1 Petro 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Petro 1:1-25

1Ndine Petro, mtumwi wa Yesu Khristu.

Ndikulemba kalatayi kwa onse osankhidwa ndi Mulungu, alendo mʼdziko lapansi, obalalikira ku Ponto, Galatiya, Kapadokiya, Asiya ndi Bituniya. 2Mulungu Atate anakusankhani, atakudziwani kuyambira pachiyambi, ndipo Mzimu Woyera wakuyeretsani kuti mumvere Yesu Khristu ndikutsukidwa ndi magazi ake.

Chisomo ndi mtendere zikhale ndi inu mochuluka.

Kuyamika Mulungu Chifukwa cha Chiyembekezo Chamoyo

3Alemekezedwe Mulungu, Atate wa Ambuye athu Yesu Khristu. Mwachifundo chake chachikulu anatibadwitsa kwatsopano, mʼchiyembekezo chamoyo pomuukitsa Yesu Khristu kwa akufa, 4kuti tidzalandire chuma chomwe sichingawonongeke, kuyipitsidwa kapena kufota. Chuma chimenechi akukusungirani kumwamba. 5Mwachikhulupiriro, mukusungidwa ndi mphamvu ya Mulungu mpaka chipulumutso chitafika chimene chinakonzedwa kuti adzachionetse nthawi yotsiriza. 6Zimenezi zikukondweretseni kwambiri, ngakhale tsopano, kwa kanthawi kochepa, mukumva zowawa mʼmayesero osiyanasiyana. 7Mayeserowa abwera nʼcholinga chakuti chikhulupiriro chanu, chimene ndi chamtengo woposa wa golide, amene amawonongeka ngakhale amayengedwa ndi moto, chitsimikizike kuti ndi chenicheni. Pamenepo ndiye mudzalandire mayamiko, ulemerero ndi ulemu pamene Yesu Khristu adzaoneka. 8Ngakhale kuti simunamuone, mumamukonda; ndipo ngakhale kuti simukumuona tsopano, mumamukhulupirira ndipo mumakondwera ndi chimwemwe chachikulu ndi chosaneneka. 9Motero mukulandira mphotho ya chikhulupiriro chanu, ndiyo chipulumutso cha moyo wanu.

10Kunena za chipulumutso chimenechi, aneneri amene ananeneratu za chisomo chimene chimabwera kwa inu, anafunafuna mofufuzafufuza za chipulumutsochi, 11kufuna kudziwa nthawi ndi momwe zidzachitikire zinthu zimene Mzimu wa Khristu amene ali mwa iwo ankanenera za kuvutika kwa Khristu, ndi ulemerero umene adzakhale nawo pambuyo pake. 12Mulungu anawawululira kuti ntchito yawoyo sankayigwira chifukwa cha iwo eni, koma chifukwa inu, pamene iwo ankayankhula zinthu zimene mwamva tsopano kuchokera kwa amene amalalikira Uthenga Wabwino mwamphamvu ya Mzimu Woyera wotumidwa kuchokera kumwamba. Ngakhale angelo amalakalaka kuona nawo zinthuzi.

Khalani Oyera Mtima

13Choncho konzani mtima wanu, khalani odziretsa; khazikitsani chiyembekezo chanu kotheratu pa chisomo chimene mudzapatsidwe pamene Yesu Khristu adzaonekera. 14Monga ana omvera, musatsatenso zilakolako zoyipa zomwe munali nazo pamene munali osadziwa. 15Koma monga amene anakuyitanani ndi woyera, inunso khalani oyera mtima mʼmakhalidwe anu wonse. 16Pakuti, kwalembedwa kuti, “Khalani oyera mtima, chifukwa Ine ndine Woyera.”

17Popeza mumapemphera kwa Atate amene amaweruza munthu aliyense mopanda tsankho molingana ndi zochita zake, pa nthawi imene muli alendo pa dziko lapansi khalani moopa Mulungu. 18Pakuti mukudziwa kuti simunawomboledwe ndi zinthu zimene zimawonongeka monga siliva kapena golide, kuchoka ku khalidwe lanu lachabe limene munalandira kwa makolo anu. 19Koma munawomboledwa ndi magazi a mtengowapatali a Khristu, Mwana Wankhosa wopanda banga kapena chilema. 20Iye anasankhidwa lisanalengedwe dziko lapansi, koma waonetsedwa chifukwa cha inu pa nthawi ino yotsiriza. 21Kudzera mwa Iye mumakhulupirira Mulungu, amene anamuukitsa kwa akufa namupatsa ulemerero. Nʼchifukwa chake chikhulupiriro ndi chiyembekezo chanu chili mwa Mulungu.

