耶利米书 11 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

耶利米书 11:1-23

犹大毁约

1耶和华对耶利米说: 2“你要听这约上的话,把内容告诉犹大人和耶路撒冷的居民。 3你要告诉他们,以色列的上帝耶和华说,‘不遵守这约的人必受咒诅。 4我把你们的祖先从埃及——苦难的熔炉里带出来,那时我吩咐他们遵守这约。他们若听从我的话,遵行我的吩咐,就必做我的子民,我也必做他们的上帝。 5这样,我就实现我向你们祖先起的誓——赐给他们那奶蜜之乡,正如今日一样。’”我回答说:“耶和华啊,遵命!”

6耶和华对我说:“你要在犹大各城和耶路撒冷的街头宣告,呼吁百姓听从、遵行这约。 7因为自从我把你们祖先从埃及领出来的那天起,一直到今天,我一再劝诫他们要听从我的话。 8然而,他们却不听不理,人人凭自己顽固的恶念行事。因此,我要使约中的一切咒诅临到他们,因为我吩咐他们遵守这约,他们却拒绝遵守。”

9耶和华对我说:“犹大人和耶路撒冷的居民阴谋背叛我。 10他们重蹈祖先的覆辙,不听从我的话,跟从、祭拜别的神明。以色列犹大都违背了我与他们祖先立的约。 11所以我要使他们灾难临头,无法逃脱,任他们高声呼求,我也不听。这是耶和华说的。 12那时,犹大各城和耶路撒冷的居民必去呼求他们烧香供奉的神明,却得不到任何帮助。 13犹大啊,你的神明多如你的城邑,你给可憎的巴力烧香的祭坛多如耶路撒冷的街道。

14“因此,耶利米啊,你不要为这些人祈祷,不要为他们呼求祷告,因为他们遭难时向我呼求,我必不理会他们。 15我所爱的子民既然罪恶滔天,还在我殿里做什么?难道祭肉可以为他们消灾免祸吗?他们以作恶为乐。 16耶和华曾称他们为枝繁叶茂、果实佳美的橄榄树,但现在祂要在呼啸的风暴中把它点燃,烧毁它的枝条。 17我——万军之耶和华曾栽培以色列人和犹大人,如今我要降祸给他们,因为他们作恶,向巴力献祭,惹我发怒。”

谋害耶利米

18有人想谋害我,耶和华告诉了我,并让我看见他们的所作所为。 19我好像一只被牵去宰杀的驯良羊羔,不知他们要谋害我。他们说:

“我们把这棵树连果子一同毁灭,

从世上除掉它,

使它被遗忘吧!”

20然而,审判公正、洞察肺腑心肠的万军之耶和华啊,

愿我能看见你报应他们,

因为我已向你陈明我的冤屈。

21-22亚拿突人想杀我,他们威胁我说:“你不要奉耶和华的名说预言,免得死在我们手上。”因此,万军之耶和华说:“看啊,我必惩罚他们。他们的青年必丧身刀下,他们的子女必死于饥荒, 23一个不留。因为在我报应之年,我必降灾难给亚拿突人。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 11:1-23

Pangano Liphwanyidwa

1Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti, 2“Imvani mawu a pangano ili, ndipo uwawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu. 3Awuze kuti Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ‘adzakhala wotembereredwa munthu amene samvera mawu a pangano ili. 4Awa anali mawu amene ndinalamulira makolo anu nditawatulutsa mu Igupto, kuchoka mʼngʼanjo yamoto.’ Ine ndinati, ‘Mverani Ine ndi kuchita chilichonse chimene ndakulamulirani. Mukatero mudzakhala anthu anga ndi Ine ndidzakhala Mulungu wanu. 5Tsono Ine ndidzakwaniritsa lumbiro lomwe ndinalumbira kwa makolo anu kuti ndidzawapatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi,’ dziko lomwe inu lero mukukhalamo.”

