利未记 1 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

利未记 1:1-17

献燔祭的条例

1耶和华在会幕里呼唤摩西,对他说: 2“你把以下条例告诉以色列人。

“如果你们有人献祭给耶和华,要用牛羊作祭物。 3如果用牛作燔祭,必须用毫无残疾的公牛,在会幕门口献上,便可蒙耶和华悦纳。 4献祭者要把手放在牛头上,所献的燔祭便蒙悦纳,为他赎罪。 5他要在耶和华面前宰牛,然后祭司——亚伦的子孙要把牛血洒在会幕门口的祭坛四周。 6献祭者要剥掉牛皮,把牛切成块。 7祭司——亚伦的子孙要在祭坛上生火,把木柴摆在火上, 8然后将肉块、头颅和脂肪都摆在祭坛燃烧的木柴上。 9献祭者要用水洗净牛的内脏和腿。祭司要把这一切都放在坛上焚烧。这是燔祭,是蒙耶和华悦纳的馨香火祭。

10“如果用绵羊或山羊作燔祭,必须用毫无残疾的公羊。 11献祭者要在祭坛北面,在耶和华面前宰羊。祭司——亚伦的子孙要把羊血洒在祭坛四周。 12献祭者将羊切成块后,祭司要把肉块、头颅和脂肪摆在祭坛燃烧的木柴上。 13献祭者要用水洗净羊的内脏和腿。祭司要把这一切都放在坛上焚烧。这是燔祭,是蒙耶和华悦纳的馨香火祭。

14“如果有人用鸟作燔祭,要用斑鸠或雏鸽。 15祭司要把鸟带到祭坛前,拧下鸟头,放在祭坛上焚烧;要在祭坛旁放尽鸟血; 16要除掉鸟的嗉子和羽毛,丢在祭坛东边倒灰的地方。 17祭司要抓着两个翅膀把鸟撕开,但不可撕断,然后把鸟放在坛上焚烧。这是燔祭,是蒙耶和华悦纳的馨香火祭。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 1:1-17

Nsembe Zopsereza

126 Yehova anayitana Mose mu tenti ya msonkhano. Iye anati, 2“Aliyense wa inu ngati abwera ndi nsembe kwa Yehova kuchokera pa ziweto zake, choperekacho chikhale ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi.

3“ ‘Ngati munthu apereka nsembe yopsereza ya ngʼombe, ikhale yayimuna yopanda chilema. Aziyipereka pa khomo la tenti ya msonkhano, kuti Yehova alandire. 4Munthuyo asanjike dzanja lake pa mutu pa nsembe yopserezayo, ndipo idzalandiridwa kuti ikhale yopepesera machimo ake. 5Pambuyo pake aphe ngʼombeyo pamaso pa Yehova, ndipo ansembe, ana a Aaroni, atenge magazi ake ndi kuwawaza mbali zonse za guwa lansembe limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano. 6Munthuyo asende nsembe yopserezayo ndi kuyidula nthulinthuli. 7Ndipo ana a Aaroni, wansembe uja asonkhe moto pa guwa ndi kuyalapo nkhuni pa motopo. 8Kenaka ana a Aaroni, wansembe uja, ayike nthuli za nyamayo, mutu wake pamodzi ndi mafuta omwe pa nkhuni zimene zili paguwapo. 9Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe awotche nyama yonse paguwapo. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chowotcha pa moto, cha fungo lokomera Yehova.

10“ ‘Koma ngati chopereka cha nsembe yopserezayo ndi nkhosa kapena mbuzi kuchokera pa ziweto zake, munthuyo apereke yayimuna yopanda chilema. 11Ayiphere kumpoto kwa guwa, pamaso pa Yehova, ndipo ana a Aaroni amene ndi ansembe, awaze magazi ake mbali zonse za guwalo. 12Kenaka ayidule nyamayo nthulinthuli, ndipo wansembe ayike nthulizo pa guwa, atengenso mutu ndi mafuta omwe, ndipo ayike zonsezi pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa. 13Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe abwere nazo zonse ndi kuzitentha pa guwa. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chotentha pa moto, fungo lokomera Yehova.

14“ ‘Koma ngati chopereka kwa Yehova ndi nsembe yopsereza ya mbalame, ndiye ikhale njiwa kapena mawunda. 15Wansembe abwere nayo ku guwa, ayidule mutu moyipotola ndi kutentha mutuwo pa guwa. Magazi ake awathire pansi kuti ayenderere pambali pa guwa. 16Iye achotse chithokomiro pamodzi ndi nthenga zake zomwe ndi kuzitaya ku malo wotayirako phulusa, kummawa kwa guwalo. 17Kenaka ayingʼambe pakati, koma asachotse mapiko. Ndipo wansembe ayiwotche pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa. Imeneyi ndi nsembe yopsereza, yowotcha pa moto ndiponso ya fungo lokomera Yehova.