馬可福音 14 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

馬可福音 14:1-72

謀害耶穌

1再過兩天就是逾越節和除酵節,祭司長和律法教師正暗暗地找機會拘捕、殺害耶穌。

2他們說:「我們不能在節期那天下手,以免在百姓中引起騷亂。」

耶穌受膏

3耶穌在伯大尼村患過痲瘋病的西門家裡吃飯,有個女人帶了一瓶極貴重的純哪噠香膏進來,把玉瓶打破,將香膏倒在耶穌頭上。 4有些人生氣地彼此議論說:「為什麼這樣浪費? 5這瓶香膏可以賣三百多個銀幣14·5 三百多個銀幣」相當於當時人們一年的工錢。來賙濟窮人。」他們就責備那女人。

6耶穌說:「隨她吧!何必為難她呢?她在我身上做的是一件美事。 7因為你們身邊總會有窮人,你們隨時都可以幫助他們,可是你們身邊不會總有我。 8她做了自己能做的。她是為我的安葬做準備,提前用香膏抹了我的身體。 9我實在告訴你們,無論福音傳到世界哪個角落,人們都會傳揚這女人的事蹟,紀念她。」

猶大出賣耶穌

10十二門徒當中的加略猶大去見祭司長,要把耶穌出賣給他們。 11他們聽了喜出望外,答應給他酬金。於是猶大伺機出賣耶穌。

最後的晚餐

12除酵節的第一天,就是宰殺逾越節羔羊的那天,門徒問耶穌:「我們該到什麼地方為你準備逾越節的晚餐呢?」

13耶穌就派了兩個門徒,並囑咐他們:「你們進城會看到一個人帶著一瓶水迎面而來,你們就跟著他。 14他進哪一家,你們也跟著進去,對那家的主人說,『我們的老師問你,祂的客房在哪裡,祂要和門徒在裡面吃逾越節的晚餐。』 15主人會帶你們到樓上一間布置整齊的大房間,你們就在那裡準備吧。」

16兩個門徒出去,進了城,所遇見的果然和耶穌所說的一樣。他們預備了逾越節的晚餐。

17傍晚時分,耶穌帶著十二門徒來了。 18用餐的時候,耶穌說:「我實在告訴你們,你們中間有一個人要出賣我,他現在正和我同桌吃飯。」

19他們聽了都感到不安,一個一個地問耶穌:「不是我吧?」 20耶穌說:「是你們十二個人中的一個,他現在正和我一起在盤子裡蘸餅吃。 21人子一定會受害,正如聖經的記載,但出賣人子的人有禍了,他還不如不生在這世上!」

22他們吃的時候,耶穌拿起餅來,祝謝後,便掰開,分給門徒,說:「拿去吃吧!這是我的身體。」 23接著又拿起杯來,祝謝後,遞給他們,他們都喝了。 24耶穌說:「這是我為萬人所流的立約之血。 25我實在告訴你們,從今天起,一直到我在上帝的國喝新酒的那天之前,我不會再喝這葡萄酒。」

26他們唱完詩歌,就出門去了橄欖山。

預言彼得不認主

27耶穌對他們說:「你們都要背棄我,因為聖經上說,

『我要擊打牧人,

羊群將四散。』

28但我復活後,要先你們一步去加利利。」

29彼得說:「即使所有人都背棄你,我也決不會背棄你!」

30耶穌說:「我實在告訴你,就在今天晚上雞叫兩次以前,你會三次不認我。」

31彼得鄭重地說:「就算要我跟你一起死,我也不會不認你。」其他門徒也都這樣說。

客西馬尼園的禱告

32他們到了客西馬尼園,耶穌對門徒說:「你們坐在這裡,我要去禱告。」

33於是耶穌帶著彼得雅各約翰向前走。祂覺得極其難過,非常傷痛, 34說:「我心裡非常憂傷,幾乎要死,你們留在這裡警醒。」 35耶穌往前走了不遠,俯伏在地禱告,如果可以,不要讓那時刻臨到祂。