Tsono Ine ndinayankha kuti, “Ameni, Yehova.”

6Yehova anandiwuza kuti, “Lengeza mawu onsewa mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu: ‘Mverani mawu a pangano ili ndi kuzitsatira. 7Kuyambira nthawi imene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto mpaka lero, ndakhala ndi kuwachenjeza kawirikawiri kuti, ‘Mverani Ine.’ 8Koma sanamvere kapena kulabadirako. Aliyense anawumirira kuchita zoyipa za mʼmitima yawo. Ngakhale ndinawalamulira kuti asunge pangano langa koma iwo sanasunge. Choncho ndinawalanga monga ndinaneneramo.’ ”

9Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu andiwukira. 10Abwereranso ku machimo a makolo awo, amene anakana kumvera mawu anga. Akutsata milungu ina ndi kumayitumikira. Aisraeli ndi Ayuda aphwanya pangano limene ndinachita ndi makolo awo. 11Choncho Yehova akuti, ‘Ndidzawagwetsera mavuto amene sadzatha kuwalewa. Ngakhale adzandilirire, sindidzawamvera. 12Anthu a mʼmizinda ya Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu adzapita ndi kukalirira milungu imene ankayifukizira lubani, koma milunguyo sidzawathandiza ndi pangʼono pomwe mavuto akadzafika. 13Iwe Yuda, uli ndi milungu yochuluka ngati chiwerengero cha mizinda yako; chiwerengero cha maguwa ansembe amene umafukizirapo lubani kwa Baala chili ngati misewu ya mu Yerusalemu.’

14“Tsono iwe Yeremiya usawapempherere anthu amenewa ngakhale kuwadandaulira kapena kuwapepesera, chifukwa sindidzawamvera akadzandiyitana pa nthawi ya mavuto awo.

15“Kodi anthu anga okondedwa akudzachita chiyani mʼNyumba yanga?

Kodi suja iwowa amachita zoyipa zambiri?

Kodi mungathe kupulumuka,

tsoka osakugwerani

chifukwa cha nsembe zanuzo?”

16Kale Yehova ankakutchani mtengo wa olivi wa masamba obiriwira,

wokhala ndi zipatso zokongola.

Koma tsopano adzawutentha

ndi mkuntho wamkokomo

ndipo nthambi zake zidzapserera.

17Yehova Wamphamvuzonse, amene anakudzalani, walamula kuti mavuto akugwereni. Inu a banja la Yuda ndi a banja la Israeli munachitira Yehova zoyipa ndi kumukwiyitsa pamene munkapereka nsembe zanu kwa Baala.

Amuchitira Chiwembu Yeremiya

18Yehova anandiwululira ndipo ndinadziwa. Iye anatsekula maso anga kuti ndione chiwembu chawocho. 19Ndinali ngati mwana wankhosa wofatsa amene akupita naye kukamupha; sindinkadziwa kuti chiwembu chimene ankakonzekeracho chinkaloza ine. Iwo amati:

“Tiyeni timuphe

munthu ameneyu

kuti dzina lake lisadzakumbukiridwenso.”

20Koma, Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumaweruza molungama

ndi kuyesa mitima ndi maganizo,

lolani kuti ine ndione kuti mwawalipsira,

pakuti mlandu wanga ndawupereka mʼmanja mwanu.

21“Nʼchifukwa chake Yehova akunena za anthu a ku Anatoti amene akufuna kuwononga moyo wako namanena kuti, ‘Usanenere mʼdzina la Yehova, ukatero ife tidzakupha ndi manja athu,’ 22koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzawalanga. Achinyamata awo adzaphedwa ndi lupanga, ana awo aamuna ndi aakazi adzafa ndi njala. 23Sipadzakhala otsala ndi mmodzi yemwe, chifukwa ndidzalanga anthu a ku Anatoti chikadzafika chaka chawo cha chilango.’ ”