啟示錄 1 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

啟示錄 1:1-20

1以下是上帝賜給耶穌基督的啟示,讓祂把將來要發生的事指示祂的眾奴僕。因此,祂差遣天使告訴祂的奴僕約翰2約翰便為自己所看見的一切——上帝的道和耶穌基督做見證。 3那位宣讀這預言的人和那些聽見並遵守其中內容的人有福了,因為日期近了。

問候七教會

4-5約翰寫信給你們亞細亞的七間教會。願昔在、今在、以後永在的上帝,祂寶座前的七靈1·4-5 七靈」指的就是聖靈,數字七代表完全,不是說有七個靈。和耶穌基督賜給你們恩典和平安。耶穌基督是忠心的見證人,是首先從死裡復活的,是世上君王的首領。祂愛我們,用自己的血救我們脫離罪惡, 6使我們成為祭司的國度1·6 成為祭司的國度」或譯「成為國度,做祭司」。來事奉祂的父上帝。願祂得到一切榮耀和權柄,一直到永永遠遠。阿們!

7看啊!祂要駕雲降臨,世人都要看見祂,包括曾經刺祂的人。地上的萬族都必因祂而哀哭。這事必定實現。阿們!

8主上帝說:「我是阿拉法,我是俄梅加1·8 阿拉法」和「俄梅加」分別是希臘文第一個和最後一個字母,故此句意即「我是始,我是終」。,我是昔在、今在、以後永在的全能者。」

基督的顯現

9約翰是你們的弟兄,在耶穌裡和你們患難與共、同享國度、一起忍耐。我因傳揚上帝的道、為主耶穌做見證而到了拔摩海島上。 10主日,我被聖靈感動,聽見身後有號角般響亮的聲音說: 11「把你所看見的寫在書上,然後送給以弗所士每拿別迦摩推雅推喇撒狄非拉鐵非老底嘉七間教會。」

12我轉身看究竟是誰在對我說話,我看見七個金燈臺, 13有一位好像人子耶穌的站在這些燈臺中間。祂長袍垂腳,金帶圍胸, 14頭與髮白如羊毛、潔白如雪,眼睛像火焰, 15雙腳像爐中冶煉過的銅一樣光亮,聲音如同洪濤之聲。 16祂右手拿著七顆星,口中吐出一把兩刃的利劍,面貌如烈日放光。

17我一看見祂,便仆倒在祂腳前,像死了一樣。祂把右手按在我身上,說:「不要害怕!我是首先的,我是末後的, 18我是永活者。我曾經死過,但看啊,我永永遠遠活著。我掌握死亡和陰間的鑰匙。 19所以,你要將所看見的一切——現在和將來要發生的事都記錄下來。 20你所看見在我右手中的七顆星和七個金燈臺的奧祕是,七顆星代表七間教會的天使1·20 天使」或譯「信使」或「使者」,下同,可能指教會的守護天使,或者是教會的領袖。,七個燈臺代表七間教會。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 1:1-20

Mawu Oyamba

1Vumbulutso lochokera kwa Yesu Khristu, limene Mulungu anamupatsa kuti aonetse atumiki ake zimene zinayenera kuchitika posachedwa. Iye anatuma mngelo wake kuti adziwitse mtumiki wake Yohane, 2amene akuchitira umboni chilichonse chimene anachiona. Awa ndi Mawu a Mulungu ndi umboni wa Yesu Khristu. 3Ngodala munthu amene awerenga mawu oneneratu zamʼtsogolo ndi iwo amene amamva ndi kusunga zolembedwa mʼbukuli pakuti nthawi yayandikira.

Malonje kwa Mipingo Isanu ndi Iwiri

4Ndine Yohane,

Kupita ku mipingo isanu ndi iwiri ya mʼchigawo cha Asiya.

Chisomo ndi mtendere kwa inu, kuchokera kwa Iye amene ali, amene analipo ndi amene akubwera ndi kwa mizimu isanu ndi iwiri yokhala patsogolo pa mpando wake waufumu, 5ndiponso kuchokera kwa Yesu Khristu mboni yokhulupirika, woyamba kuukitsidwa, ndi wolamulira mafumu a dziko lapansi.

Kwa Iye amene amatikonda ndipo watimasula ku machimo athu ndi magazi ake, 6ndipo watisandutsa mafumu ndi ansembe kuti tizitumikira Mulungu ndi Atate ake. Kwa Iye kukhale ulemerero ndi mphamvu ku nthawi zosatha, Ameni.

7“Onani akubwera ndi mitambo,”

ndipo “Aliyense adzamuona,

ndi amene anamubaya omwe.”

Ndipo anthu a mitundu yonse ya pa dziko lapansi “adzalira chingʼangʼadza chifukwa cha Iye.”

Zidzakhaladi momwemo, Ameni.

8“Ine ndine Alefa ndi Omega,” akutero Ambuye Mulungu Wamphamvuzonseyo “amene muli, amene munalipo, ndi amene mudzakhalapo.”

Wina Wokhala ngati Mwana wa Munthu

9Ine Yohane mʼbale wanu ndi mnzanu mʼmasautso ndi mu ufumu ndi mukupirira kwambiri, zomwe ndi zathu mwa Yesu, ndinali pa chilumba cha Patimo chifukwa cha Mawu a Mulungu ndi umboni wa Yesu. 10Pa tsiku la Ambuye ndinanyamulidwa ndi Mzimu ndipo ndinamva kumbuyo kwanga mawu ofuwula ngati lipenga, 11amene anati, “Lemba mʼbuku zimene ukuziona ndipo uzitumize ku mipingo isanu ndi iwiri ya ku Efeso, Simurna, Pergamo, Tiyatira, Sarde, Filadefiya ndi ku Laodikaya.”

12Nditatembenuka kuti ndione amene amandiyankhulayo, ndinaona zoyikapo nyale zisanu ndi ziwiri zagolide. 13Pakati pa zoyikapo nyalezo ndinaona wina wooneka ngati Mwana wa Munthu atavala mkanjo wofika kumapazi ake ndipo anamangirira lamba wagolide pa chifuwa pake. 14Tsitsi lake linali loyera ngati thonje, kuyera ngati matalala, ndipo maso ake amawala ngati malawi amoto. 15Mapazi ake anali ngati chitsulo choti chili mʼngʼanjo yamoto, ndipo mawu ake anali ngati mkokomo wamadzi othamanga. 16Mʼdzanja lake lamanja ananyamula nyenyezi zisanu ndi ziwiri, ndipo mʼkamwa mwake munali lupanga lakuthwa konsekonse. Nkhope yake imawala ngati dzuwa lowala kwambiri.

17Nditamuona ndinagwa pa mapazi ake ngati wakufa. Kenaka Iye anasanjika dzanja lake lamanja pa ine nati, “Usachite mantha. Ndine Woyamba ndi Wotsiriza. 18Ine ndine Wamoyo; ndinali wakufa ndipo taona ndine wamoyo mpaka muyaya! Ndipo ndili ndi makiyi a imfa ndi Hade.

19“Chomwecho, lemba zimene waona, zimene zilipo panopa ndi zimene zidzachitike mʼtsogolo. 20Tanthauzo la nyenyezi zisanu ndi ziwiri zimene waziona mʼdzanja langa lamanja ndi la zoyikapo nyale zagolide zisanu ndi ziwiri ndi ili: Nyenyezi zisanu ndi ziwiri ndi angelo a mipingo isanu ndi iwiri ija, ndipo zoyikapo nyale zisanu ndi ziwiri zija ndi mipingo isanu ndi iwiri ija.”