路加福音 9 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

路加福音 9:1-62

差遣十二使徒

1耶稣召集了十二个使徒,赐他们能力和权柄可以医病赶鬼, 2又差遣他们出去宣讲上帝国的福音、医治病人。 3耶稣叮嘱他们:“出门的时候,什么也不要带,不要带手杖、背包、干粮、金钱,也不要带两件衣服。 4有人家接待你们,就住下来,一直住到你们离开。 5如果有人不欢迎你们,你们在离开那城的时候,就把脚上的尘土跺掉,作为对他们的警告。”

6使徒领命出发,走遍各个乡村,到处宣扬福音,替人治病。

希律的困惑

7耶稣的事迹很快便传到希律耳中,令他十分困惑,因为有人说:“约翰死而复活了”, 8有人说:“以利亚显现了”,还有人说:“古代的某个先知复活了”。 9希律说:“约翰已经被我斩首,这个行奇事的人到底是谁呢?”于是他想见耶稣。

五饼二鱼的神迹

10使徒回来后,向耶稣报告了他们所行的事。随后耶稣带着他们悄悄地来到伯赛大城。 11但百姓发现了耶稣的行踪,随即也赶来了。耶稣接待他们,向他们宣讲天国的福音,医好了有病的人。 12黄昏将近,十二个使徒过来对耶稣说:“请遣散众人,好让他们到附近的村庄去借宿找吃的,因为这地方很偏僻。”

13耶稣对他们说:“你们给他们吃的吧。”

使徒们说:“我们只有五个饼和两条鱼,除非我们去买食物才够这么一大群人吃。” 14当时那里约有五千男人。

耶稣便对使徒说:“让这些人分组坐下,每组大约五十人。” 15于是使徒安排众人都坐好。 16耶稣拿起那五个饼、两条鱼,举目望着天祝谢后,掰开递给门徒,让他们分给众人。 17大家都吃饱了,把剩下的零碎收拾起来,竟装满了十二个篮子。

彼得宣告耶稣是基督

18有一次,耶稣独自祷告的时候,门徒也在旁边。

耶稣问他们:“人们说我是谁?”

19他们答道:“有人说你是施洗者约翰,也有人说你是以利亚,或是一位复活的古代先知。”

20耶稣对他们说:“那么,你们说我是谁?”

彼得回答说:“你是上帝所立的基督。”

21耶稣郑重地吩咐他们不许泄露祂的身份, 22又说:“人子必须受许多苦,被长老、祭司长和律法教师弃绝,杀害,但必在第三天复活。”

跟从主的代价

23耶稣又教导众人说:“如果有人要跟从我,就应当舍己,天天背起他的十字架跟从我。 24因为想救自己生命的,必失去生命;但为了我而失去生命的,必得到生命。 25人若赚得全世界,却失去自己或丧掉自己,又有什么益处呢? 26如果有人以我和我的道为耻,将来人子在自己、天父和圣天使的荣耀中降临时,也必以这人为耻。 27我实在告诉你们,有些站在这里的人在有生之年就必看见上帝的国。”

登山变象

28讲完这些话后大约八天,耶稣带着彼得约翰雅各一同到山上祷告。 29耶稣在祷告的时候,容貌改变了,衣裳洁白发光。 30忽然,摩西以利亚二人在跟耶稣交谈。 31二人在荣光中显现,谈论有关耶稣离世的事情,就是祂在耶路撒冷将要成就的事。 32彼得和两个同伴都困得睡着了,他们醒来后,看见了耶稣的荣光以及站在祂身边的两个人。 33摩西以利亚要离开时,彼得对耶稣说:“老师,我们在这里真好!让我们搭三座帐篷,一座给你,一座给摩西,一座给以利亚。”其实彼得并不知道自己在说什么。 34他的话还没说完,有一朵云彩飘来,笼罩他们,他们进入云彩中,都很害怕。 35云彩中有声音说:“这是我的儿子,是我拣选的,你们要听从祂!” 36声音消逝了,门徒只见耶稣独自在那里。那些日子,他们对这事都绝口不提,没有告诉任何人。

山下赶鬼

37次日,他们来到山下,有一大群人迎接耶稣。 38人群中有一个人高声喊叫:“老师,求求你看看我的儿子吧!他是我的独生子, 39鬼控制着他,他常常突然狂喊乱叫、抽搐、口吐白沫,倍受折磨,无休无止。 40我曾求过你的门徒把鬼赶出去,但他们都无能为力。”

41耶稣回答说:“唉!这又不信又败坏的世代啊!我要跟你们在一起容忍你们多久呢?把你的儿子带来吧。”

