1 Akorinto 3 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Akorinto 3:1-23

Mpingo ndi Atsogoleri Ake

1Ndipo abale sindikanakuyankhulani ngati auzimu koma adziko lapansi, makanda chabe mwa Khristu. 2Ndinakupatsani mkaka osati chakudya cholimba pakuti munali musanakonzeke kuchilandira. Zoonadi, simunakonzekebe. 3Mukanali adziko lapansi. Pakuti pakati panu pali kaduka ndi kukangana, kodi si inu a dziko lapansi? Kodi simukuchita ngati anthu wamba? 4Pamene wina anena kuti, “Ine ndimatsatira Paulo,” ndipo wina akuti, “Ine ndimatsatira Apolo,” Kodi si inu akunja?

5Ndiponso kodi Apolo ndi ndani? Nanga Paulo ndi ndani? Otumikira chabe, omwe kudzera mwa iwo inu munakhulupirira monga Ambuye anawagawira aliyense ntchito yake. 6Ine ndinadzala mbewu, Apolo anayithirira, koma Mulungu ndiye anayikulitsa. 7Choncho kuphatikiza iye wodzala ndi iye wothirira, onse sali kanthu, koma Mulungu yekha amene amakulitsa zinthu. 8Munthu wodzala ndi munthu wothirira ali ndi cholinga chimodzi, ndipo aliyense adzapatsidwa mphotho molingana ndi ntchito yake. 9Pakuti ife ndife antchito anzake a Mulungu; inu ndinu munda wa Mulungu, Nyumba ya Mulungu.

10Mwachisomo chimene Mulungu wandipatsa, ine ndinayika maziko monga mmisiri waluntha, ndipo ena akumangapo. Koma aliyense ayenera kuchenjera mmene akumangira. 11Pakuti wina sangayikenso maziko ena oposera amene anakhazikitsidwa kale, amene ndi Yesu Khristu. 12Ngati munthu aliyense amanga pa maziko awa pogwiritsa ntchito golide, siliva, miyala yamtengowapatali, milimo yamitengo, tsekera kapena udzu, 13ntchito yake idzaonekera pamene Tsiku la chiweruzo lidzazionetsa poyera. Tsikulo lidzafika ndi moto, ndipo motowo ndi umene udzayesa ntchito ya munthu aliyense. 14Ngati zimene zamangidwazo sizidzagwa, adzalandira mphotho yake. 15Ndipo ngati zidzanyeke ndi moto, sadzalandira mphotho koma iye mwini adzapulumukabe, koma monga ngati munthu amene wapulumuka mʼmoto.

16Kodi inu simukudziwa kuti ndinu Nyumba ya Mulungu ndipo kuti Mzimu wa Mulungu amakhala mwa inu? 17Ngati wina aliyense awononga Nyumba ya Mulunguyo, Mulungu nayenso adzamuwononga ameneyo; popeza Nyumba ya Mulungu ndi yopatulika ndipo Nyumbayo ndi inu amene.

18Choncho musadzinyenge. Ngati wina wa inu akuganiza kuti ndi wanzeru pa mulingo wa mʼbado uno, ayenera kukhala “wopusa” kuti athe kukhala wanzeru. 19Pakuti nzeru ya dziko lapansi ndi yopusa pamaso pa Mulungu. Monga kwalembedwera kuti, “Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,” 20ndiponso, “Ambuye amadziwa kuti maganizo a wanzeru ndi opandapake.” 21Choncho, wina asanyadire anthu chabe! Zonse ndi zanu, 22kaya Paulo kapena Apolo kapena Kefa kapena dziko lapansi, kapena moyo, kapena imfa, kapena tsopano, kapena mʼtsogolo, zonse ndi zanu, 23ndipo inu ndinu a Khristu, ndipo Khristu ndi wa Mulungu.

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

1 Wakorintho 3:1-23

Kuhusu Mgawanyiko Katika Kanisa

13:1 1Kor 2:15; Rum 7:14; 1Kor 2:14; 14:20Ndugu zangu, mimi sikuweza kusema nanyi kama watu wa kiroho, bali kama watu wa mwilini, kama watoto wachanga katika Kristo. 23:2 Ebr 5:12-14; 1Pet 2:2; Yn 16:12Naliwanywesha maziwa, wala si chakula kigumu, kwa kuwa hamkuwa tayari kwa hicho chakula. Naam, hata sasa hamko tayari. 33:3 Rum 13:13; 1Kor 1:11; Gal 5:20Ninyi bado ni watu wa mwilini. Kwa kuwa bado kuna wivu na magombano miongoni mwenu, je, ninyi si watu wa mwilini? Je, si mwaendelea kama watu wa kawaida? 43:4 1Kor 1:12Kwa maana mmoja anaposema, “Mimi ni wa Paulo,” na mwingine, “Mimi ni wa Apolo,” je, ninyi si wanadamu wa kawaida?

