約翰一書 3 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

約翰一書 3:1-24

上帝的兒女

1你們看,父上帝何等愛我們,稱我們為祂的兒女!我們也實在是祂的兒女,世人之所以不認識我們,是因為他們不認識父上帝。 2親愛的弟兄姊妹,我們現在是上帝的兒女,將來如何還未顯明。但我們知道,當主顯現的時候,我們必會像祂,因為我們必見到祂的本體。 3凡心存這種盼望的人都會自潔,因為主是聖潔的。

4犯罪的人都違背上帝的律法,違背上帝的律法就是罪。 5你們知道,耶穌降世是為了除掉人的罪,祂自己並沒有罪。 6住在祂裡面的人不會一直犯罪;一直犯罪的人既沒見過祂也不認識祂。

7孩子們,不要受人迷惑,要知道行義的才是義人,正如主是公義的。 8一直犯罪的人是屬魔鬼的,因為魔鬼從起初便犯罪,但上帝兒子的顯現是為了摧毀魔鬼的工作。 9從上帝生的人不會繼續犯罪,因為他裡面有上帝的生命3·9 上帝的生命」希臘文是「上帝的種子」。。他不能犯罪,因為他是從上帝生的。 10這樣,就可以看出誰是上帝的兒女,誰是魔鬼的兒女。凡不按公義行事、不愛弟兄姊妹的,都不是上帝的兒女。

彼此相愛

11我們應當彼此相愛,這是你們起初聽見的信息。 12不要步該隱的後塵。他屬於那惡者,殺害了自己的弟弟。他為什麼要殺害自己的弟弟呢?因為他的行為邪惡,而他弟弟秉行公義。

13弟兄姊妹,世人若恨你們,不要驚奇。 14我們因愛弟兄姊妹,便知道自己已經出死入生了。不愛弟兄姊妹的,仍然陷在死亡中。 15恨弟兄姊妹的就是殺人的,你們知道殺人的沒有永生。 16主耶穌為我們捨命,我們由此便知道什麼是愛,我們也應當為弟兄姊妹捨命。 17如果一個豐衣足食的人看見貧窮的弟兄姊妹,卻毫無憐憫之心,怎能說他愛上帝呢? 18所以,孩子們啊,不要單在口頭上說愛人,總要以真誠的行動表現出來。

19-20這樣,我們必知道自己屬於真理,即使我們心中自責,也可以在上帝面前心安,因為上帝比我們的心大,祂知道一切。

21親愛的弟兄姊妹,我們若能凡事問心無愧,就可以在上帝面前坦然無懼。 22這樣,我們無論向上帝祈求什麼,都必得到,因為我們遵守祂的命令,做祂喜悅的事。 23其實上帝的命令是:我們要信祂兒子耶穌基督的名,遵照祂的命令彼此相愛。 24遵行上帝命令的人就住在上帝裡面,上帝也住在他裡面。我們藉著上帝賜給我們的聖靈知道:祂住在我們裡面。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Yohane 3:1-24

1Taonani kukula kwake kwa chikondi chimene Atate anatikonda nacho, kuti titchedwe ana a Mulungu! Ndipo nʼchimene ife tili! Nʼchifukwa chake dziko lapansi silitidziwa chifukwa silinamudziwe Iye. 2Abale okondedwa, tsopano ndife ana a Mulungu, ndipo sichinaoneke chimene tidzakhala. Koma tikudziwa kuti Yesu akadzaonekera, tidzafanana naye, pakuti tidzamuona Iyeyo monga momwe alili. 3Aliyense amene ali ndi chiyembekezo ichi mwa Iye adziyeretse yekha, monga Iye ali woyera.

4Aliyense amene amachimwa amaphwanya lamulo; pakuti tchimo ndi kuphwanya lamulo. 5Koma inu mukudziwa kuti Yesu anabwera kuti adzachotse machimo athu. Ndipo mwa Iye mulibe tchimo. 6Aliyense wokhala mwa Khristu sachimwa. Aliyense amene amachimwa sanamuone kapena kumudziwa.

7Ana okondedwa, musalole kuti aliyense akusocheretseni. Munthu amene amachita chilungamo ndi wolungama, monga Khristu ali wolungama. 8Iye amene amachimwa ndi wa Satana, chifukwa mdierekezi wakhala akuchimwa kuyambira pa chiyambi. Mwana wa Mulungu anaonekera kuti awononge ntchito za mdierekezi. 9Aliyense amene ndi mwana wa Mulungu, sachimwirachimwira, popeza mbewu ya Mulungu ili mwa iye, sangathe kuchimwa, chifukwa ndi mwana wa Mulungu. 10Mmenemu ndi mmene timadziwira ana a Mulungu ndi amene ali ana a mdierekezi. Aliyense amene sachita chilungamo si mwana wa Mulungu; ngakhalenso amene sakonda mʼbale wake.

Kukondana Wina ndi Mnzake

11Uthenga umene munawumva kuyambira pachiyambi ndi uwu: Tizikondana wina ndi mnzake. 12Musakhale ngati Kaini, amene anali wa woyipayo ndipo anapha mʼbale wake. Nanga anamupha chifukwa chiyani? Chifukwa zochita zake zinali zoyipa ndipo zochita za mʼbale wake zinali zolungama. 13Abale anga, musadabwe ngati dziko lapansi lidana nanu. 14Ife tikudziwa kuti tinatuluka mu imfa ndi kulowa mʼmoyo, chifukwa timakonda abale athu. Aliyense amene sakonda mʼbale wake akanali mu imfa. 15Aliyense amene amadana ndi mʼbale wake ndi wakupha, ndipo inu mukudziwa kuti wopha anthu mwa iye mulibe moyo wosatha.

16Mmene timadziwira chikondi chenicheni ndi umu: Yesu anapereka moyo wake chifukwa cha ife. Ndipo nafenso tiyenera kupereka miyoyo yathu chifukwa cha abale athu. 17Ngati wina ali ndi chuma ndipo nʼkuona mʼbale wake akusowa, koma wosamvera chisoni, kodi mwa iyeyo muli chikondi cha Mulungu? 18Ana okondedwa, chikondi chathu chisakhale cha pakamwa pokha koma cha ntchito zathu ndi mʼchoonadi. 19Pamenepo tidzadziwa kuti tili pa choonadi ndipo tidzakhala okhazikika mtima pamaso pa Mulungu, 20nthawi zonse pamene mtima wathu utitsutsa. Pakuti Mulungu ndi wamkulu kuposa mitima yathu ndipo Iye amadziwa zonse.

21Anzanga okondedwa, ngati mitima yathu sikutitsutsa, tili nako kulimbika mtima pamaso pa Mulungu. 22Ndipo timalandira chilichonse chimene tichipempha kwa Iye, chifukwa timamvera malamulo ake ndi kuchita zimene zimamukondweretsa. 23Ndipo lamulo lake ndi ili: kukhulupirira dzina la Mwana wake, Yesu Khristu, ndi kukondana wina ndi mnzake monga Iye anatilamulira. 24Iwo amene amamvera malamulo ake amakhala mwa Iye, ndipo Iye amakhala mwa iwo. Ndipo mmenemu ndi momwe timadziwira kuti Iye akukhala mwa ife. Timadziwa mwa Mzimu Woyera amene anatipatsa.