22Tsopano mwayeretsa mitima yanu pomvera choonadi, kuti muzikondana ndi abale anu, kukondana kwenikweni kochokera pansi pa mtima. 23Popeza mwabadwanso, osati ndi mbewu imene imawonongeka, koma imene siwonongeka, ndiye kuti ndi Mawu a Mulungu amoyo ndi okhalitsa. 24Pakuti,

“Anthu onse ali ngati udzu,

ndipo ulemerero wawo uli ngati duwa la kuthengo.

Udzu umafota ndipo duwa limathothoka,

25koma mawu a Ambuye adzakhala mpaka muyaya.”

Ndipo awa ndi mawu amene tinalalikira kwa inu.

New Russian Translation

1 Петра 1:1-25

Приветствие

1От Петра, апостола Иисуса Христа.

Скитальцам, рассеянным в Понте, Галатии, Каппадокии, провинции Азия1:1 Азия – здесь имеется в виду не материк, а римская провинция на западе Малой Азии (часть современной территории Турции), которая позднее дала свое название материку. и Вифинии, избранным 2по предведению Бога Отца, через освящение Духом, для повиновения Иисусу Христу и окропления Его кровью.

Благодать вам и мир да преумножатся.

Благодарность Богу за живую надежду

3Благословен Бог и Отец нашего Господа Иисуса Христа. По Своей великой милости Он через воскресение Иисуса Христа из мертвых дал нам новую жизнь в живой надежде. 4Он дал нам нетленное, неоскверненное и неувядаемое наследие. Оно хранится на небесах для вас, 5защищенных через веру Божьей силой для спасения, которое готово явиться в последнее время.

6Поэтому радуйтесь, даже если сейчас какое-то время вам и приходится страдать в различных испытаниях. 7Ведь через такие страдания доказывается подлинность вашей веры, что ценнее золота (которое хоть и испытывается огнем, но все равно не вечно), чтобы она принесла вам похвалу, славу и честь, когда явится Иисус Христос. 8Вы не видели Его, но уже любите Его, и сейчас, не видя Его, вы верите в Него и радуетесь неописуемой и славной радостью, 9достигая цели вашей веры – спасения душ ваших.

10Этому спасению были посвящены поиски и исследования пророков, которые пророчествовали об ожидающей вас благодати. 11Они старались понять, на какое время и на Кого им указывал находившийся в них Дух Христа, заранее свидетельствовавший о предназначенных Христу страданиях и о последующей за ними славе. 12Им было открыто, что они служили не для себя, а для вас, когда возвещали то, что ныне, в силе посланного с небес Святого Духа, проповедано вам теми, кто принес Радостную Весть, то, во что даже ангелы жаждут заглянуть.

Будьте святы

13Поэтому приготовьте свой ум к действию. Храните самообладание, полностью надейтесь на благодать, которая будет вам дана, когда явится Иисус Христос. 14Как послушные дети не позволяйте управлять собой желаниям, жившим в вас, когда вы еще пребывали в неведении. 15Но будьте святы во всем, что бы вы ни делали, как свят Тот, Кто призвал вас, 16так как написано: «Будьте святы, потому что Я свят»1:16 См. Лев. 11:44, 45; 19:2; 20:7..

17Если вы называете Отцом Того, Кто беспристрастно судит каждого по делам, то, будучи странниками на этой земле, проводите вашу жизнь в почтительном страхе перед Ним. 18Ведь вы знаете, что не такими тленными вещами, как серебро или золото, вы были выкуплены от бессмысленной жизни, переданной вам по наследству предками, 19но драгоценной кровью Христа, как чистого и непорочного ягненка. 20Он был предопределен еще до создания мира, но ради вас был явлен в конце времен. 21Через Него вы и верите в Бога, воскресившего Его из мертвых и прославившего Его, чтобы вы имели веру и надежду на Бога.

22Послушанием истине вы очистили ваши души для того, чтобы искренне любить своих братьев. Итак, глубоко любите друг друга от чистого сердца! 23Вы были заново рождены не от тленного семени, а от нетленного, живого и вечнопребывающего Божьего слова, 24потому что

«все люди1:24 Букв.: «всякая плоть». – как трава,

и вся их1:24 Букв.: «ее». слава – как полевые цветы.

Трава засыхает, и цветы опадают,

25но слово Господа пребывает вовек»1:24-25 См. Ис. 40:6-8..

Это и есть слово возвещаемой вам Радостной Вести.