啟示錄 12 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

啟示錄 12:1-18

婦人與巨龍

1在天上出現了一個奇異的景象:有一個婦人,身披太陽,腳踏月亮,頭戴有十二顆星的冠冕。 2她懷了孕,正因產痛而呼叫。

3這時天上出現了另一個奇異的景象:有一條紅色巨龍出現,牠有七頭十角,每個頭上都戴著冠冕。 4牠的尾巴將天上三分之一的星掃落到地上。巨龍站在那正要生產的婦人面前,等著要吃掉她生下來的嬰孩。 5婦人生下一個男嬰,就是將來要用鐵杖治理列國的。那男嬰被提到了上帝的寶座那裡, 6婦人則逃到曠野,在上帝為她預備的地方安度一千二百六十天。

7天上起了戰爭,米迦勒和他的天使出戰巨龍。巨龍和牠的天使極力抵抗, 8那巨龍敗下陣來,天上再沒有牠們的立足之地, 9牠和牠的天使都一同從天上被摔到地上。巨龍就是那古蛇,又名魔鬼或撒旦,也就是那迷惑全人類的。

10我聽見天上有大響聲說:「我們上帝的救贖、權能、國度和祂所立的基督的權柄現在來臨了。因為那晝夜不停地在我們上帝面前控告我們弟兄的,已經被摔到地上了。 11弟兄們是靠著羔羊的血和自己所見證的道戰勝了牠,他們甘願犧牲,視死如歸。 12因此,諸天和其中的居民都要歡欣雀躍!但大地和海洋有禍了,因為魔鬼知道牠的時日不多了,就怒氣沖沖地下到你們那裡。」

13巨龍見自己被摔到地上,就迫害那先前產下男嬰的婦人。 14但那婦人得到一對巨鷹的翅膀,使她能飛到曠野,去上帝為她預備的地方避難,在那裡被照顧三年半。 15巨龍緊追不捨,張口吐出大量的水,如同江河一般,要沖走那婦人, 16大地卻幫助她,張口吞了巨龍口中吐出來的大水。 17巨龍大怒,轉而攻擊她的其他兒女,就是那些堅守上帝的誡命、為耶穌做見證的人。 18那時巨龍站在海邊的沙地上。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 12:1-18

Mayi ndi Chinjoka

1Chizindikiro chachikulu chinaoneka kuthambo; mayi atavala dzuwa, mapazi ake ataponda mwezi, pamutu pake pali chipewa chaufumu chokhala ndi nyenyezi khumi ndi ziwiri. 2Mayiyo anali woyembekezera ndipo pa nthawi yake yochira analira mokuwa chifukwa cha ululu wakubala. 3Kenaka ku thambo kunaonekanso chizindikiro china; chinjoka chachikulu kwambiri, chofiira chomwe chinali ndi mitu isanu ndi iwiri ndi nyanga khumi; pamutu uliwonse chitavala chipewa chaufumu. 4Mchira wake unakokolola gawo limodzi la magawo atatu a nyenyezi kuzichotsa ku thambo ndi kuziponya pa dziko lapansi. Chinjoka chija chinadzayima patsogolo pa mayi uja amene anali pafupi kuberekayu kuti mwanayo akangobadwa chimudye. 5Mayiyo anabereka mwana wamwamuna amene adzalamulira anthu a mitundu ina yonse ndi ndodo yachitsulo. Ndipo mwanayo analandidwa ku dzanja la mayiyo ndi kupita naye kwa Mulungu ku mpando wake waufumu. 6Mayiyo anathawira ku chipululu ku malo kumene Mulungu anamukonzera, kumene akasamalidweko masiku 1,260.

7Zitatero, kumwamba kunayambika nkhondo. Mikayeli ndi angelo ake kumenyana ndi chinjoka chija. Chinjokacho ndi angelo ake anabwezeranso. 8Koma analibe mphamvu ndipo anagonjetsedwa nathamangitsidwa kumwambako. 9Chinjoka chachikulu chija chinagwetsedwa pansi. Ichocho ndiye njoka yakalekale ija yotchedwa Mdierekezi kapena Satana, amene amasocheretsa anthu a pa dziko lonse lapansi. Chinaponyedwa pa dziko la pansi pamodzi ndi angelo ake.

10Kenaka ndinamva mawu ofuwula kumwamba akunena kuti,

“Tsopano chipulumutso, mphamvu,

ufumu wa Mulungu wathu

ndi ulamuliro wa Khristu wake zabwera.

Pakuti woneneza abale athu uja,

amene amangokhalira kuwaneneza pamaso pa Mulungu usana ndi usiku,

wagwetsedwa pansi.

11Abale athuwo anamugonjetsa

ndi magazi a Mwana Wankhosa

ndiponso mawu a umboni wawo.

Iwo anadzipereka kwathunthu,

moti sanakonde miyoyo yawo.

12Choncho, kondwerani, inu dziko lakumwamba

ndi onse okhala kumeneko!

Koma tsoka dziko lapansi ndi nyanja

chifukwa Mdierekezi wagwetsedwa kwa inu!

Iye wadzazidwa ndi ukali

chifukwa akudziwa kuti nthawi yake ndi yochepa.”

13Pamene chinjokacho chinaona kuti chagwetsedwa pa dziko lapansi, chinayamba kuthamangitsa mayi uja amene anali atabala mwana wamwamunayu. 14Mayiyo anapatsidwa mapiko awiri a chiwombankhanga chachikulu kuti athawire ku malo ake aja a ku chipululu. Kumeneko adzasamalidwako zaka zitatu ndi theka kuti chinjoka chija chisamupeze. 15Kenaka chinjoka chija chinalavulira mayiyo madzi ambiri ngati mtsinje, kuti madziwo amukokolole. 16Koma dziko lapansi linamuthandiza mayiyo. Nthaka inatsekuka ndi kumeza mtsinje uja unachokera mʼkamwa mwa chinjokacho. 17Pamenepo chinjokacho chinamupsera mtima mayiyo ndipo chinachoka kupita kukachita nkhondo ndi ana ena onse a mayiyo, ndiye kuti anthu amene anasunga malamulo a Mulungu ndi kuchitira umboni za Yesu.

18Kenaka ndinaona chinjokacho chitayima mʼmbali mwa nyanja.