诗篇 137 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 137:1-9

第 137 篇

被掳者的哀歌

1我们坐在巴比伦河畔,

想起锡安禁不住凄然泪下。

2我们把琴挂在柳树上。

3俘虏我们的人要我们唱歌,

掳掠我们的人要我们歌唱,说:

“给我们唱一首锡安的歌。”

4我们流落异邦,

怎能唱颂赞耶和华的歌呢?

5耶路撒冷啊,倘若我忘了你,

情愿我的右手无法再拨弄琴弦;

6倘若我忘了你,

不以你为我的至爱,

情愿我的舌头不能再歌唱。

7耶和华啊,

求你记住耶路撒冷沦陷时以东人的行径。

他们喊道:

“拆毁这城,把它夷为平地!”

8巴比伦城啊,

你快要灭亡了,

那向你以牙还牙为我们复仇的人有福了!

9那抓住你的婴孩摔在石头上的人有福了!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 137:1-9

Salimo 137

1Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira

pamene tinakumbukira Ziyoni.

2Kumeneko, pa mitengo ya misondozi

tinapachika apangwe athu,

3pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo.

Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo;

iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”

4Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova

mʼdziko lachilendo?

5Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu,

dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.

6Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga

ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu,

ngati sindiyesa iwe

chimwemwe changa chachikulu.

7Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita

pa tsiku limene Yerusalemu anagonja.

Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi

mpaka pa maziko ake!”

8Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa,

wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera

pa zimene watichitira.

9Amene adzagwira makanda ako

ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.