42那孩子走过来时,鬼又把他摔倒,使他抽搐,耶稣立刻斥责污鬼,把那孩子治好了,交给他父亲。 43大家看见了上帝的大能,都很惊奇。

再次预言受难

他们正为耶稣所做的一切惊讶不已时,耶稣对门徒说: 44“你们要牢记人子所说的话,因为祂将要被交到人的手里。” 45但门徒不明白这句话的意思,因为还没有向他们显明,他们听不懂,又不敢追问耶稣。

论地位

46门徒开始议论他们当中谁最伟大。 47耶稣知道他们的心思,就叫了一个小孩子来,让他站在自己身旁, 48然后对门徒说:“任何人为了我的缘故接待这样一个小孩子,就是接待我;接待我,就是接待差我来的那位。你们当中最卑微的其实是最伟大的。”

49约翰说:“老师,我们看见有人奉你的名赶鬼,就阻止他,因为他不是和我们一起跟从你的。” 50耶稣却对他说:“你不要阻止他,因为不反对你们的,就是支持你们的。”

不肯接待耶稣的村庄

51耶稣被接回天家的日子快到了,祂决定前往耶路撒冷52祂先派人到撒玛利亚的一个村庄去预备食宿, 53撒玛利亚人见他们是上耶路撒冷去的,不肯接待他们。 54祂的门徒雅各约翰见状,说:“主啊,你要我们9:54 有古卷加“像以利亚一样”。叫天上的火降下来烧死他们吗?” 55耶稣转过身来责备他们9:55 有古卷在“责备他们”之后有“说,‘你们的心如何,你们自己不知道,人子来是为了拯救人,不是为了毁灭人。’”56接着,一行人改道去另一个村子。

跟从主的代价

57在路上有人对耶稣说:“无论你往哪里去,我都要跟从你。”

58耶稣对他说:“狐狸有洞,飞鸟有窝,人子却没有安枕之处。”

59耶稣又对另一个人说:“跟从我!”但是那人说:“主啊,请让我先回去安葬我的父亲。”

60耶稣说:“让死人去埋葬他们的死人吧,你只管去传扬上帝国的福音。”

61又有一个人说:“主啊!我愿意跟从你,但请让我先回去向家人告别。”

62耶稣说:“手扶着犁向后看的人不配进上帝的国。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 9:1-62

Yesu Atuma Ophunzira ake Khumi ndi Awiri

1Yesu atawayitana khumi ndi awiriwo pamodzi, Iye anawapatsa mphamvu ndi ulamuliro wotulutsa ziwanda zonse ndi kuchiritsa matenda. 2Ndipo Iye anawatumiza kukalalikira za ufumu wa Mulungu ndi kukachiritsa odwala. 3Iye anawawuza kuti, “Musatenge kanthu paulendo. Musatenge ndodo, thumba, buledi, ndalama, ndi malaya apadera. 4Nyumba iliyonse imene mulowa, mukhale momwemo kufikira mutachoka mu mzindawo. 5Ngati anthu sakulandirani, sasani fumbi la kumapazi anu pomwe mukuchoka mu mzinda wawo ngati umboni owatsutsa.” 6Ndipo iwo ananyamuka napita, mudzi ndi mudzi, kulalikira Uthenga Wabwino ndi kuchiritsa anthu paliponse.

7Tsopano Herode olamulirayo anamva zonse zimachitikazi. Ndipo iye anavutika kwambiri chifukwa ena amati Yohane waukitsidwa kwa akufa, 8ena amati Eliya waonekera, ndipo ena anatinso mmodzi wa aneneri akalekale waukanso. 9Koma Herode anati, “Ine ndinamudula mutu Yohane. Nanga uyu ndani amene ndikumva zinthu zotere za Iye?” Ndipo iye anayesetsa kuti amuone Iye.

Yesu Adyetsa Anthu 5,000

10Atumwi atabwerera, anamuwuza Yesu zimene anachita. Kenaka Iye anawatenga napita kwa okha ku mudzi wa Betisaida. 11Koma gulu la anthu linadziwa ndipo anamutsatira. Iye anawalandira ndi kuyankhula nawo za ufumu wa Mulungu, ndi kuchiritsa amene amafuna machiritso.

12Chakumadzulo dzuwa litapita, khumi ndi awiriwo anabwera kwa Iye ndipo anati, “Uzani gulu la anthuli lichoke kuti apite ku midzi yotizungulira ndi madera a ku mudzi kuti akapeze chakudya ndi pogona, chifukwa kuno ndi kuthengo.”