36祂說:「阿爸,父啊,你無所不能,求你撤去此杯。然而,願你的旨意成就,而非我的意願。」

37祂回來,見他們都睡著了,就對彼得說:「西門,你在睡覺嗎?你不能警醒一時嗎? 38你們要警醒禱告,免得陷入誘惑。你們的心靈雖然願意,肉體卻很軟弱。」

39耶穌又去禱告,所祈求的跟上次一樣。 40祂回來時見他們又睡著了,因為他們睏得眼皮發沉,也不知道對祂說什麼。 41祂第三次禱告回來後,對他們說:「你們還在睡覺休息嗎?夠了,時候到了,看啊,人子要被出賣、交在罪人的手裡了。 42起來,我們走吧。看啊,出賣我的人已經來了!」

耶穌被捕

43耶穌還在說話的時候,十二門徒之一的猶大已帶了一群人拿著刀棍迎面而來。他們奉了祭司長、律法教師和長老之命來捉拿耶穌。 44出賣耶穌的猶大預先和他們定了暗號,說:「我親吻誰,誰就是耶穌,你們把祂抓起來,小心押走。」

45猶大隨即走到耶穌跟前說:「老師。」然後就親吻耶穌。 46其他人就下手捉拿耶穌。 47站在旁邊的一個門徒拔出刀朝大祭司的奴僕砍去,削掉了他一隻耳朵。

48耶穌問那群人:「你們像對付強盜一樣拿著刀棍來抓我嗎? 49我天天和你們在一起,在聖殿裡教導人,你們沒有來抓我。你們現在這樣做是要應驗聖經的話。」

50那時,門徒都撇下耶穌,各自逃命去了。 51只有一個身上披著一塊麻布的青年跟著耶穌。他們上去捉他, 52他丟了那塊麻布,赤身逃走了。

大祭司審問耶穌

53他們把耶穌押到大祭司那裡,眾祭司長、長老和律法教師都來了。 54那時彼得遠遠地跟著耶穌,一直來到大祭司的院子,與衛兵們坐在一起烤火。 55祭司長和全公會的人正在尋找證據控告耶穌,要定祂死罪,只是找不到。 56不少人作偽證控告祂,他們的證詞卻不一致。 57後來,有幾個人站起來作偽證說: 58「我們聽見祂說,『我要拆毀這座人手建造的聖殿,三天內不靠人力另造一座。』」 59即使這樣,他們的證詞也不一致。

60最後,大祭司在眾人面前站起來質問耶穌:「你不回答嗎?這些人作證控告你的是什麼呢?」

61耶穌還是沉默不語,什麼也不答。大祭司又問祂:「你是那當受稱頌者的兒子基督嗎?」 62耶穌說:「我是!將來你們要看見人子坐在全能上帝的右邊,駕著天上的雲降臨。」

63大祭司便撕裂衣服,說:「我們還需要什麼證人呢? 64你們聽見祂說褻瀆的話了,你們看怎麼辦?」他們都判祂死罪。

65有幾個人向祂吐唾沫,蒙上祂的眼睛,揮拳打祂,嘲笑祂說:「你說預言吧!」衛兵押祂下去時,也打祂。

彼得三次不認耶穌

66那時,彼得仍在院子裡,大祭司的一個婢女走過來, 67彼得在烤火,打量了他一番,說:「你也是那個拿撒勒人耶穌的同夥。」

68「我不知道也不明白你在說什麼!」彼得一邊否認,一邊躲到外院去。那時,雞叫了。

69一會兒,那婢女又看見彼得,就對旁邊的人說:「他是跟他們一夥的!」 70彼得又加以否認。

再過了一會兒,旁觀的人也指著彼得說:「你一定是跟他們一夥的,因為你也是加利利人!」

71彼得又賭咒又發誓,說:「我根本不認識你們說的這個人。」 72就在這時候,雞又叫了。彼得突然想起耶穌曾對他說:「在雞叫兩次以前,你會三次不認我」,忍不住痛哭起來。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 14:1-72

Yesu Adzozedwa ku Betaniya

1Tsopano panali patatsala masiku awiri okha kuti tsiku la Paska ndi Phwando la Buledi wopanda yisiti lifike, ndipo akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo ankafunafuna mpata woti amugwire Yesu ndi kumupha. 2Iwo anati, “Koma osati nthawi yaphwando, chifukwa anthu angachite chiwawa.”

