啟示錄 11 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

啟示錄 11:1-19

兩位見證人

1有一根杆子賜給我當量尺,同時有聲音吩咐我說:「起來,量一量上帝的殿和祭壇,並數點在殿裡敬拜的人。 2你不用量聖殿的外院,因為這部分已經給了外族人,他們要踐踏聖城四十二個月。 3我要賜權柄給我的兩個見證人,他們將身穿麻衣,傳道一千二百六十天。」

4這兩位見證人就是豎立在世界之主面前的那兩棵橄欖樹和兩座燈臺。 5若有人要傷害他們,他們便從口中噴出火焰,燒滅敵人;若有人企圖加害他們,必定會這樣被殺。 6他們擁有權能,在傳道期間可以關閉天空使雨不降在地上,又有權使水變成血,並隨時用各樣的災禍擊打世界。

7當他們做完見證以後,從無底坑上來的獸要和他們交戰,並戰勝他們,把他們殺掉。 8他們便陳屍在大城的街上,這大城按寓意名叫所多瑪,又名埃及,是他們的主被釘在十字架上的地方。 9三天半之久,他們的屍體不得埋葬,各民族、各部落、各語言族群、各國家的人都觀看他們的屍體。 10地上萬民便興高采烈,互相送禮道賀,因為這兩位先知曾使地上的人受苦。

11三天半過後,上帝的生命之氣進入二人裡面,他們便站立起來。看見的人都害怕極了! 12接著天上有大聲音呼喚他們說:「上這裡來!」他們就在敵人的注視下駕雲升上天去。 13就在那一刻,發生了強烈的地震,那座城的十分之一倒塌了,因地震死亡的共七千人,生還者都在恐懼中將榮耀歸給天上的上帝。

14第二樣災難過去了,第三樣災難又接踵而來!

第七位天使吹號

15第七位天使吹響號角的時候,天上有大聲音說:「世上的國度現在已經屬於我們的主和祂所立的基督了。祂要作王,直到永永遠遠。」 16在上帝面前,坐在自己座位上的二十四位長老都一同俯伏敬拜上帝,說:

17「主啊!昔在、今在的全能上帝啊!

我們感謝你,

因你已施展大能作王了。

18世上的列國曾向你發怒,

現在是你向他們發烈怒的日子了。

時候已到,你要審判死人,

你要賞賜你的奴僕、先知、聖徒

和一切不論尊卑敬畏你名的人,

你要毀滅那些毀壞世界的人。」

19那時,天上上帝的聖殿敞開了,殿內的約櫃清晰可見,又有閃電、巨響、雷鳴、地震和大冰雹。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 11:1-19

Mboni Ziwiri

1Ndinapatsidwa bango longa ndodo yoyezera ndipo ndinawuzidwa kuti, “Pita, kayeze Nyumba ya Mulungu ndi guwa lansembe, ndipo ukawerenge anthu opembedza mʼNyumbamo. 2Koma bwalo lakunja ulisiye, usaliyeze chifukwa linaperekedwa kwa a mitundu ina. Iwo adzawupondereza mzinda woyerawo kwa miyezi 42. 3Ndipo ndidzapereka mphamvu kwa mboni zanga ziwiri, zitavala ziguduli, ndipo kwa masiku 1,260 zidzakhala zikulalikira.” 4Mboni ziwirizo ndi mitengo iwiri ya olivi ndi zoyikapo nyale ziwiri zija zimene zili pamaso pa Ambuye wa dziko lapansi. 5Ngati wina atafuna kuzipweteka mbonizo, moto umatuluka mʼkamwa mwawo ndikuwononga adani awo. 6Mbonizo zili ndi mphamvu yomanga mvula kuti isagwe pa nthawi imene akulalikirayo; ndipo zili ndi mphamvu yosanduliza madzi kukhala magazi ndi yokantha dziko lapansi ndi miliri ya mitundumitundu nthawi iliyonse imene zingafune.

7Tsono zikadzatsiriza umboni wawowo, chirombo chotuluka mʼChidzenje chakuya chija chidzachita nawo nkhondo nʼkuzigonjetsa mpaka kuzipha. 8Mitembo yawo idzakhala ili gone pabwalo la mu mzinda waukulu umene mozimbayitsa umatchedwa Sodomu ndi Igupto, kumenenso Ambuye wawo anapachikidwako. 9Kwa masiku atatu ndi theka, anthu ochokera ku mtundu uliwonse, fuko lililonse, chiyankhulo chilichonse ndi dziko lililonse, azidzayangʼanitsitsa mitembo yawoyo koma adzakana kuyikwirira. 10Anthu okhala pa dziko lapansi adzasangalala nazo zimenezi. Adzachita chikondwerero ndi kutumizirana mphatso, chifukwa aneneri awiri amenewa ankasautsa anthu okhala pa dziko lapansi.

11Koma patapita masiku atatu ndi theka aja, mpweya wopatsa moyo wochoka kwa Mulungu unalowa mwa aneneriwo, ndipo anayimirira, ndipo amene anawaona anachita mantha aakulu. 12Kenaka aneneri aja anamva mawu ofuwula ochokera kumwamba owawuza kuti, “Bwerani kuno.” Ndipo anapitadi kumwamba mu mtambo adani awo aja akuwaona.

13Nthawi yomweyo panachitika chivomerezi choopsa mwakuti chigawo chimodzi cha magawo khumi a mzinda chinagwa. Anthu 7,000 anaphedwa ndi chivomerezicho, ndipo opulumukawo anachita mantha kwambiri nayamba kutamanda Mulungu wakumwamba.

14Tsoka lachiwiri lapita; koma tsoka lachitatu likubwera posachedwapa.

Lipenga Lachisanu ndi Chiwiri

15Mngelo wachisanu ndi chiwiri anawomba lipenga lake, ndipo kumwamba kunamveka mawu ofuwula amene anati,

“Ufumu wa dziko lapansi uli

mʼmanja mwa Ambuye athu ndi Khristu wake uja,

ndipo adzalamulira mpaka muyaya.”

16Ndipo akuluakulu 24 aja okhala pa mipando yawo yaufumu pamaso pa Mulungu, anadzigwetsa chafufumimba napembedza Mulungu 17Iwo anati,

“Ife tikuyamika Inu Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse,

amene mulipo ndipo munalipo,

chifukwa mwaonetsa mphamvu yanu yayikulu,

ndipo mwayamba kulamulira.

18A mitundu ina anapsa mtima;

koma yafika nthawi yoonetsa mkwiyo.

Nthawi yakwana yoweruza anthu akufa,

yopereka mphotho kwa atumiki anu, aneneri,

anthu oyera mtima anu ndi amene amaopa dzina lanu,

wamngʼono pamodzi ndi wamkulu yemwe.

Yafika nthawi yowononga amene awononga dziko lapansi.”

19Pamenepo anatsekula Nyumba ya Mulungu kumwamba ndipo mʼkati mwake munaoneka Bokosi la Chipangano. Kenaka kunachita mphenzi, phokoso, mabingu, chivomerezi ndipo kunachita mkuntho wamatalala akuluakulu.