民数记 17 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

民数记 17:1-13

亚伦的杖

1耶和华对摩西说: 2“你叫以色列各支派的首领每人拿一根杖来,共十二根,你要在上面写上他们各人的名字。 3你要把亚伦的名字写在利未支派的杖上,每个支派的首领都要有一根杖。 4你要把这些杖放在会幕内的约柜前,就是我跟你会面的地方。 5谁的杖发芽,谁就是我所拣选的人。这样,我必消除以色列人对你们的埋怨。” 6于是,摩西吩咐以色列每个支派的首领把杖都交给他,包括亚伦的杖在内,共十二根。 7他把杖放在放约柜的圣幕里——耶和华面前。 8第二天,摩西进入约柜所在的圣幕里,看见利未支派亚伦的杖不单发了芽,长了花蕾,还开了花,结出熟杏。 9摩西就从耶和华那里拿出所有的杖给以色列人看。他们看后,各位首领便取回自己的杖。 10耶和华对摩西说:“把亚伦的杖放回约柜前,让叛逆之徒引以为戒。这样,你就可以平息他们对我的怨言,使他们不致灭亡。” 11摩西照耶和华的吩咐行了。 12以色列人对摩西说:“完了!我们死定了!我们全死定了! 13凡走近耶和华圣幕的都要死,我们岂不是全都要灭亡吗?”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 17:1-13

Kuphukira kwa Ndodo ya Aaroni

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Yankhula ndi Aisraeli ndipo akupatse ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse. Ulembe dzina la munthu aliyense pa ndodo yake. 3Pa ndodo ya Levi ulembepo dzina la Aaroni, chifukwa pafunika ndodo imodzi ya mtsogoleri pa fuko lililonse. 4Uyike ndodozo mu tenti ya msonkhano, kutsogolo kwa Bokosi la Umboni, kumene ndimakumana nawe. 5Ndodo ya munthu amene ndamusankha idzachita maluwa potero ndidzaletsa madandawulo osatha a Aisraeli otsutsana nawe.”

6Choncho Mose anayankhula ndi Aisraeli, ndipo atsogoleri awo anapereka ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse ndipo ndodo ya Aaroni inali pakati pa ndodo zawozo. 7Mose anayika ndodozo pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano.

8Pa tsiku lotsatira Mose analowa mu tenti ya msonkhanoyo ndipo anaona kuti ndodo ya Aaroni, yomwe inkayimira fuko la Levi, sinangophuka masamba chabe, komanso inachita maluwa nʼkubala zipatso za alimondi. 9Choncho Mose anatulutsa ndodo zonse pamaso pa Yehova napita nazo kwa Aisraeli onse. Iwowo anaziona ndipo munthu aliyense anatenga ndodo yake.

10Yehova anawuza Mose kuti, “Bwezera ndodo ya Aaroni patsogolo pa Bokosi la Umboni, kuti chikhale chizindikiro cha kuwukira kwawo. Zimenezi zidzathetsa kudandaula kwawo kotsutsana nane, kuopa kuti angafe.” 11Mose anachita monga Yehova anamulamulira.

12Aisraeli anati kwa Mose, “Tikufa! Tatayika, tonse tatayika! 13Aliyense woyandikira chihema adzafa. Kodi ndiye kuti tonse tikufa?”