2 Akorinto 1 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Akorinto 1:1-24

1Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, pamodzi ndi mʼbale wathu Timoteyo,

Kulembera mpingo wa Mulungu mu Korinto, pamodzi ndi oyera mtima onse mu Akaya monse.

2Mukhale ndi chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.

Mulungu Mwini Chitonthozo

3Alemekezeke Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, Atate achifundo chonse, Mulungu wachitonthozo chonse. 4Iye amatitonthoza ife mʼmavuto athu onse, kuti ifenso tithe kutonthoza amene ali pavuto lililonse ndi chitonthozo chimene ife tilandira kwa Mulungu. 5Pakuti monga momwe tili mʼmasautso pamodzi ndi Khristu, momwemonso Khristu amatitonthoza kwambiri. 6Ngati ife tikusautsidwa, nʼchifukwa choti inu mutonthozedwe ndi kupulumutsidwa. Ngati ife tikutonthozedwa nʼchifukwa choti inu mutonthozedwe, ndi chitonthozo chimene chimabweretsa mwa inu kupirira kosawiringula pa zosautsa zomwe timasauka nazo ife. 7Ndipo chiyembekezo chathu pa inu nʼcholimba chifukwa tikudziwa kuti monga momwe mumamva zowawa pamodzi nafe, momwemonso mumatonthozedwa nafe pamodzi.

8Abale, sitikufuna kuti mukhale osadziwa za masautso amene tinakumana nawo mʼchigawo cha Asiya. Tinapanikizidwa koopsa kuposa muyeso woti nʼkutha kupirira, mwakuti sitinkadziwa kuti nʼkukhalabe ndi moyo. 9Zoonadi, tinamva mʼmitima mwathu chilango cha imfa. Koma izi zimachitika kuti tisangodzidalira mwa ife tokha koma Mulungu yemwe amaukitsa akufa. 10Mulungu watilanditsa ku zoopsa zotere za imfa, ndipo adzatilanditsanso. Ife tayika chiyembekezo chathu pa Iyeyo kuti adzapitiriza kutilanditsabe. 11Mutithandize potipempherera. Pamenepo ambiri adzathokoza mʼmalo mwathu, chifukwa cha chisomo chake poyankha mapemphero a anthu ambiri.

Paulo Afotokoza za Kusintha kwa Ulendo Wake

12Tsono chonyadira chathu nʼchakuti, chikumbumtima chathu chimatitsimikizira kuti timakhala bwino mʼdziko lapansi, makamaka pa ubale wathu ndi inu. Takhala moona mtima ndi oyera mtima. Sitinachite chomwechi mwa nzeru ya dziko lapansi koma monga mwa chisomo cha Mulungu. 13Pakuti sitikukulemberani zoti simungawerenge kapena kumvetsetsa. 14Monga mwamva pangʼono chabe, ndikuyembekeza kuti mudzamvetsa kwenikweni, kuti mutha kutinyadira monga ife tidzakunyadirani, pa tsiku la Ambuye Yesu.

15Popeza ndinatsimikiza mtima za ichi, nʼchifukwa chake ndinafuna kuti poyamba, ndidzakuchezereni kuti mupindule pawiri. 16Ndinafuna kuti ndidzakuchezereni pa ulendo wanga wopita ku Makedoniya ndi kudzakuonaninso pochokera ku Makedoniyako kuti inu mudzandithandize pa ulendo wanga wopita ku Yudeya. 17Kodi pamene ndinkakonzekera zimenezi, mukuganiza kuti ndinkachita mwachibwana? Kapena kuti ndinkaganiza ngati mwa dziko lapansi; kuti ndikhoza kumanena kuti, “Inde, Inde,” nthawi yomweyo nʼkumatinso “Ayi, Ayi?”

18Koma zoona monga Mulungu ali wokhulupirika, uthenga wathu kwa inu siwakuti, “Inde” nʼkutinso “Ayi.” 19Pakuti Yesu Khristu mwana wa Mulungu amene ine, Silivano ndi Timoteyo tinamulalikira pakati panu sali “Inde” yemweyonso “Ayi.” Koma nthawi zonse mwa Iye muli “Inde.” 20Pakuti ngakhale malonjezo a Mulungu atachuluka chotani, onsewo ndi “Inde” mwa Khristu. Kotero kuti mwa Iye, ife timati “Ameni” kuchitira Mulungu ulemu. 21Tsono ndi Mulungu amene anachititsa kuti inu ndi ife tiyime molimba mwa Khristu. Anatidzoza ife, 22nayikanso Mzimu wake mʼmitima mwathu kutitsimikizira za mʼtsogolo.

23Mulungu ndi mboni yanga kuti sindinabwererenso ku Korinto kuno kuti ndisakumvetseni chisoni. 24Sikuti ife tikufuna kukhala olamulira chikhulupiriro chanu, koma timagwira nanu ntchito pamodzi kuti mukhale achimwemwe, chifukwa ndinu okhazikika kwambiri mʼchikhulupiriro.

Slovo na cestu

2. Korintským 1:1-24

Úvodní pozdravy

1Drazí bratři, tento dopis vám píši jako Bohem zmocněný posel Ježíše Krista, společně s Timotejem. Adresovaný je sice k vám do Korintu, ale je určen všem křesťanům v celém Řecku: 2kéž vás náš Otec Bůh i Ježíš Kristus bohatě obdarují svou milostí a pokojem.

Bůh pomáhá v utrpení

3-4Jak nevýslovně dobrý je náš Bůh. V něm, Otci našeho Pána Ježíše Krista, máme nevyčerpatelný zdroj útěchy a posily pro naše zkoušky a utrpení, takže i jiné pak můžeme těšit a posilovat, když je to zapotřebí. 5Stejnou pomoc, jakou jsme obdrželi od Boha, rozdáváme všude kolem sebe. 6Můžete se spolehnout, že čím víc utrpení podstoupíme pro Krista, tím hojněji nás zahrne svou útěchou a povzbuzením. Kristovo utrpení je mým denním chlebem, ale to je můj příspěvek k vaší záchraně. 7On mi však denně dává též novou sílu a klid – a to má být zase posilou vám ve vašich zkouškách. Pokud s námi sdílíte naše bolesti, nemám o vás obavy: zdroj naší útěchy je otevřen i pro vás.

8-9Nebudu vám, drazí, tajit, že tady v Malé Asii jsme prožili snad nejhorší chvíle svého života. Vypadalo to už, že je s námi konec, připravovali jsme se na smrt. Cítím, že to muselo dojít tak daleko proto, abychom nespoléhali již na nic jiného než na Boha, který má moc vzkřísit i mrtvé. 10Skutečně nás vyrval přímo z drápů smrti a věřím, že ne naposledy. 11Přesto prosím, abyste na nás stále mysleli ve svých modlitbách – tím větší budou pak vaše chvály a vděčnost za jejich vyslyšení.

12S naprosto čistým svědomím mohu prohlásit, že jsem s vámi ve všech směrech jednal vždy jen a jen upřímně, jak mě Bůh vedl, a na to jsem hrdý. Ne lidská vypočítavost, ale Boží milost je mi vůdčí silou. To platilo vždy i ve vztahu k vám. 13-14Všechno, co čtete v mých listech, je míněno naprosto upřímně. Doufám, že to tak přijmete, i když se dosud mnoho neznáme, a že při Kristově návratu se za sebe navzájem nebudeme muset stydět, ale naopak budeme mít důvod k hrdosti.

Pavel mění plán svých cest

15V této důvěře jsem vás chtěl navštívit už na cestě do Makedonie a pak se vrátit do Judska zase přes Korint. 16-20Proč jsem svůj plán později změnil? Nebylo to z vrtkavosti ani z lehkomyslnosti. Když jednou něco řeknu, pak to také tak myslím; nikdy neříkám „ano“, když myslím „ne“, a naopak. Boží Syn Ježíš Kristus, jak jsme vám ho přiblížili se Silvánem a Timotejem, také nebyl muž dvojí tváře. Jeho osoba je hmatatelným ANO všem slibům, které Bůh kdy dal člověku. Proto taky, když k modlitbě připojíme Amen (tj. „ano“), připomínáme si vlastně, že v Kristu na ně Bůh už odpověděl, a oslavujeme ho za to. 21Že jste v Kristu obdrželi tentýž nový život jako my, že v něm dosud pevně stojíme – to je jen Boží dílo. 22To on nás učinil svým vlastnictvím, pověřil svým poselstvím a vtiskl nám svou vlastnickou pečeť – svatého Ducha – jako záruku na vše ostatní, co má ještě pro nás přichystáno.

23Pán Bůh ví, že to nebylo jinak, než vám tady píšu: Korint jsem nakonec rozhodl vynechat jen proto, abych vás ušetřil setkání, které by pro vás mohlo být velice trapné. 24Ne že bych vám chtěl vytýkat nedostatky ve vaší víře – v té si stojíte docela dobře.