1 Mbiri 14 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 14:1-17

Nyumba ya Davide ndi Banja Lake

1Hiramu mfumu ya ku Turo inatumiza amithenga kwa Davide pamodzi ndi mitengo ya mkungudza ndiponso amisiri a miyala ndi amisiri a matabwa kuti adzamumangire nyumba yaufumu. 2Choncho Davide anazindikira kuti Yehova wamukhazikitsa kukhala mfumu ya Israeli ndipo wakuza kwambiri ufumu wake chifukwa cha anthu ake, Aisraeli.

3Davide anakwatira akazi ena ambiri ku Yerusalemu ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri. 4Mayina a ana amene anaberekera ku Yerusalemu anali awa: Samua, Sobabu, Natani, Solomoni, 5Ibihari, Elisua, Elipeleti, 6Noga, Nefegi, Yafiya, 7Elisama, Beeliada ndi Elifeleti.

Davide Agonjetsa Afilisti

8Afilisti atamva kuti Davide wadzozedwa kukhala mfumu ya dziko lonse la Israeli, iwo anapita mwamphamvu kukamusakasaka. Koma Davide atamva zimenezi anapita kukakumana nawo. 9Ndipo Afilisti anabwera ndi kulanda zinthu mʼChigwa cha Refaimu. 10Davide anafunsa Mulungu kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?”

Yehova anamuyankha kuti, “Pita, Ine ndidzawapereka mʼmanja mwako.”

11Choncho Davide ndi anthu ake anapita ku Baala-Perazimu ndi kugonjetsa Afilistiwo. Iye anati, “Monga amasefukira madzi, Mulungu waphwanya adani anga ine ndikuona.” Motero anawatcha malowa Baala Perazimu. 12Afilisti anasiya milungu yawo kumeneko ndipo Davide analamulira kuti itenthedwe ndi moto.

13Nthawi inanso Afilisti anadzalanda katundu mu Chigwamo. 14Choncho Davide anafunsa Mulungu ndipo Mulunguyo anayankha kuti, “Usapite molunjika, koma uzungulire kumbuyo kwawo. Ukawathire nkhondo patsogolo pa mitengo ya mkandankhuku. 15Mukakangomva phokoso pa msonga za mitengo ya mkandankhuku, mukapite kukamenyana nawo, chifukwa izi zikasonyeza kuti Mulungu ali patsogolo panu kukantha ankhondo a Afilisti.” 16Kotero Davide anachita zimene Mulungu anamulamulira ndipo anakantha ankhondo a Afilisti njira yonse kuchokera ku Gibiyoni mpaka ku Gezeri.

17Choncho mbiri ya Davide inafalikira dziko lonse, ndipo Yehova anachititsa kuti mayiko ena azimuopa.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

歷代志上 14:1-17

大衛的宮殿和家人

1泰爾希蘭差遣使者帶著香柏木、木匠和石匠去為大衛建造宮殿。 2那時,大衛知道耶和華已立他做以色列的王,並因自己以色列子民的緣故而使他國家興旺。

3大衛耶路撒冷又娶了多位妻子,生了許多兒女。 4他在耶路撒冷所生的孩子有沙姆亞朔罷拿單所羅門5益轄以利書亞以法列6挪迦尼斐雅非亞7以利沙瑪比利雅大以利法列

打敗非利士人

8非利士人聽說大衛已被膏立為以色列王,就全軍出動搜尋大衛大衛得知後,便出來迎敵。 9非利士人前來襲擊利乏音谷。 10大衛就求問上帝說:「我可以去迎戰非利士人嗎?你會把他們交在我手裡嗎?」耶和華說:「去吧,我必把他們交在你手裡。」

11於是,大衛前往巴力·毗拉心,擊敗了非利士人。他說:「上帝藉我的手擊潰敵人,如洪水沖垮堤岸。」所以,那地方叫巴力·毗拉心14·11 巴力·毗拉心」意思是「沖垮之主」。12非利士人在那裡丟棄了他們的神像,大衛命人把它們燒掉。 13非利士人又來襲擊那山谷, 14大衛又求問上帝,上帝對他說:「你不要正面出擊,要繞到他們後面,從桑林對面攻打他們。 15當你聽見桑樹梢上響起腳步聲時,就要進攻,因為那表示耶和華已在你前頭去攻擊非利士的軍隊了。」 16大衛遵命而行,打敗非利士人,從基遍一直殺到基色17於是,大衛名揚列國,耶和華使列國都懼怕他。