1 Akorinto 2 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Akorinto 2:1-16

1Pamene ndinabwera kwa inu, abale, sindinabwere ndi luntha lodziwa kuyankhula kapena nzeru zapamwamba pamene ndinachitira umboni chinsinsi cha Mulungu. 2Pakuti ndinatsimikiza pamene ndinali ndi inu kuti ndisadziwe kanthu kena kupatula Yesu Khristu wopachikidwayo. 3Ndinabwera kwa inu wofowoka ndi wamantha, ndiponso wonjenjemera kwambiri. 4Uthenga ndi ulaliki wanga sunali wa mawu anzeru ndi onyengerera koma woonetsa mphamvu za Mzimu, 5kuti chikhulupiriro chanu chisatsamire pa nzeru ya anthu koma pa mphamvu za Mulungu.

Nzeru Yochokera kwa Mzimu

6Komabe ife timayankhula uthenga wa nzeru kwa okhwima, koma osati ndi nzeru ya mʼbado uno kapena ya olamula a mʼbado uno, amene mphamvu yawo ikutha. 7Ayi, ife timayankhula za nzeru yobisika ya Mulungu, nzeru imene inabisidwa ndipo imene Mulungu anatikonzera mu ulemerero wathu isanayambe nthawi. 8Palibe olamulira aliyense wa mʼbado uno amene anamumvetsetsa popeza anakamumvetsetsa sakanamupachika Ambuye wa ulemerero. 9Komabe monga zalembedwa kuti,

“Palibe diso linaona,

palibe khutu linamva,

palibe amene anaganizira,

zimene Mulungu anakonzera amene amukonda”

10koma Mulungu waululira ife mwa Mzimu wake.

Mzimu amafufuza zinthu zonse, ndi zozama za Mulungu zomwe. 11Kodi ndani mwa anthu angadziwe maganizo a munthu wina, kupatula mzimu wa munthuyo wokhala mʼkati mwake? Chimodzimodzinso palibe amene adziwa maganizo a Mulungu kupatula Mzimu wa Mulunguyo. 12Mzimu amene tinalandira ife si wa dziko lapansi koma Mzimu wochokera kwa Mulungu wotipatsa ife mwaulere. 13Izi ndi zimene timayankhula osati mʼmawu wophunzitsidwa ndi nzeru za munthu koma mʼmawu wophunzitsidwa ndi Mzimu, kufotokozera zoonadi zauzimu mʼmawu auzimu. 14Munthu wopanda Mzimu savomereza zinthu zimene zichokera kwa Mzimu wa Mulungu, popeza ndi zopusa kwa iyeyo, ndipo sangazimvetsetse chifukwa zimazindikirika mwa Mzimu. 15Munthu wauzimu amaweruza pa zinthu zonse, koma iye mwini saweruzidwa ndi munthu aliyense. 16Pakuti

“Ndani anadziwa malingaliro a Ambuye,

kuti akhoza kumulangiza Iye.”

Koma tili nawo mtima wa Khristu.

Słowo Życia

1 Koryntian 2:1-16

1Przyjaciele, ja także, gdy do was przybyłem i opowiadałem wam o Bożej tajemnicy, nie używałem wielkich słów i błyskotliwych myśli. 2Postanowiłem bowiem mówić tylko o Jezusie Chrystusie i Jego śmierci na krzyżu. 3Stanąłem przed wami jako słaby człowiek—nieśmiały i drżący ze strachu. 4Moje nauczanie nie było podobne do przemówień mędrców, ale było za to pełne Ducha i mocy Boga. 5Chciałem bowiem, aby wasza wiara opierała się właśnie na Jego mocy, a nie na ludzkiej mądrości.

Mądrość od Ducha

6A jednak to, co głosimy, ludzie dojrzali w wierze przyjmują jako mądrość, choć nie jest to mądrość tego świata ani jego przemijających przywódców. 7Mówimy bowiem o tajemnej mądrości samego Boga, która, ze względu na nas, była ukryta przez całe wieki. 8Żaden z przywódców tego świata jej nie pojął, bo gdyby było inaczej, nie ukrzyżowaliby Pana chwały. 9Pismo mówi:

„Dla tych, którzy kochają Boga,

przygotował On rzeczy,

jakich nikt nigdy nie widział,

o jakich nikt nigdy nie słyszał,

i jakie nikomu nawet nie przyszły na myśl”.

10Bóg objawił to nam przez swojego Ducha! On bowiem przenika wszystko i zna najgłębsze Boże tajemnice. 11Kto wie, co kryje się w człowieku, jeśli nie on sam, czyli jego duch? Podobnie nikt, poza Duchem Bożym, nie może wniknąć w Boga. 12Nie przyjęliśmy przecież ducha tego świata. Otrzymaliśmy Ducha Boga, abyśmy mogli zrozumieć, czym nas obdarował. 13I mówimy o tym nie w błyskotliwych słowach ludzkiej mądrości, ale słowami pochodzącymi od Ducha Świętego—duchowe sprawy wyrażając w duchowy sposób. 14Człowiek, kierujący się tylko zmysłami, nie rozumie rzeczy pochodzących od Ducha Bożego. Wydają mu się głupie i nie jest w stanie ich pojąć, bo można je zrozumieć tylko dzięki Duchowi. 15Człowiek kierowany przez Ducha Świętego rozumie zaś to wszystko, ale inni go nie rozumieją. 16Pismo mówi:

„Kto ogarnie myśli Pana?

Kto może zostać Jego doradcą?”.

My znamy zamiary Chrystusa!