13Iye anayankha kuti, “Apatseni chakudya kuti adye.”

Iwo anayankha kuti, “Ife tili ndi malofu a buledi asanu okha ndi nsomba ziwiri, pokhapokha titapita kukagula chakudya cha gulu la anthu onsewa.” 14(Pamenepo panali amuna pafupifupi 5,000).

Koma Iye anati kwa ophunzira ake, “Akhazikeni pansi mʼmagulu a anthu pafupifupi makumi asanu.” 15Ophunzira ake anachita zomwezo ndipo aliyense anakhala pansi. 16Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri zija anayangʼana kumwamba, nayamika ndipo anazigawa. Kenaka anazipereka kwa ophunzira ake kuti azipereke kwa anthu. 17Onse anadya nakhuta, ndipo ophunzira ake anatolera madengu khumi ndi awiri odzaza ndi nyenyeswa zomwe zinatsala.

Petro Avomereza Khristu

18Nthawi ina pamene Yesu amapemphera malo a yekha ali ndi ophunzira ake, Iye anawafunsa kuti, “Kodi anthu amati Ine ndine yani?”

19Iwo anayankha kuti, “Ena amati Yohane Mʼbatizi; ena amati Eliya; ndipo enanso amati mmodzi wa aneneri akalekale waukanso.”

20Iye anafunsa kuti, “Koma nanga inu mumati Ine ndine yani?”

Petro anayankha kuti, “Mpulumutsi wolonjezedwa uja wa Mulungu.”

Yesu Aneneratu za Imfa yake

21Yesu anawachenjeza kwambiri kuti asawuze wina aliyense za izi. 22Ndipo Iye anati, “Mwana wa Munthu ayenera kuzunzika kwambiri ndi kukanidwa ndi akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, Iye ayenera kuphedwa ndipo tsiku lachitatu adzauka kwa akufa.”

23Ndipo Iye anawuza onse kuti, “Ngati wina aliyense akufuna kutsata Ine, ayenera kudzikana yekha ndi kusenza mtanda wake tsiku ndi tsiku nʼkumanditsata Ine. 24Popeza aliyense amene akufuna kupulumutsa moyo wake adzawutaya, koma aliyense amene adzataya moyo wake chifukwa cha Ine adzawupulumutsa. 25Kodi chabwino ndi chiti kwa munthu, kupata zonse zapansi pano, koma ndi kutaya moyo wake kapena kudziwononga iye mwini? 26Ngati wina aliyense achita nane manyazi ndi ndiponso mawu anga, Mwana wa Munthu adzachita naye manyazi pamene adzabwera mu ulemerero wake ndi mu ulemerero wa Atate ndi angelo oyera. 27Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti ena mwa inu amene mwayima pano simudzalawa imfa musanaone ufumu wa Mulungu.”

Maonekedwe a Ulemerero wa Yesu pa Phiri

28Patatha pafupifupi masiku asanu ndi atatu Yesu atanena izi, Iye anatenga Petro, Yohane ndi Yakobo ndi kukwera ku phiri kukapemphera. 29Pamene Iye ankapemphera, maonekedwe a nkhope yake, ndi zovala zake zinawala monyezimira kwambiri. 30Anthu awiri, Mose ndi Eliya, 31anaonekera mu ulemerero opambana akuyankhulana ndi Yesu. Iwo amayankhulana za kuchoka kwake, kumene Iye anali pafupi kukakwaniritsa ku Yerusalemu. 32Petro ndi anzake anali ndi tulo tambiri, koma atadzuka, iwo anaona ulemerero wake ndi anthu awiri atayima pamodzi ndi Iye. 33Pamene anthuwo ankamusiya Yesu, Petro anati kwa Iye, “Ambuye, ndi chabwino kwa ife kuti tikhale pano. Tiloleni kuti timange misasa itatu, umodzi wanu, umodzi wa Mose ndi umodzi wa Eliya.” (Iye sanadziwe chimene amayankhula).

34Pamene Iye ankayankhula, mtambo unaonekera ndi kuwaphimba iwo, ndipo anachita mantha pamene mtambowo unawakuta. 35Mawu anachokera mu mtambomo nati, “Uyu ndi Mwana wanga amene ndamusankha; mumvereni Iye.” 36Atamveka mawuwa, anaona kuti Yesu anali yekha. Ophunzirawo anazisunga izi mwa iwo okha ndipo sanawuze wina aliyense pa nthawiyi za zomwe iwo anaziona.

