馬可福音 16 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

馬可福音 16:1-20

耶穌復活

1過了安息日,抹大拉瑪麗亞雅各的母親瑪麗亞撒羅米買了香料,要去抹耶穌的遺體。 2週日清早,太陽剛剛升起,她們就去墳墓那裡。 3途中她們彼此議論說:「誰能替我們滾開墓口那塊大石頭呢?」 4她們抬頭一看,那塊大石頭已經滾到一旁。 5她們進了墳墓,看見一位身穿潔白長袍的青年坐在右邊,嚇了一跳。 6那青年對她們說:「不要害怕,你們要找那位被釘十字架的拿撒勒人耶穌嗎?祂已經復活了,不在這裡。你們看!這是安放祂的地方。 7你們快回去,告訴祂的門徒,特別是彼得,『祂先你們一步去了加利利,你們將在那裡見到祂,正如祂以前所說的一樣。』」

8她們從墳墓出來,跑走了,戰戰兢兢,疑惑不已,什麼也沒有告訴他人,因為她們很害怕。

耶穌顯現

9耶穌在週日清晨復活後,首先向抹大拉瑪麗亞顯現,耶穌曾在她身上趕出七個鬼。 10瑪麗亞趕到門徒那裡,看見他們仍然在哭泣哀悼, 11就告訴他們耶穌已經復活了,還向她顯現過,但他們不相信。

12此後,有兩個門徒在去鄉下的路上,看到耶穌以另一種形像向他們顯現。 13他們回去告訴其他的門徒,但門徒還是不相信。

最後的使命

14後來,當十一位門徒在一起吃飯的時候,耶穌向他們顯現,責備他們又不信又固執,因為他們不肯相信那些人在祂復活後見過祂。 15耶穌又對他們說:「你們要到世界各地去,向全人類傳揚福音。 16相信並接受洗禮的人必定得救,不肯相信的人必被定罪。 17必有神蹟隨著信我的人,他們能奉我的名趕鬼,說新的方言, 18又能用手拿蛇,萬一喝了什麼毒物,也不會受害。他們把手按在病人身上,病人就可痊癒。」 19主耶穌說完這些話,就被接回天上,坐在上帝的右邊。 20門徒出去到處傳揚福音,主和他們一同工作,藉著神蹟證實他們所傳的道。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 16:1-20

Kuuka kwa Yesu

1Litapita tsiku la Sabata, Mariya Magadalena, ndi amayi ake a Yakobo, ndi Salome anagula zonunkhiritsa ndi cholinga chakuti apite akadzoze thupi la Yesu. 2Mmamawa, tsiku loyamba la Sabata, dzuwa litangotuluka kumene, anali pa ulendo wopita ku manda 3ndipo anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi akatikugudubuzira mwala pa khomo la manda ndani?”

4Koma atakweza maso awo, anaona kuti mwala umene unali waukulu kwambiri wagubuduzidwa kale. 5Atalowa mʼmanda, anaona mnyamata atavala mwinjiro woyera atakhala ku mbali ya kumanja, ndipo iwo anachita mantha.

6Iye anati, “Musaope. Kodi mukufuna Yesu wa ku Nazareti, amene anapachikidwa? Wauka! Sali muno. Onani malo amene anamugonekapo. 7Koma pitani, kawuzeni ophunzira ake ndi Petro kuti, ‘Iye watsogola kupita ku Galileya. Kumeneko mukamuona Iye monga momwe anakuwuzirani.’ ”

8Akunjenjemera ndi kudabwa, amayiwo anatuluka ndipo anathawa ku mandako. Sananene china chilichonse kwa aliyense, chifukwa anachita mantha.

[Mipukutu yoyambirira ndi maumboni akale mulibe vesi 9 mpaka 20.]

Yesu Aonekera kwa Mariya Magadalena

9Yesu atauka kwa akufa mmawa pa tsiku loyamba la Sabata, anayamba kuonekera kwa Mariya Magadalena, amene anatulutsa mwa iye ziwanda zisanu ndi ziwiri. 10Iye anapita ndi kukawawuza amene anali ndi Yesu, amene ankakhuza maliro ndi kulira. 11Atamva kuti Yesu ali moyo ndikuti amuona, iwo sanakhulupirire.

Yesu Aonekera kwa Ophunzira Awiri

12Zitatha izi Yesu anaonekera mʼmaonekedwe ena kwa awiri a iwo amene anali ku dera la ku mudzi. 13Iwo anabwerera ndi kudzawawuza enawo; koma iwo sanakhulupirirebe.

Yesu Ayankhula kwa Ophunzira Khumi ndi Mmodzi

14Pambuyo pake Yesu anaonekera kwa khumi ndi mmodziwo pamene ankadya; anawadzudzula chifukwa chopanda chikhulupiriro ndi kukanitsitsa kwawo kuti akhulupirire amene anamuona Iye atauka.

15Anati kwa iwo, “Pitani mʼdziko lonse lapansi ndipo mukalalikire Uthenga Wabwino kwa zolengedwa zonse. 16Aliyense amene akakhulupirire nabatizidwa adzapulumuka, koma amene sakakhulupirira adzalangidwa. 17Tsono zizindikiro izi zidzawatsata amene adzakhulupirira: Mʼdzina langa adzatulutsa ziwanda; adzayankhula malilime atsopano; 18adzanyamula njoka ndi manja awo; ndipo pamene adzamwa mankhwala akupha, sadzawapweteka nʼpangʼonongʼono pomwe; adzasanjika manja awo pa anthu odwala ndipo odwalawo adzachira.”

Yesu Apita Kumwamba

19Ambuye Yesu atatha kuyankhulana nawo, anatengedwa kupita kumwamba ndipo anakhala kudzanja lamanja la Mulungu. 20Pamenepo ophunzira aja anapita ndi kukalalikira ponseponse, ndipo Ambuye anagwira nawo ntchito pamodzi, ndipo anatsimikizira mawuwo ndi zizindikiro zimene ankachita.