利未記 6 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

利未記 6:1-30

1耶和華對摩西說: 2「如果有人犯罪,不忠於耶和華,拒絕歸還同胞委託他保管的物品或抵押品,或搶掠同胞,或欺騙同胞, 3或撿到東西卻矢口否認,或起假誓,或犯其他類似的罪, 4他必須歸還一切靠偷盜、欺詐、侵佔、拾遺、 5或起假誓得來的東西,他必須在獻贖過祭那天如數歸還物主,並加賠五分之一。 6他要從羊群中選一隻毫無殘疾的公綿羊,或把同等價值的銀子帶到祭司那裡,獻給耶和華作贖過祭。 7祭司要在耶和華面前為他贖罪,他就會得到赦免。」

祭司獻燔祭的條例

8耶和華對摩西說: 9「你要吩咐亞倫及其子孫遵行以下獻燔祭的條例。

「燔祭要整夜留在祭壇上,壇上的火要不停地燃燒。 10早晨,祭司要穿上細麻衣袍和內衣,將燔祭壇上的灰燼清理好,放在祭壇旁邊。 11然後,他要更換衣服,把灰燼拿到營外潔淨的地方。 12祭壇上的火要不斷燃燒,不能熄滅。祭司每天早上要在壇上加柴,擺上燔祭,在上面燒平安祭牲的脂肪。 13壇上的火必須不斷燃燒,不可熄滅。

祭司獻素祭的條例

14「以下是獻素祭的條例。

「祭司——亞倫的子孫要在祭壇前向耶和華獻素祭。 15祭司要從素祭中拿一把調油的細麵粉和所有的乳香,作為象徵放在壇上焚燒,作蒙耶和華悅納的馨香之祭。 16亞倫及其子孫要吃剩下的祭物,要在會幕院子裡的聖潔之處做無酵餅吃。 17做餅時不可加酵。這些祭物是我從獻給我的火祭中賜給他們的,像贖罪祭和贖過祭一樣是至聖之物。 18亞倫的子孫中,男子都可以吃。這是他們世世代代應得之份。凡接觸到這些祭物的都會變得聖潔。」

19耶和華對摩西說: 20亞倫及其子孫受膏那天,要獻給耶和華一公斤細麵粉作為日常獻的素祭,早晚各獻一半。 21要把這些細麵粉調上油,用煎鍋做餅,切成塊獻上,作為蒙耶和華悅納的馨香之祭。 22亞倫子孫中繼任大祭司的,受膏時要獻上素祭。這種祭物屬於耶和華,必須全部燒掉。 23祭司獻的這種素祭不可以吃,要全部燒掉。」

祭司獻贖罪祭的條例

24耶和華對摩西說: 25「你把以下贖罪祭的條例告訴亞倫及其子孫。

「贖罪祭是至聖的,要在殺燔祭牲的地方,在耶和華面前宰祭牲。 26獻這祭的祭司要在會幕院子裡的聖潔之處吃這祭牲。 27凡接觸到這些祭肉的,都會變得聖潔。如果衣服被濺上血,則要在聖潔之處把衣服洗淨。 28用來煮祭肉的瓦鍋,用後都要打碎。如果用的是銅鍋,要擦乾淨並用水沖洗。 29這些祭肉是至聖之物,祭司家族中的男子都可以吃。 30如果祭牲的血被帶進會幕,在聖所內進行贖罪,就不可吃祭肉,必須全部燒掉。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 6:1-30

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Ngati munthu wina aliyense achimwa, nachita zinthu mosakhulupirika kwa Yehova chifukwa cha kunyenga mnzake pokana kumubwezera zimene anamusungitsa, kapena kumubera kapenanso kumulanda, 3kapena ndi kunama kuti sanatole chinthu chimene chinatayika, kapena kulumbira mwachinyengo pa chinthu chilichonse chimene munthu akachita amachimwa nacho, 4ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kubweza zimene anabazo, zimene analanda mwachinyengozo, zimene anamusungitsazo, zimene anatolazo 5kapena zimene analumbira monyengazo. Pa tsiku limene apezeke kuti wapalamuladi, iye ayenera kumubwezera mwini wake zinthu zonsezi ndi kuwonjezerapo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse. 6Pambuyo pake apereke kwa Yehova nsembe yopalamula. Nsembe yake ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake wogwirizana ndi nsembe yopepesera machimo. 7Kenaka wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo pamaso pa Yehova, ndipo adzakhululukidwa chilichonse chomwe anachita kuti akhale wopalamula.”