Kuchiritsidwa kwa Mwana Wogwidwa ndi Chiwanda

37Mmawa mwake, akutsika ku phiri, anthu ambiri anakumana naye. 38Munthu wina mʼgulu la anthulo anayitana kuti, “Aphunzitsi, ndikupemphani kuti muone mwana wangayu, pakuti ndi mmodzi yekhayu. 39Chiwanda chikamugwira amafuwula mwadzidzidzi; chimamugwedeza kolimba mpaka kutuluka thovu kukamwa. Sichimusiya ndipo chikumuwononga. 40Ine ndinapempha ophunzira anu kuti achitulutse, koma alephera.”

41Yesu anayankha kuti, “Haa! Anthu osakhulupirira ndi mʼbado wokhota. Kodi Ine ndidzakhala nanu nthawi yayitali yotani ndi kukupirirani? Bweretsa mwana wako kuno.”

42Ngakhale pamene mnyamata amabwera kwa Yesu, chiwandacho chinamugwetsa pansi ndi kumugwedeza. Koma Yesu anadzudzula mzimu woyipawo nachiritsa mwa mnyamatayo ndi kumuperekanso kwa abambo ake. 43Ndipo iwo onse anadabwa ndi ukulu wa Mulungu.

Yesu Abwereza Kunena za Imfa yake

Aliyense akudabwa ndi zimene Yesu anachita, Iyeyo anati kwa ophunzira ake, 44“Tamvetsetsani zimene ndikufuna kukuwuzani: Mwana wa Munthu akupita kukaperekedwa mʼmanja mwa anthu.” 45Koma iwo sanazindikire zimene amatanthauza. Izi zinawadabwitsa kotero sanathe kuzimvetsa ndipo anaopa kumufunsa.

Wamkulu Ndani?

46Mkangano unayambika pakati pa ophunzira wa kuti wamkulu koposa akanakhala ndani mwa iwo. 47Yesu podziwa maganizo awo, anatenga kamwana nakayimika pambali pake. 48Ndipo Iye anawawuza kuti, “Aliyense wolandira bwino kamwana aka mʼdzina langa, ndiye kuti akulandiranso bwino Ine; ndipo aliyense wolandira bwino Ine, ndiye kuti akulandiranso bwino amene anandituma Ine. Pakuti amene ndi wamngʼono pakati panu, ndiye amene ali wamkulu koposa.”

49Yohane anati, “Ambuye, ife tinaona munthu akutulutsa ziwanda mʼdzina lanu ndipo tinayesa kumuletsa, chifukwa iyeyo si mmodzi wa ife.”

50Yesu anati, “Wosamuletsa, pakuti amene satsutsana nanu ali mbali yanu.”

A Samariya Akana Yesu

51Nthawi itayandikira yoti Iye atengedwe kupita kumwamba, Yesu anatsimikiza zopita ku Yerusalemu, 52ndipo anatuma nthumwi kuti zitsogole. Iwo anapita mʼmudzi wa Asamariya kuti akonzekere kumulandira, 53koma anthu kumeneko sanamulandire chifukwa Iye ankapita ku Yerusalemu. 54Ophunzira awa, Yohane ndi Yakobo ataona zimenezi, anafunsa kuti, “Ambuye, kodi mukufuna ife tiyitane moto kuchokera kumwamba kuti uwawononge?” 55Koma Yesu anatembenuka ndi kuwadzudzula, 56ndipo iwo anapita ku mudzi wina.

Kutsatira Yesu

57Pamene iwo ankayenda mu msewu, munthu wina anati kwa Iye, “Inu ndikutsatirani kulikonse kumene mudzapita.”

58Yesu anayankha kuti, “Nkhandwe zili ndi mapanga ake, mbalame zili ndi zisa zake, koma Mwana wa Munthu alibe malo wogonekapo mutu wake.”

59Iye anati kwa wina, “Nditsate Ine.”

Koma munthuyo anayankha kuti, “Ambuye, choyamba loleni ndipite kuti ndikayike maliro a abambo anga.”

60Yesu anati kwa iye, “Aleke akufa ayikane akufa okhaokha, koma iwe pita ukalalikire ufumu wa Mulungu.”

61Koma winanso anati, “Ine ndidzakutsatani Ambuye; koma choyamba ndiloleni ndibwerere kuti ndikatsanzikane nalo banja langa.”

62Yesu anayankha kuti, “Munthu amene akulima ndi khasu lokokedwa nʼkumayangʼana mʼmbuyo, si woyenera kugwira ntchito mu ufumu wa Mulungu.”