箴言 11 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

箴言 11:1-31

1耶和華憎惡騙人的天平,

喜愛公平的法碼。

2傲慢帶來羞辱,

謙卑者有智慧。

3正直人靠誠實引導,

奸詐者被奸詐毀滅。

4在降怒之日,財富毫無益處,

唯有公義能救人免於死亡。

5純全人行義走坦途,

惡人作惡致沉淪。

6正直人被義行所救,

奸詐者被私慾所擄。

7惡人一死,他的希望就破滅,

他對財勢的冀望轉眼成空。

8義人脫離患難,

惡人落入苦難。

9不敬虔的張口敗壞鄰舍,

義人卻因知識獲得拯救。

10義人亨通,全城快樂;

惡人滅亡,人人歡呼。

11城因正直人的祝福而興盛,

因惡人的口舌而傾覆。

12無知者輕視鄰舍,

明哲人保持緘默。

13嚼舌者洩露秘密,

忠信者守口如瓶。

14缺乏智謀,國必敗亡;

謀士眾多,戰無不勝。

15為他人作保,必受虧損;

厭惡當保人,得享平安。

16賢淑的女子得到尊榮,

殘暴的男子得到資財。

17仁慈的人造福自己,

殘酷的人惹禍上身。

18惡人賺來的轉眼成空,

播種公義的必獲獎賞。

19堅持行義,必得生命;

追逐罪惡,終必滅亡。

20心術不正的人令耶和華憎惡,

純全無過的人蒙耶和華喜愛。

21惡人終必落入法網,

義人的子孫必得拯救。

22女子貌美無內涵,

如同豬鼻掛金環。

23義人的願望結出善果,

惡人的希望招致烈怒。

24有人樂善好施,反倒越來越富;

有人一毛不拔,反而越來越窮。

25慷慨好施的必得昌盛,

恩待他人的必蒙恩待。

26囤糧不賣,惹人咒詛;

樂意賣糧,必蒙祝福。

27尋求良善得恩惠,

追求罪惡遭禍患。

28倚仗財勢者必衰敗,

義人必興旺如綠葉。

29禍害自家,必一無所有,

愚人必做智者的僕役。

30義人結果如生命之樹,

智者深得人心。

31看啊!義人在世上尚且遭報11·31 義人在世上尚且遭報」七十士譯本為「義人尚且難以得救」,參見彼得前書4·18

更何況罪人和惡人呢?

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 11:1-31

1Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa,

koma amakondwera ndi muyeso woyenera.

2Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi,

koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.

3Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera,

koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.

4Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu,

koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.

5Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo,

koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.

6Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa,

koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.

7Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso.

Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.

8Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto,

koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.

9Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake,

koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.

10Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera,

ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.

11Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima,

koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.

12Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru,

koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.

13Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi;

koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.

14Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa;

koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.

15Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto,

koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.

16Mkazi wodekha amalandira ulemu,

koma amuna ankhanza amangopata chuma.

17Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino

koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.

18Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu,

koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.

19Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo,

koma wothamangira zoyipa adzafa.

20Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota

koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.

21Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa,

koma anthu olungama adzapulumuka.

22Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba,

ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.

23Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha,

koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.

24Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe;

wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.

25Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera;

iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.

26Anthu amatemberera womana anzake chakudya,

koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.

27Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo,

koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.

28Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota,

koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.

29Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto,

ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.

30Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo,

ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.

31Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi,

kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!