詩篇 50 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 50:1-23

第 50 篇

真正的敬拜

亞薩的詩。

1從日出之地到日落之處,

大能的上帝耶和華召喚世人。

2上帝的光輝從完美的錫安發出。

3我們的上帝來臨,

並非悄然無聲,

祂前面有烈火燃燒,

周圍有暴風怒吼。

4祂召喚天地,

為要審判祂的子民。

5祂說:「把我忠心的子民——那些藉著獻祭和我立約的人招聚到我這裡。」

6諸天宣揚上帝的公義,

因為祂是審判官。(細拉)

7祂說:「我的子民啊,聽我說!

以色列啊,我要指控你!

我是上帝,是你的上帝。

8我責怪你,不是因為你的祭物,

也不是因為你經常獻給我的燔祭。

9我不需要你棚裡的公牛和圈裡的山羊,

10因為林中的百獸是我的,

群山上的牲畜是我的。

11山中的飛鳥和田野的動物都是我的。

12就是我餓了,也不用告訴你,

因為世界和其中的一切都是我的。

13難道我吃公牛的肉,

喝山羊的血嗎?

14你要向上帝獻上感恩祭,

向至高者恪守諾言,

15在患難中呼求我,

我必拯救你,你必尊崇我。」

16但上帝對惡人說:

「你怎能背誦我的律法,

談論我的約?

17你憎惡我的管教,

把我的話拋在腦後。

18你見了盜賊就與他同流合污,

又喜歡與淫亂的人交往。

19你滿口惡言,謊話連篇,

20肆意譭謗自己的同胞兄弟。

21我對你的所作所為默然不語,

你就以為我與你是同道。

現在我要責備你,

當面指出你的罪狀。

22忘記上帝的人啊,

你們要省察,

免得我毀滅你們,

那時誰也救不了你們。

23向我獻上感恩就是尊崇我,

我必拯救走正路的人。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 50:1-23

Salimo 50

Salimo la Asafu.

1Wamphamvuyo, Yehova Mulungu,

akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi

kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.

2Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri

Mulungu akuwala.

3Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete;

moto ukunyeketsa patsogolo pake,

ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho

4Iye akuyitanitsa zamumlengalenga

ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.

5Mundisonkhanitsire okhulupirika anga,

amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.

6Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake,

pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.

7Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula,

iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa;

ndine Mulungu, Mulungu wako.

8Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako,

kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.

9Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako

kapena mbuzi za mʼkhola lako,

10pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga

ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.

11Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri

ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.

12Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani,

pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.

13Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna

kapena kumwa magazi a mbuzi?

14“Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu,

kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.

15Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso;

Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”

16Koma kwa woyipa, Mulungu akuti,

“Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga

kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?

17Iwe umadana ndi malangizo anga

ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.

18Ukaona wakuba umamutsatira,

umachita maere ako pamodzi ndi achigololo

19Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa

ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.

20Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako

ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.

21Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete;

umaganiza kuti ndine wofanana nawe

koma ndidzakudzudzula

ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.

22“Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu

kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:

23Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza,

ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse

chipulumutso cha Mulungu.”