53:5 Mdo 18:24; 1Kor 4:1; 2Kor 6:4; Efe 3:7; Kol 1:23-25Kwani, Apolo ni nani? Naye Paulo ni nani? Ni watumishi tu ambao kupitia wao mliamini, kama vile Bwana alivyompa kila mtu huduma yake. 63:6 Mdo 18:4-11; 1Kor 4:15; 9:1; 15:1Mimi nilipanda mbegu, Apolo akatia maji, lakini Mungu ndiye aliikuza. 73:7 2Kor 12:11; Gal 6:3Hivyo mwenye kupanda na mwenye kutia maji si kitu, bali Mungu peke yake ambaye huifanya ikue. 83:8 Za 18:20; 62:12; Mt 25:21; 1Kor 9:17Apandaye mbegu ana lengo sawa na yule atiaye maji na kila mmoja atalipwa kulingana na kazi yake. 93:9 Mk 16:20; 2Kor 6:1; 1The 2:2; Isa 61:3; Efe 2:20-22; 1Pet 5:5Kwa kuwa sisi tu watendakazi pamoja na Mungu. Ninyi ni shamba la Mungu, jengo la Mungu.

103:10 Rum 12:3; 15:20; Efe 2:20Kwa neema Mungu aliyonipa, niliweka msingi kama mjenzi stadi na mtu mwingine anajenga juu yake. Lakini kila mmoja inampasa awe mwangalifu jinsi anavyojenga. 113:11 Isa 28:16; Efe 2:20Kwa maana hakuna mtu yeyote awezaye kuweka msingi mwingine wowote isipokuwa ule uliokwisha kuwekwa, ambao ni Yesu Kristo. 12Kama mtu yeyote akijenga juu ya msingi huu kwa kutumia dhahabu, fedha, vito vya thamani, miti, majani au nyasi, 133:13 1Kor 4:5; 1:8; 2The 1:7-10; 2Tim 1:12-18; 4:8; Hes 31:22-23; Yer 23:28-29; Mal 3:3; 2The 1:7kazi yake itaonekana ilivyo, kwa kuwa Siku ile itaidhihirisha. Itadhihirishwa kwa moto, nao moto utapima ubora wa kazi ya kila mtu. 143:14 1Kor 3:8; 4:5Kama kile alichojenga kitabaki, atapokea thawabu yake. 153:15 Yud 23Kama kazi kitateketea, atapata hasara, ila yeye mwenyewe ataokolewa, lakini tu kama mtu aliyenusurika kwenye moto.

163:16 1Kor 6:9; 2Kor 6:16; Efe 2:21-22; Ebr 3:6; Rum 8:9Je, hamjui ya kwamba ninyi wenyewe ni hekalu la Mungu na kwamba Roho wa Mungu anakaa ndani yenu? 17Kama mtu yeyote akiliharibu hekalu la Mungu, Mungu atamwangamiza; kwa maana hekalu la Mungu ni takatifu, na ninyi ndiyo hilo hekalu.

183:18 Isa 5:12; 1Kor 8:2; Gal 6:3; 1Kor 1:20Msijidanganye. Kama mtu yeyote miongoni mwenu akidhani kuwa ana hekima kwa viwango vya dunia hii, inampasa awe mjinga ili apate kuwa na hekima. 193:19 Rum 1:22; 1Kor 1:20-27; Ay 5:13Kwa maana hekima ya ulimwengu huu ni upuzi mbele za Mungu. Kama ilivyoandikwa: “Mungu huwanasa wenye hekima katika hila yao,” 203:20 Za 94:11tena, “Bwana anajua kwamba mawazo ya wenye hekima ni ubatili.” 213:21 1Kor 4:6; Rum 8:32Hivyo basi, mtu asijivune kuhusu wanadamu! Vitu vyote ni vyenu, 223:22 1Kor 1:12; Rum 8:38ikiwa ni Paulo au Apolo au Kefa3:22 Yaani Petro. au dunia au uzima au mauti, au wakati uliopo au wakati ujao, haya yote ni yenu 233:23 1Kor 15:23; 2Kor 10:7; Gal 3:29na ninyi ni wa Kristo, naye Kristo ni wa Mungu.