3Pamene Iye anali mʼBetaniya, atakhala pa tebulo akudya mʼnyumba ya munthu wodziwika kuti Simoni wakhate, anabwera mayi ndi botolo la mafuta onunkhira amtengo wapamwamba opangidwa ndi nadi. Anaphwanya botololo nakhuthula mafutawo pa mutu wa Yesu.

4Ena mwa iwo amene analipo, anakwiya nati kwa wina ndi mnzake, “Chifukwa chiyani akuwononga mafuta onunkhirawa? 5Akanatheka kugulitsidwa ndi ndalama zambiri zoposa malipiro a pa chaka ndipo ndalamazo ndi kupatsa osauka.” Ndipo anamudzudzula iye mwaukali.

6Yesu anati, “Musiyeni, chifukwa chiyani mukumuvutitsa? Wandichitira Ine chinthu chabwino. 7Anthu osauka mudzakhala nawo nthawi zonse, ndipo mukhoza kuwathandiza nthawi iliyonse mungafune. Koma simudzakhala ndi Ine nthawi zonse. 8Wachita zimene akanatha. Wathira mafuta onunkhira pa thupi langa nthawi isanakwane kukonzekera kuyikidwa kwanga mʼmanda. 9Zoonadi, ndikuwuzani kuti kulikonse kumene Uthenga Wabwino udzalalikidwa pa dziko lonse, zimene wachitazi zidzanenedwa pomukumbukira iye.”

10Kenaka Yudasi Isikarioti, mmodzi mwa khumi ndi awiriwo, anapita kwa akulu a ansembe kuti akamupereke Yesu. 11Iwo anakondwa pakumva zimenezi ndipo analonjeza kumupatsa iye ndalama. Ndipo ankadikira mpata wabwino woti amupereke.

Mgonero wa Ambuye

12Pa tsiku loyamba la Phwando la Buledi wopanda yisiti, nthawi imene mwa mwambo inali ya kupha mwana wankhosa wa Paska, ophunzira a Yesu anafunsa Iye kuti, “Mufuna tipite kuti kumene tikakonzekere kuti mukadyere Paska?”

13Pamenepo anatumiza awiri mwa ophunzira ake, nawawuza kuti, “Pitani mu mzinda, ndipo mukakumana ndi mwamuna wonyamula mtsuko wa madzi. Kamutsatireni iye. 14Kawuzeni mwini nyumba imene iye akalowemo kuti, ‘Aphunzitsi akufunsa: kodi chili kuti chipinda changa cha alendo, kumene ndidyere Paska ndi ophunzira anga?’ 15Iye adzakuonetsani chipinda chachikulu chapamwamba, chokhala kale ndi zonse ndi chokonzedwa kale. Katikonzereni ife Paska kumeneko.”

16Ophunzirawo anachoka, napita mu mzindawo ndipo anakapeza zinthu monga mmene Yesu anawawuzira. Choncho anakakonza Paska.

17Ndipo kutada Yesu anafika ndi khumi ndi awiriwo. 18Pamene ankadya pa tebulo Iye anati, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti mmodzi wa inu adzandipereka, mmodzi amene akudya ndi Ine.”

19Iwo anamva chisoni, ndipo mmodzi ndi mmodzi anati kwa Iye, “Kodi ndine?”

20Iye anayankha kuti, “Ndi mmodzi mwa khumi ndi awirinu, amene akusunsa buledi mʼmbale pamodzi ndi Ine. 21Mwana wa Munthu adzapita monga momwe zinalembedwera za Iye. Koma tsoka kwa munthu amene adzapereka Mwana wa Munthu! Kukanakhala bwino kwa iye akanapanda kubadwa.”

22Pamene ankadya, Yesu anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema nagawira ophunzira ake nanena kuti, “Tengani, ili ndi thupi langa.”

