雅歌 7 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

雅歌 7:1-13

1我的公主啊,你的雙腳配上鞋子多麼美啊!

你美玉般圓潤的腿是巧匠的傑作。

2你的肚臍好像圓杯,

不缺調和的酒。

你的腰好比一堆麥子,

四周圍繞著百合花。

3你的胸脯好像一對孿生的小鹿。

4你的脖子如象牙塔,

眼睛好像希實本境內巴特·拉並門旁的水池。

你的鼻子好像眺望大馬士革黎巴嫩塔。

5你的頭如同迦密山,

你的秀髮好像紫黑色的緞子,

君王的心被你的縷縷青絲繫住。

6我的愛人,你是多麼美麗,

多麼討人喜愛,令人陶醉啊!

7你亭亭玉立如同棕櫚樹,

胸脯就像樹上的果串。

8我要攀上這棵樹,

握住樹上的果子。

願你的胸脯像葡萄串,

你的氣息如蘋果般清香。

9你的親吻像上好的美酒。

女子:

願美酒流入我良人的口中,

緩緩注入他陶醉的唇齒間。

10我屬於我的良人,

是他所戀慕的。

11我的良人,來吧!

讓我們到田間去,

在村莊裡住宿吧。

12我們清晨去葡萄園,

看看葡萄樹是否已經發芽開花,

石榴樹是否正在開花。

我要在那裡把我的愛情獻給你。

13那裡風茄飄香,

門口有各樣上好的新陳美果。

我的良人,這都是我為你存留的。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 7:1-13

1Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola

mu nsapato wavalazo!

Ntchafu zako nʼzowumbika bwino ngati miyala yamtengowapatali,

ntchito ya manja ya mmisiri waluso.

2Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino

chimene nthawi zonse ndi chodzaza ndi vinyo.

Chiwuno chako ndi choningʼa ngati mtolo wa tirigu

utazunguliridwa ndi maluwa okongola.

3Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala,

ngati mphoyo zamapasa.

4Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu.

Maso ako ali ngati mayiwe a ku Hesiboni,

amene ali pafupi ndi chipata cha Bati Rabimu.

Mphuno yako ili ngati nsanja ya ku Lebanoni,

yoyangʼana ku Damasiko.

5Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli.

Tsitsi lako lili ngati nsalu yakuda yaufumu;

mfumu yakopeka ndi maonekedwe ake okongola.

6Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa,

iwe wokondedwa, namwali wokondweretsawe!

7Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa,

ndipo mawere ako ali ngati phava la zipatso.

8Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa;

ndidzathyola zipatso zake.”

Mawere ako ali ngati maphava a mphesa,

fungo la mpweya wako lili ngati ma apulosi,

9ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri.

Mkazi

Tsono vinyo ameneyu amuthirire wachikondi wanga,

ayenderere bwino pa milomo yake ndi mano ake.

10Wokondedwayo ine ndine wake,

ndipo chilakolako chake chili pa ine.

11Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi,

tikagone ku midzi.

12Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa,

tikaone ngati mitengo ya mpesa yayamba kuphukira,

ngati maluwa ake ayamba kuoneka,

komanso ngati makangadza ayamba kuonetsa maluwa.

Kumeneko ndidzakuonetsa chikondi changa.

13Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino,

ndipo pa khomo pathu pali zipatso zonse zokoma,

zatsopano ndi zakale zomwe,

zimene ndakusungira wokondedwa wanga.