箴言 24 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

箴言 24:1-34

1不要羡慕惡人,

不要嚮往與他們為友;

2因為他們心裡圖謀暴行,

口中談論惡事。

3家靠智慧而建立,

靠悟性而穩固,

4藉知識而充滿各種珍寶。

5智者充滿能力,

哲士力上加力。

6出征打仗,要憑智謀;

謀士眾多,勝券在握。

7智慧對愚人高不可及,

他在城門口沉默不語。

8圖謀作惡的必被稱為陰謀家。

9愚人的計謀是罪惡,

人人都厭惡嘲諷者。

10逆境中喪膽的是弱者。

11被拉去屠殺的,你要搶救;

踉蹌受死的,你要攔阻。

12不要推說自己毫不知情,

鑒察人心的主洞悉一切,

保守你生命的上帝知情,

祂必按你的行為報應你。

13孩子啊,你要吃美好的蜂蜜,

蜂房滴下的蜜甘甜可口。

14智慧同樣使你的心靈甘甜;

你若找到智慧,前途必光明,

盼望也不會幻滅。

15不要像惡人一樣暗算義人,

破壞他的家。

16因為義人跌倒七次也必起來,

惡人卻被災禍擊垮。

17仇敵跌倒,不要幸災樂禍;

仇敵敗落,不要心裡歡喜。

18否則,耶和華看見會不悅,

不再向仇敵發烈怒。

19不要因惡人而憤憤不平,

也不要羡慕歹徒;

20因為惡人毫無前途,

惡人的燈終必熄滅。

21孩子啊,要敬畏耶和華和君王,

不要跟反復無常之徒為伍。

22因為災禍必驟然臨到他們,

誰知道耶和華和君王如何毀滅他們?

其他智言

23以下也是智者的箴言:

判案時偏袒實為不善。

24判惡人無罪的,

必遭萬人咒詛,

為列國痛恨。

25責備惡人的必有歡樂,

美好的福氣必臨到他。

26誠實的回答如同友好的親吻。

27要安排好外面的事,

把田間的工作準備妥當,

然後建造房屋。

28別無故作證害鄰舍,

也不可撒謊欺騙人。

29不可說:「別人怎樣待我,

我就怎樣待他;

我要照他所做的報復他。」

30我走過懶惰人的田地和無知者的葡萄園,

31那裡荊棘遍地,

刺草叢生,

石牆倒塌。

32我仔細思想所見之事,

領悟到一個教訓:

33再睡一會兒,

打個盹兒,

抱著手躺一會兒,

34貧窮必像強盜一樣臨到你,

缺乏必像武士一樣撲向你。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 24:1-34

1Usachitire nsanje anthu oyipa,

usalakalake kuti uzikhala nawo,

2pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa,

ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.

3Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru,

ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;

4Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake

ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.

5Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri,

ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.

6Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo.

Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.

7Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru;

chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.

8Amene amakonzekera kuchita zoyipa

adzatchedwa mvundulamadzi.

9Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo,

ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.

10Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti

mphamvu yako ndi yochepadi!

11Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe;

uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.

12Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,”

kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi?

Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi?

Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?

13Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino;

uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.

14Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako;

ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo,

ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.

15Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa.

Usachite nayo nkhondo nyumba yake;

16paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso.

Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.

17Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako.

Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.

18Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo,

angaleke kukwiyira mdaniyo.

19Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa

kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,

20paja munthu woyipa alibe tsogolo.

Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.

21Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu,

ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,

22awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi.

Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?

Malangizo Enanso a Anthu Anzeru

23Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa:

Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:

24Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,”

anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.

25Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino

ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.

26Woyankhula mawu owona

ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.

27Ugwiriretu ntchito zako zonse,

makamaka za ku munda

ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.

28Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa,

kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.

29Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine;

ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”

30Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi

ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.

31Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga,

mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa,

ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.

32Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga

ndipo ndinatolapo phunziro ili:

33Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,”

kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”

34umphawi udzafika pa iwe ngati mbala

ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.