1 Akorinto 2 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Akorinto 2:1-16

1Pamene ndinabwera kwa inu, abale, sindinabwere ndi luntha lodziwa kuyankhula kapena nzeru zapamwamba pamene ndinachitira umboni chinsinsi cha Mulungu. 2Pakuti ndinatsimikiza pamene ndinali ndi inu kuti ndisadziwe kanthu kena kupatula Yesu Khristu wopachikidwayo. 3Ndinabwera kwa inu wofowoka ndi wamantha, ndiponso wonjenjemera kwambiri. 4Uthenga ndi ulaliki wanga sunali wa mawu anzeru ndi onyengerera koma woonetsa mphamvu za Mzimu, 5kuti chikhulupiriro chanu chisatsamire pa nzeru ya anthu koma pa mphamvu za Mulungu.

Nzeru Yochokera kwa Mzimu

6Komabe ife timayankhula uthenga wa nzeru kwa okhwima, koma osati ndi nzeru ya mʼbado uno kapena ya olamula a mʼbado uno, amene mphamvu yawo ikutha. 7Ayi, ife timayankhula za nzeru yobisika ya Mulungu, nzeru imene inabisidwa ndipo imene Mulungu anatikonzera mu ulemerero wathu isanayambe nthawi. 8Palibe olamulira aliyense wa mʼbado uno amene anamumvetsetsa popeza anakamumvetsetsa sakanamupachika Ambuye wa ulemerero. 9Komabe monga zalembedwa kuti,

“Palibe diso linaona,

palibe khutu linamva,

palibe amene anaganizira,

zimene Mulungu anakonzera amene amukonda”

10koma Mulungu waululira ife mwa Mzimu wake.

Mzimu amafufuza zinthu zonse, ndi zozama za Mulungu zomwe. 11Kodi ndani mwa anthu angadziwe maganizo a munthu wina, kupatula mzimu wa munthuyo wokhala mʼkati mwake? Chimodzimodzinso palibe amene adziwa maganizo a Mulungu kupatula Mzimu wa Mulunguyo. 12Mzimu amene tinalandira ife si wa dziko lapansi koma Mzimu wochokera kwa Mulungu wotipatsa ife mwaulere. 13Izi ndi zimene timayankhula osati mʼmawu wophunzitsidwa ndi nzeru za munthu koma mʼmawu wophunzitsidwa ndi Mzimu, kufotokozera zoonadi zauzimu mʼmawu auzimu. 14Munthu wopanda Mzimu savomereza zinthu zimene zichokera kwa Mzimu wa Mulungu, popeza ndi zopusa kwa iyeyo, ndipo sangazimvetsetse chifukwa zimazindikirika mwa Mzimu. 15Munthu wauzimu amaweruza pa zinthu zonse, koma iye mwini saweruzidwa ndi munthu aliyense. 16Pakuti

“Ndani anadziwa malingaliro a Ambuye,

kuti akhoza kumulangiza Iye.”

Koma tili nawo mtima wa Khristu.

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

1 Wakorintho 2:1-16

Kumtangaza Kristo Aliyesulubiwa

12:1 1Kor 1:17; 2:4; 13; 2Kor 10:10; 11; 1Kor 1:6Ndugu zangu nilipokuja kwenu, sikuja na maneno ya ushawishi wala hekima ya hali ya juu nilipowahubiria siri ya Mungu. 22:2 Gal 6:14; 1Kor 1:23Kwa kuwa niliamua kutokujua kitu chochote wakati nikiwa nanyi isipokuwa Yesu Kristo aliyesulubiwa. 32:3 Mdo 18:1-18; 1Kor 4:10; 9:22; 2Kor 11:29-30; 12:5-10; 13:9; 7:15Mimi nilikuja kwenu nikiwa dhaifu na mwenye hofu na kwa kutetemeka sana. 42:4 Rum 15:13; 1Kor 2:1; 1:17; 2Pet 1:16Kuhubiri kwangu na ujumbe wangu haukuwa kwa hekima na maneno ya ushawishi bali kwa madhihirisho ya nguvu za Roho 5ili imani yenu isiwe imejengwa katika hekima ya wanadamu bali katika nguvu za Mungu.

Hekima Ya Kweli Itokayo Kwa Mungu

62:6 Efe 4:13; Flp 3:15; Kol 4:12; Ebr 5:14; 6:1; Yak 1:4; 1Kor 1:20; Za 146:4Lakini miongoni mwa watu waliokomaa twanena hekima, wala si hekima ya ulimwengu huu au ya watawala wa dunia hii wanaobatilika. 72:7 Rum 16:25; Efe 3:5, 9; Kol 1:26; 2Tim 1:9Sisi tunanena hekima ya Mungu ambayo ni siri, tena iliyofichika, ambayo Mungu aliikusudia kabla ya ulimwengu kuwepo, kwa ajili ya utukufu wetu. 82:8 1Kor 1:20; Za 24:7; Mdo 7:2; Yak 2:1Hakuna hata mtawala mmoja wa nyakati hizi aliyeelewa jambo hili. Kwa maana kama wangelielewa, wasingemsulubisha Bwana wa utukufu. 92:9 Isa 64:4; 65:17Lakini ni kama ilivyoandikwa:

“Hakuna jicho limepata kuona,

wala sikio limepata kusikia,

wala hayakuingia moyoni wowote,

yale Mungu amewaandalia

wale wampendao”:

102:10 Mt 13:11; 2Kor 12:1-7; Gal 1:12; 2:2; Efe 3:3-5; Yn 14:26Lakini mambo haya Mungu ametufunulia kwa Roho wake.

Roho huchunguza kila kitu, hata mambo ya ndani sana ya Mungu. 112:11 Yer 17:9; Mit 20:27Kwa maana ni nani anayejua mawazo ya mtu isipokuwa roho iliyo ndani ya huyo mtu? Vivyo hivyo hakuna mtu ajuaye mawazo ya Mungu isipokuwa Roho wa Mungu. 122:12 Rum 8:15; 1Kor 1:20-27; Yak 2:5Basi hatukupokea roho ya dunia bali Roho atokaye kwa Mungu, ili tuweze kuelewa kile kipawa ambacho Mungu ametupatia bure. 132:13 1Kor 1:17Haya ndiyo tusemayo, si kwa maneno tuliyofundishwa kwa hekima ya wanadamu bali kwa maneno tuliyofundishwa na Roho, tukifafanua kweli za kiroho kwa maneno ya kiroho. 142:14 Yn 14:17; 1Kor 3:1Mtu ambaye hana Roho hawezi kupokea mambo yatokayo kwa Roho wa Mungu, kwa kuwa ni upuzi kwake, naye hawezi kuyaelewa kwa sababu hayo yanaeleweka tu kwa upambanuzi wa rohoni. 152:15 1Kor 3:1; Gal 6:1Mtu wa kiroho hubainisha mambo yote, lakini yeye mwenyewe habainishwi na mtu yeyote.

162:16 Isa 40:13; Rum 11:34; Yn 15:15“Kwa maana ni nani aliyefahamu mawazo ya Bwana

ili apate kumfundisha?”

Lakini sisi tunayo mawazo ya Kristo.