箴言 9 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

箴言 9:1-18

智慧和愚昧

1智慧建造她的房屋,

鑿出七根柱子。

2她宰了牲口,

調了美酒,

設了宴席,

3派婢女出去邀請賓客,

自己在城中高處呼喊:

4「愚昧人啊,到這裡來吧!」

她又對無知者說:

5「來吃我做的飯,

嚐嚐我調的酒吧!

6你們要拋棄愚昧,就能存活,

要轉向悟性之道。」

7糾正嘲諷者,必自招羞辱;

責備惡人,必自招傷害。

8不要責備嘲諷者,免得他恨你;

要責備智者,他必愛你。

9教導智者,他就更有智慧;

指教義人,他就更有見識。

10智慧始於敬畏耶和華,

認識至聖者便是明智。

11智慧可增添你的年日,

加添你的壽數。

12人有智慧,自得益處;

人好嘲諷,自食惡果。

13愚昧的女人喧嚷,蒙昧,無知。

14她坐在自己的家門口,

坐在城中高處的座位上,

15招呼著行色匆匆的過客:

16「愚昧人啊,到這裡來吧!」

她又對無知者說:

17「偷喝的水甜,偷吃的餅香。」

18他們卻不知她那裡鬼影幢幢,

她的客人已落在陰間的深處。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 9:1-18

Za Nzeru ndi Uchitsiru

1Nzeru inamanga nyumba yake;

inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.

2Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake;

inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.

3Nzeruyo inatuma adzakazi ake,

kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,

4“Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!”

Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,

5“Bwerani, dzadyeni chakudya changa

ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.

6Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo;

yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”

7Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo;

aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.

8Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe;

dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.

9Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru;

ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.

10Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru;

kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.

11Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka,

ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.

12Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa;

ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.

13Uchitsiru ndi mkazi waphokoso,

wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.

14Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake,

pamalo aatali a mu mzinda,

15kuti aziyitana anthu ongodutsa,

amene akunka nayenda njira zawo.

16Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,”

ndipo kwa wopanda nzeru amati,

17“Madzi akuba ndiye amatsekemera;

chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”

18Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko,

ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya.