzalandira chipewa cha ulemerero chimene Mulungu analonjeza anthu amene amamukonda.

13Munthu akayesedwa asanene kuti, “Mulungu akundiyesa.” Pakuti Mulungu sangayesedwe ndi choyipa kapena Iyeyo kuyesa munthu aliyense. 14Koma munthu aliyense amayesedwa akakokedwa ndi zilakolako zake zoyipa ndi kukopedwa nazo. 15Pamenepo, chilakolako chikakula chimabala tchimo; ndipo tchimo likakhwima limabereka imfa.

16Musanyengedwe abale anga okondedwa. 17Mphatso iliyonse yabwino ndi yangwiro imachokera kumwamba, kwa Atate mwini kuwala, amene sasintha ngati mthunzi woyendayenda. 18Iye anasankha kutibereka ife kudzera mʼmawu a choonadi, kuti pakati pa zolengedwa zake zonse, tikakhale ngati zipatso zoyamba.

Kumva ndi Kuchita

19Abale anga okondedwa, gwiritsitsani mawu awa: munthu aliyense azifulumira kumva, koma asamafulumire kuyankhula, ndipo asamafulumirenso kupsa mtima. 20Pakuti mkwiyo wa munthu subweretsa chilungamo chimene amafuna Mulungu. 21Choncho chotsani chizolowezi choyipa ndi khalidwe loyipa pakati panu, ndipo modzichepetsa landirani mawu amene anadzalidwa mwa inu, amene akhoza kukupulumutsani.

22Musamangomvetsera chabe mawu, ndi kumadzinyenga nokha. Chitani zimene mawuwo amanena. 23Munthu aliyense amene amangomva mawu koma osachita zimene mawuwo amanena, ali ngati munthu amene amayangʼana nkhope yake pa galasi. 24Akadziyangʼana amachoka, nthawi yomweyo nʼkuyiwala mmene akuonekera. 25Koma munthu amene amayangʼana mwachidwi lamulo langwiro limene limapatsa ufulu ndi kupitiriza kutero, osayiwala chimene wamva koma kuchita adzadalitsika pa zimene amachita.

26Ngati wina amadziyesa ngati ndi wachipembedzo, koma chonsecho saletsa lilime lake, amadzinyenga yekha ndipo chipembedzo chakecho ndi cha chabechabe. 27Chipembedzo chimene Mulungu Atate athu amachivomereza kuti ndi changwiro ndi chopanda zolakwika ndi ichi: kusamalira ana amasiye ndi akazi amasiye pa mavuto awo, ndi kudzisunga bwino kuopa kudetsedwa ndi dziko lapansi.

Habrit Hakhadasha/Haderekh

אגרת יעקב 1:1-27

1אל שנים עשר השבטים שפזורים בתפוצות.

מאת יעקב, עבדו של אלוהים ושל ישוע המשיח.

שלום וברכה לכולכם!

2אחים יקרים, אם יש לכם צרות ובעיות, ואם אתם עומדים בפני פיתויים חזקים, תחשיבו זאת כהזדמנות לשמחה גדולה. 3שכן צרות, בעיות ופיתויים מחזקים את כוח הסבל. 4לכן אל תברחו מהבעיות, אלא תנו לסבלנותכם להתחזק. כאשר תהיה סבלנותכם חזקה די הצורך, לא יחסר לכם דבר, אופייכם יהיה חזק מן הרגיל ותהיו מסוגלים לכל דבר.

5ברצונכם לדעת מה רוצה האלוהים שתעשו? שאלו אותו והוא יגיד לכם ברצון. ה׳ מוכן תמיד להעניק חכמה באהבה וברוחב לב למי שמבקש ממנו, בלי לגעור בו על שביקש. 6אך עליכם להאמין, ללא צל של ספק, שהוא באמת ייתן לכם מה שאתם מבקשים ממנו, כי אדם ספקן וחסר־אמונה דומה לגל בים הנישא וניזרק על־ידי הרוח. 7‏-8אדם ספקן הוא אדם הפכפך שמשנה את דעתו בכל רגע, שכן אינו בטוח בהחלטותיו. אם אינכם מבקשים באמונה, אל תצפו מה׳ להיענות לכם.

9מאמין משיחי הנחשב לעני בעולם הזה צריך לשמוח, כי בעיני אלוהים הוא חשוב מאוד, 10‏-11והמאמין העשיר צריך לשמוח על שעושרו חסר כל ערך בעיני ה׳. כי כמו הפרח שמאבד את יופיו, מתייבש בקרני השמש הצורבות וָמֶת, כך ימותו העשירים תוך זמן קצר וישאירו אחריהם את כל רכושם.

12טוב לאדם שעומד בפיתויים ולא נכשל, כי הוא יקבל פרס – את כתר החיים שהבטיח ה׳ לכל האוהבים אותו. 13זכרו, אלוהים אף פעם אינו מנסה לפתותכם לעשות מעשים רעים, כי אלוהים עצמו שונא את הרע.

לכן, אם אתם עומדים לפני פיתויים שונים, אל תאשימו את אלוהים! 14מקור הפיתויים הוא בלב האדם, בתשוקותיו ובמחשבותיו הרעות.

15המחשבות האלה מולידות מעשים רעים. כאשר נותנים לחטא לצמוח, זה מוליד מוות.

16לכן, אחים יקרים, אל תטעו בשום פנים.

17כל המתנות הטובות והמושלמות ניתנות לנו מהאלוהים אשר ברא את כל האורות, ואשר בעצמו מקרין אור נפלא שאינו משתנה ואינו נחלש לעולם. 18אלוהים בחר מרצונו החופשי לתת לנו חיים חדשים, באמצעות האמת שבכתבי־הקודש, וכך הפכנו להיות הילדים הראשונים במשפחתו החדשה.

19זכרו, אחים יקרים, כולם צריכים להיות מהירים להקשיב, אך איטיים לדבר ואיטיים להתרגז, 20כי הרוגז מכער אותנו ואת אופיינו, ואילו ה׳ רוצה שנהיה טובים ומושלמים. 21על כן היפטרו מכל דבר רע בחייכם, מבפנים ומבחוץ, וקבלו בשמחה ובענווה את דבר אלוהים אשר בכוחו להושיענו.

22עליכם לבצע את דבר אלוהים הלכה למעשה, כי אם אתם מקשיבים ואינכם מקיימים, אתם מרמים את עצמכם. 23מי שמקשיב בלבד ואינו מקיים את אשר שמע, דומה לאדם שמביט בדמותו במראה; 24ברגע שהוא מפנה את גבו למראה, שוב אינו יכול לראות את בבואתו ושוכח כיצד הוא נראה. 25אך החוקר והלומד את תורת החופש שנתן ה׳ לבני אדם, לא זו בלבד שיזכור את הכתוב, הוא גם יבצע אותו הלכה למעשה, ואלוהים יברכו בכל מעשיו.

26הטוען שהוא מאמין משיחי, אך אינו מסוגל לשלוט בלשונו, מרמה את עצמו, ואמונתו אינה שווה הרבה. 27אמונה טהורה ואמיתית בעיני אלוהים האב פירושה לדאוג לאלמנות וליתומים בצרתם, ולסרב להשפעה המטמאת של העולם.