Nsembe Yopsereza

8Yehova anawuza Mose kuti, 9“Lamula Aaroni ndi ana ake kuti, ‘Lamulo la nsembe yopsereza ndi ili: Nsembe yopserezayo izikhala pa moto pa guwa usiku wonse mpaka mmawa, ndipo moto wa paguwapo uzikhala ukuyaka nthawi zonse. 10Tsono wansembe avale mkanjo wake wa nsalu yofewa ndi yosalala. Mʼkati avalenso kabudula wofewa, wosalala. Pambuyo pake atenge phulusa la nyama imene yatenthedwa pa guwa lansembe paja ndi kulithira pambali pa guwa lomwelo. 11Akatero avule zovala zakezo ndi kuvala zovala zina. Kenaka atulutse phulusalo ndi kukaliyika pa malo woyeretsedwa kunja kwa chithando. 12Moto wa pa guwa uzikhala ukuyaka nthawi zonse, usamazime. Mmawa uliwonse wansembe aziwonjezerapo nkhuni pa motopo ndi kukonza nsembe yopsereza, ndi kutentha mafuta a nsembe yachiyanjano pamenepo. 13Moto uzikhala ukuyaka pa guwa nthawi zonse ndipo usazimepo.

Nsembe Zachakudya

14“ ‘Lamulo la nsembe yachakudya ndi ili: ana a Aaroni azibwera nayo nsembeyo pamaso pa Yehova, patsogolo pa guwa. 15Wansembe mmodzi atapeko dzanja limodzi la ufa wosalala wa nsembe yachakudya ija kuti ukhala ufa wachikumbutso ndi mafuta pamodzi ndi lubani yense amene ali pa nsembe ya chakudyacho, ndipo azitenthe pa guwa kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse kuti zikhale nsembe ya fungo lokomera Yehova. 16Aaroni ndi ana ake azidya zimene zatsala koma azidya zopanda yisiti ku malo wopatulika, ku bwalo la tenti ya msonkhano. 17Poziphika asathire yisiti. Ndawapatsa zotsalazo kuti zikhale gawo lawo la nsembe zanga zopsereza. Zonsezi ndi zopatulika kwambiri monga nsembe yopepesera tchimo ndiponso nsembe yopepesera machimo. 18Mwana aliyense wamwamuna wa Aaroni azidyako za nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova. Ndi gawo lake lokhazikika la chopereka chopsereza kwa Yehova pa mibado yanu yonse. Chilichonse chimene chidzakhudza nsembezo chidzakhala chopatulika.’ ”

19Yehova anawuzanso Mose kuti, 20“Nsembe imene Aaroni ndi ana ake ayenera kupereka kwa Yehova pa tsiku limene wansembe akudzozedwa ndi iyi: ufa wosalala kilogalamu imodzi ngati chopereka chachakudya cha nthawi zonse. Azipereka theka limodzi mmawa ndipo theka linalo madzulo. 21Ipangidwe ndi mafuta pa chiwaya ndipo ubwere nayo ili yosakaniza bwino, yophikidwa mitandamitanda monga amachitira ndi nsembe yachakudya. Iphikidwe moti itulutse fungo lokomera Yehova. 22Mwana wa fuko la Aaroni amene adzadzozedwe kukhala wansembe kulowa mʼmalo mwa Aaroni ndiye amene azidzakonza ndi kupereka nsembeyi kwa Yehova nthawi zonse monga kunalembedwera. 23Nsembe iliyonse yachakudya ya wansembe izitenthedwa kwathunthu, isamadyedwe.”

Nsembe Yopepesera Tchimo

24Yehova anawuza Mose kuti 25“Uza Aaroni ndi ana ake kuti, ‘Malamulo a nsembe ya tchimo ndi awa: Nsembeyi iziphedwa pamaso pa Yehova pa malo pamene mumaphera nsembe yopsereza popeza ndi nsembe yopatulika. 26Wansembe amene apereke nsembeyi adyere ku malo wopatulika ndiye kuti mʼbwalo la tenti ya msonkhano. 27Chilichonse chimene chidzakhudza nsembeyo chidzakhala chopatulika, ndipo ngati magazi ake agwera pa chovala, muchape chovalacho pa malo opatulika. 28Mʼphika wadothi umene aphikira nyamayo auphwanye. Koma ngati yaphikidwa mu mʼphika wa mkuwa, awukweche ndi kuwutsukuluza ndi madzi. 29Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kuyidya popeza nsembeyi ndi yopatulika kwambiri. 30Koma nsembe yopepesera tchimo imene magazi ake amabwera nawo mu tenti ya msonkhano kudzachita mwambo wopepesera tchimo ku malo opatulika isadyedwe, mʼmalo mwake itenthedwe.’ ”