1 Akorinto 12 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Akorinto 12:1-31

Mphatso za Mzimu Woyera

1Tsopano abale anga okondedwa, sindikufuna mukhale osadziwa za mphatso za Mzimu. 2Inu mukudziwa kuti pamene munali akunja, ankakusocheretsani mʼnjira zosiyanasiyana ndi kukukokerani ku mafano osayankhula. 3Nʼchifukwa chake ndikuwuzani kuti palibe munthu amene ali ndi Mzimu wa Mulungu angayankhule kuti, “Yesu atembereredwe,” ndiponso palibe munthu anganene kuti “Yesu ndi Ambuye,” popanda kutsogozedwa ndi Mzimu Woyera.

4Pali mphatso zosiyanasiyana, koma Mzimu yemweyo. 5Pali mautumiki osiyanasiyana koma Ambuye yemweyo. 6Pali magwiridwe antchito osiyanasiyana, koma Mulungu yemweyo amagwira ntchito monsemo mwa anthu onse.

7Tsono Mzimu amapereka mphatso kwa aliyense kuti ipindulire onse. 8Mzimu amapereka kwa munthu wina mawu anzeru, Mzimu yemweyonso amapereka kwa wina mawu achidziwitso. 9Kwa wina, Mzimu yemweyo amapereka chikhulupiriro, kwa wina mphatso zamachiritso, Mzimu yemweyo. 10Kwa wina mphamvu zochita zodabwitsa, kwa wina mawu a uneneri, kwa wina mphatso yozindikira mizimu, kwa wina malilime osiyanasiyana, ndiponso kwa wina kutanthauzira malilimewo. 11Zonsezi ndi ntchito za Mzimu mmodzi yemweyo, ndipo amapereka kwa munthu aliyense monga momwe Mzimuyo wafunira.

Thupi Limodzi Ziwalo Zambiri

12Thupi ndi limodzi, ngakhale kuti lapangidwa ndi ziwalo zambiri. Ndipo ngakhale ziwalo zake zonse ndi zambiri, zimapanga thupi limodzi. Momwemonso ndi mmene alili Khristu. 13Pakuti tonse tinabatizidwa ndi Mzimu mmodzi mʼthupi limodzi. Myuda kapena Mgriki, kapolo kapena mfulu tonse tinapatsidwa kuti timwe Mzimu mmodzi yemweyo. 14Tsopano thupi silinapangidwe ndi chiwalo chimodzi koma ndi ziwalo zambiri.

15Ngati phazi litanena kuti, “Pakuti sindine dzanja, sindine chiwalo cha thupi.” Chifukwa chimenechi sichingachititse phazi kuti lisakhale chiwalo cha thupi. 16Ndipo ngati khutu litanena kuti, “Pakuti sindine diso, sindine chiwalo cha thupi.” Chifukwa chimenechi sichingachititse khutu kuti lisakhale chiwalo cha thupi. 17Kodi thupi lonse likanakhala diso, tikanamamva bwanji? Nanga thupi lonse likanakhala khutu, tikanamanunkhiza bwanji? 18Koma zoona nʼzakuti, Mulungu anayika ziwalo mʼthupi, chilichonse monga momwe Iye anafunira. 19Nanga zonse zikanakhala chiwalo chimodzi, ndiye thupi likanakhala lotani? 20Mmene zililimu, pali ziwalo zambiri koma thupi ndi limodzi lokha.

21Diso silingawuze dzanja kuti, “Iwe sindikukufuna!” Ndipo mutu sungawuze phazi kuti “Iwe sindikukufuna!” 22Mʼmalo mwake, ziwalo zathupi zimene zimaoneka ngati zofowoka ndizo zili zofunikira kwambiri, 23ndipo ziwalo zathupi zimene timaziyesa zopanda ulemu, ndizo timazilemekeza kwambiri. Ndipo ziwalo zosaoneka bwino ndizo zimalandira ulemu wapadera. 24Koma ziwalo zooneka bwino, nʼkosafunika kuti tizisamalire mwapadera. Mulungu polumikiza ziwalo zathupi, anapereka ulemu wopambana kwa ziwalo zimene zimafunadi ulemuwo 25kuti pasakhale kugawikana mʼthupi koma kuti ziwalo zonse zisamalirane. 26Ngati chiwalo chimodzi chikumva kuwawa, ziwalo zonse zimamvanso kuwawa. Ngati chiwalo chimodzi chilandira ulemu, ziwalo zonse zimakondwera nawo.