23Kenaka anatenga chikho, nayamika nachipereka kwa iwo ndipo onse anamweramo.

24Iye anawawuza kuti, “Awa ndi magazi anga a pangano amene akhetsedwa chifukwa cha ambiri. 25Zoonadi, ndikuwuzani kuti sindidzamwanso kuchokera ku chipatso cha mphesa mpaka tsikulo pamene ndidzamwa chatsopano mu ufumu wa Mulungu.”

26Atayimba nyimbo, anapita ku phiri la Olivi.

Yesu Aneneratu zakuti Petro Adzamukana

27Yesu anati, “Nonse mudzandithawa, pakuti kwalembedwa:

“ ‘Kantha Mʼbusa,

ndipo nkhosa zidzabalalika.’

28Koma ndikadzauka, ndidzatsogola kupita ku Galileya.”

29Petro anati, “Ngakhale onse adzakuthaweni, ine sindidzatero.”

30Yesu anayankha kuti, “Zoona ndikukuwuza kuti lero lino, usiku uno, tambala asanalire kawiri, iweyo udzandikana katatu.”

31Koma Petro ananenetsa kuti, “Ngakhale kutakhala kufa nanu, ine sindidzakukanani.” Ndipo ena onse ananena chimodzimodzi.

Mu Getsemani

32Ndipo anapita ku malo otchedwa Getsemani, ndipo Yesu anati kwa ophunzira ake, “Khalani pano pamene Ine ndi kupemphera.” 33Iye anatenga Petro, Yakobo ndi Yohane, ndipo anayamba kumva chisoni kwambiri ndi kuvutika mu mtima. 34Iye anawawuza kuti, “Moyo wanga wagwidwa ndi chisoni chofa nacho. Khalani pano ndipo musagone.”

35Atapita patsogolo pangʼono, anagwa pansi ndi kupemphera kuti ngati ndi kotheka oralo limupitirire. 36Iye anati, “Abba, Atate, zinthu zonse ndi zotheka ndi Inu. Chotsereni chikhochi. Komabe chitani zimene Inu mukufuna, osati zimene Ine ndikufuna.”

37Kenaka anabwerera kwa ophunzira ake ndipo anawapeza akugona, Iye anati kwa Petro, “Simoni, kodi uli mtulo? Kodi simukanatha kukhala maso kwa ora limodzi? 38Khalani tcheru ndi kupemphera kuti musalowe mʼmayesero. Mzimu ukufuna, koma thupi ndi lofowoka.”

39Kenakanso anachoka ndi kukapemphera chimodzimodzi. 40Iye atabwerera, anawapezanso akugona, chifukwa mʼmaso mwawo munadzaza tulo. Iwo sanadziwe choti anene kwa Iye.

41Atabweranso kachitatu, anawafunsa kuti, “Kodi mukugonabe ndi kupumula? Pakwana! Nthawi yafika. Taonani, Mwana wa Munthu akuperekedwa mʼmanja mwa anthu ochimwa. 42Nyamukani! Tiyeni tizipita! Uyu wondipereka Ine wafika!”

Amugwira Yesu

43Iye akuyankhulabe, Yudasi, mmodzi mwa khumi ndi awiriwo, anatulukira. Anali ndi gulu la anthu litanyamula malupanga ndi zibonga, otumidwa ndi akulu a ansembe, aphunzitsi amalamulo, ndi akuluakulu.

44Tsopano womupereka anapangana chizindikiro ndi iwo kuti: “Amene ndikapsompsone ndi iyeyo; mukamugwire ndi kumutenga ali womangidwa.” 45Atapita kwa Yesu nthawi yomweyo, Yudasi anati, “Aphunzitsi,” ndipo anapsompsona. 46Anthu anamugwira Yesu ndi kumumanga. 47Kenaka mmodzi wa iwo amene anayima pafupipo anatulutsa lupanga lake nakhapa wantchito wa wamkulu wa ansembe, nʼkudula khutu lake.

