2 Akorinto 1 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Akorinto 1:1-24

1Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, pamodzi ndi mʼbale wathu Timoteyo,

Kulembera mpingo wa Mulungu mu Korinto, pamodzi ndi oyera mtima onse mu Akaya monse.

2Mukhale ndi chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.

Mulungu Mwini Chitonthozo

3Alemekezeke Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, Atate achifundo chonse, Mulungu wachitonthozo chonse. 4Iye amatitonthoza ife mʼmavuto athu onse, kuti ifenso tithe kutonthoza amene ali pavuto lililonse ndi chitonthozo chimene ife tilandira kwa Mulungu. 5Pakuti monga momwe tili mʼmasautso pamodzi ndi Khristu, momwemonso Khristu amatitonthoza kwambiri. 6Ngati ife tikusautsidwa, nʼchifukwa choti inu mutonthozedwe ndi kupulumutsidwa. Ngati ife tikutonthozedwa nʼchifukwa choti inu mutonthozedwe, ndi chitonthozo chimene chimabweretsa mwa inu kupirira kosawiringula pa zosautsa zomwe timasauka nazo ife. 7Ndipo chiyembekezo chathu pa inu nʼcholimba chifukwa tikudziwa kuti monga momwe mumamva zowawa pamodzi nafe, momwemonso mumatonthozedwa nafe pamodzi.

8Abale, sitikufuna kuti mukhale osadziwa za masautso amene tinakumana nawo mʼchigawo cha Asiya. Tinapanikizidwa koopsa kuposa muyeso woti nʼkutha kupirira, mwakuti sitinkadziwa kuti nʼkukhalabe ndi moyo. 9Zoonadi, tinamva mʼmitima mwathu chilango cha imfa. Koma izi zimachitika kuti tisangodzidalira mwa ife tokha koma Mulungu yemwe amaukitsa akufa. 10Mulungu watilanditsa ku zoopsa zotere za imfa, ndipo adzatilanditsanso. Ife tayika chiyembekezo chathu pa Iyeyo kuti adzapitiriza kutilanditsabe. 11Mutithandize potipempherera. Pamenepo ambiri adzathokoza mʼmalo mwathu, chifukwa cha chisomo chake poyankha mapemphero a anthu ambiri.

Paulo Afotokoza za Kusintha kwa Ulendo Wake

12Tsono chonyadira chathu nʼchakuti, chikumbumtima chathu chimatitsimikizira kuti timakhala bwino mʼdziko lapansi, makamaka pa ubale wathu ndi inu. Takhala moona mtima ndi oyera mtima. Sitinachite chomwechi mwa nzeru ya dziko lapansi koma monga mwa chisomo cha Mulungu. 13Pakuti sitikukulemberani zoti simungawerenge kapena kumvetsetsa. 14Monga mwamva pangʼono chabe, ndikuyembekeza kuti mudzamvetsa kwenikweni, kuti mutha kutinyadira monga ife tidzakunyadirani, pa tsiku la Ambuye Yesu.

15Popeza ndinatsimikiza mtima za ichi, nʼchifukwa chake ndinafuna kuti poyamba, ndidzakuchezereni kuti mupindule pawiri. 16Ndinafuna kuti ndidzakuchezereni pa ulendo wanga wopita ku Makedoniya ndi kudzakuonaninso pochokera ku Makedoniyako kuti inu mudzandithandize pa ulendo wanga wopita ku Yudeya. 17Kodi pamene ndinkakonzekera zimenezi, mukuganiza kuti ndinkachita mwachibwana? Kapena kuti ndinkaganiza ngati mwa dziko lapansi; kuti ndikhoza kumanena kuti, “Inde, Inde,” nthawi yomweyo nʼkumatinso “Ayi, Ayi?”

18Koma zoona monga Mulungu ali wokhulupirika, uthenga wathu kwa inu siwakuti, “Inde” nʼkutinso “Ayi.” 19Pakuti Yesu Khristu mwana wa Mulungu amene ine, Silivano ndi Timoteyo tinamulalikira pakati panu sali “Inde” yemweyonso “Ayi.” Koma nthawi zonse mwa Iye muli “Inde.” 20Pakuti ngakhale malonjezo a Mulungu atachuluka chotani, onsewo ndi “Inde” mwa Khristu. Kotero kuti mwa Iye, ife timati “Ameni” kuchitira Mulungu ulemu. 21Tsono ndi Mulungu amene anachititsa kuti inu ndi ife tiyime molimba mwa Khristu. Anatidzoza ife, 22nayikanso Mzimu wake mʼmitima mwathu kutitsimikizira za mʼtsogolo.