27Tsopano inu ndinu thupi la Khristu, ndipo aliyense wa inu ndi chiwalo cha thupilo. 28Ndipo Mulungu mu mpingo anayika poyamba atumwi, kachiwiri aneneri, kachitatu aphunzitsi, kenaka ochita zozizwitsa, ena a mphatso zamachiritso, ena a mphatso yothandiza anzawo, ena a mphatso yotsogolera ndiponso ena a mphatso ya malilime. 29Kodi onse ndi atumwi? Kodi onse ndi aneneri? Kodi onse ndi aphunzitsi? Kodi onse amachita zozizwitsa? 30Kodi onse ali ndi mphatso zamachiritso? Kodi onse amayankhula malilime? Kodi onse amatanthauzira malilime? 31Koma funitsitsani mphatso zopambana.

Tsopano ndikuonetsani njira yopambana kwambiri.

Slovo na cestu

1. Korintským 12:1-31

Pavel ukazuje, jak Bůh obohacuje společenství věřících nevšedními duchovními dary

1Co se týká projevů Božího Ducha, rád bych, abyste v té věci měli jasno. 2-3Sami víte, že modly, které jste nevšedními dary uctívali, byly mrtvé a němé. Teď se však setkáváte s lidmi, kteří o sobě prohlašují, že jejich ústy mluví Bůh. Jak si to můžete ověřit? Spolehlivým vodítkem je vždy toto: kdo pohrdá Kristem, nejedná z pověření Božího Ducha. A naopak: za Pána prohlašuje Krista jen ten, koho k tomu vede Boží Duch.

4Je mnoho rozmanitých obdarování, ale Duch je jenom jeden. 5Způsoby služby se mohou velice různit, Pán je však stále tentýž. 6Duch se projevuje rozmanitě případ od případu, ale vždycky v každém z nás jde o dílo téhož Boha. 7Jím obdarovaní jednotlivci mají každý svým způsobem sloužit celé církvi: 8jednomu Boží Duch dává schopnost moudře mluvit, jinému skvěle formulovat nejhlubší myšlenky. 9Jednomu dává tentýž Duch víru, která působí zázraky, jinému schopnost uzdravovat 10a jinému zase schopnost velkých činů. Někdo jeho prostřednictvím dovede tlumočit Boží poselství, jiný rozlišovat, z jakého ducha co pochází. A další je obdařen schopností mluvit jinými jazyky a další zase schopností takovou neznámou řeč vyložit srozumitelně. 11To vše je dílo jednoho a téhož Ducha, který každému jednotlivci přiděluje takové obdarování, jaké uzná za dobré.

Věřící tvoří Kristovo tělo

12Křesťanské společenství se dá přirovnat k lidskému tělu, kde je také mnoho údů a orgánů, které tvoří jediný celek. 13Tak i každý z nás, ať žid nebo pohan, otrok nebo svobodný občan, byl při křtu začleněn do jednoho společného těla. Způsobil to jeden a týž Duch, kterého nyní společně sdílíme.

14Tělo – to přece není jediný orgán, nýbrž mnoho orgánů. 15Dejme tomu, že by noha řekla: „Já k tělu nepatřím, protože nejsem ruka.“ Proto však ještě nepřestává patřit k tělu. 16Nebo kdyby řeklo ucho: „Já k tělu nepatřím, když nejsem oko,“ přestává snad proto být částí těla? 17Kdyby celé tělo bylo okem, jak by mohlo slyšet? A kdyby bylo celé uchem, kde by byl čich? 18Bůh však určil každému orgánu zvláštní úlohu v těle, jak sám chtěl. 19Kdyby totiž celek byl jediným orgánem, nebylo by tu žádné tělo. 20Takto máme mnoho různých orgánů, ale všechny dohromady tvoří jediný organismus. 21Oko nemůže říci ruce: „Nepotřebuji tě,“ ani hlava noze: „Obejdu se bez tebe.“ 22Spíš naopak: právě ty zdánlivě podřadné orgány jsou nepostradatelné 23-25a zrovna těm orgánům, za které se stydíme, věnujeme při oblékání zvláštní péči. Bůh zařídil naše tělo tak, aby se „důstojné“ údy staraly o „nedůstojné“, aby za ně nesly odpovědnost a aby tělo jako celek bylo jednotné. 26Když trpí jeden orgán, cítí to i všechny ostatní. Když je jeden z nich obdivován, radují se všechny.

27Vy jste nyní Kristovo tělo a každý z vás je údem či orgánem toho těla. 28V našem společenství ustanovil Bůh jedny jako své vyslance, druhé jako proroky, třetí jako učitele, dalším dal moc k podivuhodným činům, některým schopnost uzdravovat, jiným sílu sloužit potřebným nebo spravovat církev či mluvit jazyky. 29Jsme snad všichni apoštoly? Jsou všichni proroky, všichni učiteli? Mají všichni moc činit divy, 30uzdravovat, mluvit jazyky a vykládat je? On dává organizační schopnosti k vedení církve, ale umění sloužit v maličkostech je také jeho dar.

31Usilujte o ty dary, které jsou jiným nejprospěšnější.