48Yesu anati, “Kodi Ine ndikutsogolera gulu lowukira, kuti mubwera ndi malupanga ndi zibonga kudzandigwira? 49Tsiku ndi tsiku ndinali ndi inu, kuphunzitsa mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, koma inu simunandigwire. Koma malemba ayenera kukwaniritsidwa.” 50Pamenepo ophunzira ake onse anathawa namusiya yekha.

51Mnyamata wamngʼono amene anangofundira nsalu yokha, wopanda chovala ankamutsatira Yesu. Atamugwira, 52anathawa wamaliseche kusiya nsalu yake mʼmbuyo.

Yesu ku Bwalo la Milandu

53Anamutengera Yesu kwa mkulu wa ansembe, ndipo akulu a ansembe, akuluakulu ndi aphunzitsi amalamulo anasonkhana pamodzi. 54Petro anamutsatira ali patali, mpaka ku bwalo la mkulu wa ansembe. Kumeneko anakhala pansi ndi alonda namawotha moto.

55Akulu a ansembe ndi onse olamulira a Ayuda ankafunafuna umboni womutsutsa Yesu kuti amuphe, koma sanapeze wina uliwonse. 56Ambiri anamunenera Iye maumboni abodza, koma maumboni awo sanagwirizane.

57Kenaka ena anayimirira namunenera umboni wonama womutsutsa Iye kunena kuti, 58“Tamumva akunena kuti, ‘Ndidzawononga Nyumba ya Mulungu iyi yopangidwa ndi anthu ndipo mʼmasiku atatu ndidzamanga ina, osati yopangidwa ndi munthu.’ ” 59Ngakhale iwonso umboni wawo sunagwirizane.

60Kenaka mkulu wa ansembe anayimirira pakati pawo namufunsa Yesu kuti, “Kodi suyankha? Kodi umboni uwu ndi wotani umene anthu akukuchitira?” 61Koma Yesu anakhala chete ndipo sanayankhe.

Mkulu wa ansembe anabwereza kumufunsa Iye kuti, “Kodi ndiwe Khristu Mwana wa Wodalitsikayo?”

62Yesu anati, “Ndine, ndipo mudzaona Mwana wa Munthu atakhala kudzanja lamanja la Wamphamvuzonse ndipo akubwera mʼmitambo ya kumwamba.”

63Mkulu wa ansembe anangʼamba zovala zaunsembe zake. Iye anafunsa kuti, “Chifukwa chiyani tikufuna mboni zinanso? 64Mwamva mwanowo. Muganiza chiyani?”

Onse anavomereza kuti ndi woyenera imfa. 65Kenaka ena anayamba kumulavulira malovu; anamumanga mʼmaso, namumenya ndi zibakera ndipo anati, “Nenera!” Ndipo asilikali anamutenga namumenya.

Petro Akana Yesu

66Petro ali chakumunsi kwa bwalo la milandu, mmodzi wa atsikana a ntchito a mkulu wa ansembe anabwera. 67Ataona Petro akuwotha moto, anamuyangʼanitsitsa.

Iye anati, “Iwenso unali pamodzi ndi Mnazareti, Yesu.”

68Koma iye anakana nati, “Sindikudziwa kapena kumvetsetsa zimene ukuyankhula.” Ndipo anachoka napita ku chipata.

69Pamene mtsikana wantchitoyo anamuona iye, anatinso kwa iwo amene anayimirira pomwepo, “Munthu uyu ndi mmodzi mwa iwo.” 70Anakananso kachiwiri.

Patapita kanthawi pangʼono, amene anayimirira pafupi anati kwa Petro, “Zoonadi ndiwe mmodzi wa iwo, pakuti ndiwe mu Galileya.”

71Iye anayamba kudzitemberera, nalumbira kuti, “Sindimudziwa munthu ameneyu.”

72Nthawi yomweyo tambala analira kachiwiri. Pamenepo Petro anakumbukira mawu amene Yesu ananena anamuwuza kuti, “Tambala asanalire kawiri, iwe udzandikana katatu.” Ndipo iye anasweka mtima nayamba kulira.