創世記 49 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

創世記 49:1-33

雅各的預言

1雅各把他的兒子們都叫來,對他們說:「你們到我身邊來,我要把你們將來的遭遇告訴你們。

2雅各的兒子們啊,

你們都來聽,

聽你們父親以色列的話。

3呂便啊,你是我的長子,

是我年輕力壯時生的,

比眾弟兄更有尊榮和力量。

4可是,你必不再居首位,

因為你放縱情慾,

如沸騰不止的水,

你上了你父親的床,

玷污了我的榻。

5西緬利未串通一氣,

依仗刀劍,殘暴不仁。

6我的靈啊,不要與他們同謀。

我的心啊,不要與他們聯合。

他們洩憤殺人,

隨意砍斷牛腿的筋。

7他們狂暴兇殘,該受咒詛!

我要使他們分散在雅各的子孫中,

散居在以色列各地。

8猶大啊,你的兄弟們必讚美你,

你必制伏你的仇敵,

你父親的兒子必向你下拜。

9我兒猶大是頭小獅子,

他獵食回來,躺臥如雄獅,

蹲伏如母獅,誰敢驚擾他?

10王權必不離猶大

御杖必伴他左右,

直到那位執掌王權的來到,

萬民都必歸順他。

11「他把小驢拴在葡萄樹旁,

把驢駒拴在上好的葡萄樹旁;

他在葡萄酒中洗衣服,

在葡萄汁中洗外袍。

12他的眼睛比酒烏潤,

牙齒比奶潔白。

13西布倫必安居在海濱,

成為泊船的港口,

他的疆界必伸展到西頓

14以薩迦是頭壯驢,

臥在羊圈中。

15他見那地方好作安身之處,

地土肥美,就垂下肩頭,

做了奴隸。

16必治理他的人民,

以色列的一個支派。

17他必成為路邊的蛇,

道旁的毒蛇,

咬傷馬蹄,使騎馬的人墜落。

18「耶和華啊,

我切切等候你的拯救。

19迦得必被強盜劫掠,

他卻要反敗為勝追趕他們。

20亞設必有豐美的出產和供君王享用的美味。

21拿弗他利是頭自由的母鹿,

養育美麗的小鹿49·21 養育美麗的小鹿」或譯「口出佳美之言」。

22約瑟是多結果子的枝條,

長在水泉旁,

他的枝條探出牆外。

23弓箭手兇猛地攻擊他,

惡狠狠地射他。

24但他手持強弓,

雙臂穩健有力,

因為雅各的大能者——以色列的牧者和磐石幫助他。

25你父親的上帝必幫助你,

全能者必賜你天上的恩澤、

地上的百福,

使你子孫興旺、牛羊滿圈。

26你父親的祝福高過亙古永存的峰巒,

多如綿延無盡的群山,

願這一切的祝福都臨到約瑟頭上,

臨到這超越眾弟兄的人身上。

27便雅憫是匹貪婪的狼,

早晨吞吃獵物,

晚上瓜分戰利品。」

28以上是以色列的十二支派,他們的父親按著他們不同的福分給他們祝福。 29雅各又囑咐他們說:「我要離世了,你們要把我葬在以弗崙田間的洞裡,讓我與祖先在一起。 30那洞穴在迦南幔利附近的麥比拉田間,是亞伯拉罕以弗崙買來作墳地的。 31亞伯拉罕和他的妻子撒拉以撒和他的妻子利百加都葬在那裡,我把利亞也葬在了那裡。 32那塊田和田間的洞穴是向人買的。」 33雅各囑咐完眾子,在床上躺下,嚥了氣,去他祖先那裡了。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 49:1-33

Yakobo Adalitsa Ana ake Aamuna

1Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.

2“Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo;

mverani abambo anu Israeli.

3“Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa;

mphamvu yanga ndiponso chizindikiro choyamba cha mphamvu zanga,

wopambana pa ulemerero ndi mphamvu.

4Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana,

iwe unagona pa bedi la abambo ako,

ndithu unayipitsa bedi la mdzakazi wake.

5“Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo,

anachitira nkhanza anthu amene anachita nawo pangano.

6Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri,

kapena kugwirizana nawo mʼmabwalo awo,

pakuti anapha anthu mu mkwiyo wawo

ndipo anapundula ngʼombe zamphongo monga kunawakomera.

7Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi

ndi ukali wawo wankhanza choterewu!

Ine ndidzawabalalitsa mʼdziko la Yakobo

ndi kuwamwaza iwo mʼdziko la Israeli.

8“Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda;

dzanja lako lidzagwira pa khosi pa adani ako;

abale ako adzakugwadira iwe.

9Yuda ali ngati mwana wa mkango;

umabwerera ku malo ako ndi zofunkha, mwana wanga.

Monga mkango, amadziwongola ndi kugona pansi,

ndipo ngati mkango waukazi, ndani angalimbe mtima kumudzutsa?

10Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda,

udzawupanirira ulamuliro motero kuti palibe amene adzawuchotse,

mpaka mwini wake weniweni atabwera

ndipo mitundu yonse ya anthu idzamumvera.

11Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa,

ndi mwana wa bulu ku nthambi ya mpesa wabwino.

Ndi iye amene amachapa zovala zake mu vinyo;

ndi mkanjo wake mu vinyo wofiira ngati magazi.

12Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo,

mano ake woyera chifukwa cha mkaka.

13“Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja;

adzakhala pa dooko la sitima zapamadzi;

malire ake adzafika ku Sidoni.

14“Isakara ali ngati bulu wamphamvu

wogona pansi pakati pa makola.

15Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira

ndi kukongola kwa dziko lake,

iye anaweramutsa msana kuti anyamule katundu wake

ndipo anasanduka wogwira ntchito ya ukapolo.

16“Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake

monga limodzi mwa mafuko a anthu a mu Israeli.

17Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu,

songo yokhala mʼnjira

imene imaluma chidendene cha kavalo

kuti wokwerapoyo agwe chagada.

18“Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.

19“Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo,

koma iye adzawathamangitsa.

20“Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma,

ndipo iye adzapereka chakudya kwa mafumu.

21“Nafutali ali ngati mbawala yayikazi

yokhala ndi ana okongola kwambiri.

22“Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso,

mtengo wobereka zipatso pafupi ndi kasupe,

nthambi zake zimayanga pa chipupa cha mwala.

23Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza;

anamuthamangitsa ndi mauta awo.

24Koma uta wake sunagwedezeke,

ndi manja ake amphamvu aja analimbika,

chifukwa cha mphamvu za Mulungu Wamphamvu wa Yakobo,

chifukwa ali Mʼbusa ndi Thanthwe la Israeli.

25Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza;

chifukwa cha Mulungu Wamphamvu, amene amakudalitsa

ndi mvula yochokera kumwamba,

ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka,

ndipo amakudalitsa pokupatsa ana ambiri ndi ngʼombe zambiri.

26Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa

madalitso a mapiri akale

oposa zabwino za ku zitunda zamgonagona.

Zonse izi zikhale pamutu pa Yosefe,

pa mphumi pa wopatulika uja amene anapatulidwa pakati pa abale ake.

27“Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa;

umene mmawa umapha ndi kudya zofunkha,

ndipo madzulo umagawa zofunkhazo,”

28Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.

Kumwalira kwa Yakobo

29Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti. 30Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda. 31Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya. 32Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”

33Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.