雅歌 8 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

雅歌 8:1-14

1如果你是我的同胞兄弟就好了。

這樣,在外頭遇見你,

我也可以親吻你,

沒有人會取笑我。

2我可以把你帶進我母親的家——她教養了我。

我要給你喝石榴汁釀的醇酒。

3你的左手扶著我的頭,

右手緊抱著我。

4耶路撒冷的少女啊,

我懇求你們,

不要叫醒或驚動愛情,

等它自發吧。

耶路撒冷的少女:

5那從曠野上來、靠在良人身旁的是誰呢?

女子:

我在蘋果樹下喚醒你,

你母親在那裡懷你養你,

為你受生產之苦。

6請把我印在你的心上,

刻在你的手臂上,

因為愛情如死亡一般堅固,

嫉妒像陰間一樣殘酷,

它燃起的火焰是燒滅一切的烈火。

7愛情,大水不能熄滅,

江河不能淹沒。

若有人想傾其家財買愛情,

必遭唾棄。

女子的兄長:

8我們有一個小妹,

她的胸脯還沒有發育。

若有人來提親,

我們該怎麼辦?

9她若是牆,

我們要在上面建造銀塔;

她若是門,

我們要用香柏木板圍護她。

女子:

10我是一面牆,

雙乳像城樓,

我在他眼中像找到平安的人。

11所羅門巴力·哈們有一個葡萄園,

他把葡萄園租給農夫,

租金是每人一千塊銀子。

12我的葡萄園,我自己作主。

所羅門啊,你的一千塊銀子自己留著,

二百塊銀子給管果園的人。

男子:

13你這住在園中的人啊,

同伴們都在聆聽你的聲音,

求你讓我也聽見吧!

女子:

14我的良人啊,

願你像香草山上的羚羊和小鹿,

快快來到我身邊!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 8:1-14

1Ukanakhala kuti ndiwe mlongo wanga,

amene anayamwa mawere a amayi anga!

Ndikanakumana nawe pa njira,

ndikanakupsompsona,

ndipo palibe wina aliyense akanandinyoza.

2Ndikanakutenga

ndi kukulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,

amayi amene anandiphunzitsa,

ndikanakupatsa vinyo wotsekemera kuti umwe,

zotsekemera za makangadza.

3Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere

ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.

4Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani:

musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

Abwenzi

5Kodi ndani uyo akutuluka ku chipululuyo,

atatsamira wokondedwa wakeyo?

Mkazi

Ndinakudzutsa pa tsinde pa mtengo wa apulosi,

pamenepo ndi pamene amayi anachirira,

pamenepo ndi pamene wokubereka anamva ululu pokubala iweyo.

6Undiyike pamtima pako ngati chidindo,

ngati chidindo cha pa dzanja lako;

pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa,

nsanje ndiyaliwuma ngati manda.

Chikondi chimachita kuti lawilawi

ngati malawi a moto wamphamvu.

7Madzi ochuluka sangachizimitse chikondi,

mitsinje singachikokolole chikondicho.

Ngati wina apereka chuma chonse

cha mʼnyumba mwake chifukwa cha chikondi,

adzangonyozeka nazo kotheratu.

Abwenzi

8Ife tili naye mlongo wathu wamngʼono,

koma alibe mawere,

kodi tidzamuchitira chiyani mlongo wathuyu

pa tsiku limene adzamufunsire?

9Ngati iye ndi khoma,

tidzamumangira nsanja ya siliva.

Ngati iye ndi chitseko,

tidzamutchinga ndi matabwa a mkungudza.

Mkazi

10Ine ndili ngati khoma,

ndipo mawere anga ndi nsanja zake.

Tsono mʼmaso mwa bwenzi langa

ndine wobweretsa mtendere.

11Solomoni anali ndi munda wampesa ku Baala-Hamoni;

iyeyo anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi,

aliyense mwa iwo ankayenera kupereka

ndalama zasiliva 1,000 mʼmalo mwa zipatso zake.

12Koma munda wanga wampesa ndi wangawanga ndiponso wa ine ndekha.

Iwe Solomoni, khala nazo ndalama zasiliva 1,000

ndipo ndalama zasiliva 200 ndi za amene akusamalira mundawo.

Mwamuna

13Iwe amene umakhala mʼminda

uli pamodzi ndi anzako,

ndilole kuti ndimve liwu lako!

Mkazi

14Fulumira wokondedwa wanga,

ndipo ukhale ngati gwape

kapena mwana wa mbawala

wothamanga mʼmapiri mʼmene mumamera mbewu zokometsera chakudya.