23Mulungu ndi mboni yanga kuti sindinabwererenso ku Korinto kuno kuti ndisakumvetseni chisoni. 24Sikuti ife tikufuna kukhala olamulira chikhulupiriro chanu, koma timagwira nanu ntchito pamodzi kuti mukhale achimwemwe, chifukwa ndinu okhazikika kwambiri mʼchikhulupiriro.

Słowo Życia

2 Koryntian 1:1-24

Pozdrowienie

1Ja, Paweł, powołany przez Boga na apostoła Chrystusa Jezusa, wraz z Tymoteuszem, uczniem Pana, piszę do kościoła Bożego w Koryncie oraz do wszystkich świętych w całej Achai. 2Niech Bóg, nasz Ojciec, i Jezus Chrystus, nasz Pan, obdarzają was swoją łaską i pokojem!

Bóg dodaje nam otuchy

3Jakże wspaniały jest Bóg, Ojciec Jezusa Chrystusa, naszego Pana, będący źródłem miłości i zachęty! 4To On w każdej trudnej sytuacji dodaje nam otuchy, abyśmy i my mogli dodawać otuchy tym, którzy znajdują się w jakimś trudnym położeniu. 5Im więcej cierpimy dla Chrystusa, tym większego doznajemy od Niego pokrzepienia. 6Przykrości, które nas spotykają, służą waszej zachęcie i zbawieniu. A pocieszenie, którego doznajemy, jest zachętą również dla was, abyście wytrwale znosili cierpienia, podobnie jak my. 7W pełni ufamy wam, bo wiemy, że doświadczacie tych samych cierpień i doznajecie tej samej pociechy, co my.

8Przyjaciele, chcemy, abyście wiedzieli o trudnościach, z jakimi borykaliśmy się w prowincji Azja. Byliśmy nimi przytłoczeni ponad nasze siły i nie wiedzieliśmy, czy wyjdziemy z nich z życiem. 9Stanąwszy w obliczu śmierci, zrozumieliśmy jednak, że nie mamy polegać na sobie, ale na Bogu. On może przecież nawet ożywić umarłych! 10To On ocalił nas od śmierci i wierzymy, że nadal będzie nas chronił, 11bo o to właśnie do Niego się modlicie. Wielu ludzi będzie więc dziękować Bogu za wszystko, czego dla nas dokonał w odpowiedzi na wasze modlitwy.

Zmiana planów Pawła

12Mamy ogromną satysfakcję z tego, że w stosunku do wszystkich ludzi—także do was—zawsze postępowaliśmy otwarcie i uczciwie. Nie polegaliśmy bowiem na własnej mądrości, ale na łasce Boga. 13A teraz nie piszemy wam nic, czego nie bylibyście w stanie zrozumieć i zaakceptować. Mam nadzieję, że w pełni to przyjmiecie. 14Częściowo zresztą już uznaliście, że przed Panem, w dniu Jego powrotu, będziemy wszyscy nawzajem z siebie dumni—wy z nas, a my z was.

15Z taką myślą zamierzałem już wcześniej was odwiedzić, abyście ponownie doznali radości. 16Chciałem zatrzymać się u was udając się do Macedonii, a także w drodze powrotnej, abyście mogli mnie wyprawić do Judei.

Powody zwłoki

17Czy byłem lekkomyślny, mając taki zamiar? Czy zmieniając go, postąpiłem jak ludzie, którzy mówią „tak”, a myślą „nie”? 18Bóg mi świadkiem, że nigdy was nie okłamaliśmy!

19Jezus Chrystus, Syn Boży, o którym opowiadałem wam razem z Tymoteuszem i Sylwanem, nigdy nie kłamał i Jego „tak” zawsze znaczyło „tak”. 20On jest spełnieniem wszystkich obietnic Boga. A my, potwierdzając to, oddajemy Bogu chwałę. 21To On przecież dodał nam sił, wzmocnił naszą więź z Chrystusem i wybrał nas. 22On również oznaczył nas jako swoją własność—dał nam do serc Ducha Świętego jako gwarancję przynależności do Niego.

23Bóg mi świadkiem, że chciałem zaoszczędzić wam przykrości i tylko z tego powodu nie przybyłem jeszcze do Koryntu. 24Nie chodzi przecież o to, żebyśmy udowadniali wam, że mamy nad wami władzę i możemy nauczać was, jak należy wierzyć. Chcemy przecież współdziałać z wami i pragniemy waszej radości, której podstawą jest wiara w Chrystusa.