詩篇 14 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 14:1-7

第 14 篇

世人的邪惡

大衛的詩,交給樂長。

1愚昧人心裡想:「沒有上帝。」

他們全然敗壞,行為邪惡,

無人行善。

2耶和華從天上俯視人間,

看有沒有明智者,

有沒有尋求上帝的人。

3人們都偏離正路,

一同墮落;

沒有人行善,

一個也沒有!

4惡人吞吃我的百姓如同吃飯,

他們不求告耶和華。

難道他們無知嗎?

5但他們終必充滿恐懼,

因為上帝站在義人當中。

6你們惡人使困苦人的計劃落空,

但耶和華是他們的避難所。

7以色列的拯救來自錫安

耶和華救回祂被擄的子民時,

雅各要歡欣,以色列要快樂。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 14:1-7

Salimo 14

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Chitsiru chimati mu mtima mwake,

“Kulibe Mulungu.”

Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa;

palibe amene amachita zabwino.

2Yehova kumwamba wayangʼana pansi,

kuyangʼana anthu onse

kuti aone ngati alipo wina wanzeru,

amene amafunafuna Mulungu.

3Onse atembenukira kumbali,

onse pamodzi asanduka oyipa;

palibe amene amachita zabwino,

palibiretu ndi mmodzi yemwe.

4Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse?

Akudya anthu anga ngati chakudya chawo

ndipo satamanda Yehova?

5Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu,

pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.

6Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka,

koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.

7Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni!

Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake,

Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!