撒母耳记上 3 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

撒母耳记上 3:1-21

主呼召撒母耳

1撒母耳跟着以利事奉耶和华。那时候,耶和华的话语稀少,异象也不多。 2一天晚上,老眼昏花的以利正睡在自己的房里。 3上帝的灯还没有熄灭,撒母耳睡在耶和华的殿内,即安放上帝约柜的地方。 4耶和华呼唤撒母耳撒母耳答道:“我在这里!” 5他跑到以利跟前,说:“我来了,你叫我吗?”以利说:“我没有叫你,你去睡吧。”于是,他就回去睡觉。 6耶和华又呼唤撒母耳撒母耳起来到以利跟前,说:“我来了,你叫我吗?”以利答道:“孩子,我没有叫你,回去睡吧。” 7那时,撒母耳还不认识耶和华,耶和华的话还没有向他显明。 8耶和华第三次呼唤他,撒母耳起来,到以利面前,说:“我来了,你叫我吗?”这时候,以利才明白原来是耶和华在呼唤这孩子。 9他就吩咐撒母耳说:“你回去睡吧,若再呼唤你,你就说,‘耶和华啊,请吩咐,仆人恭听。’”于是,撒母耳就回去睡下。 10耶和华来站在那里,再次像刚才一样呼唤:“撒母耳撒母耳!”撒母耳答道:“请吩咐,仆人恭听。” 11耶和华对撒母耳说:“我要在以色列做一件令人震惊的事。 12到时候,我要应验我说的有关以利家的一切预言。 13我对以利说过我要永远惩罚他家,因为他知道自己的儿子亵渎我,却没有制止他们。 14所以,我向以利家起誓说,‘靠祭物或礼物绝不能赎去以利家的罪恶。’”

15撒母耳在床上躺到天亮,然后起来打开耶和华的殿门。他不敢把耶和华的话告诉以利16以利叫他:“撒母耳,我的孩子。”撒母耳答道:“我在这里。” 17以利说:“耶和华对你说了什么?你不要向我隐瞒。如果你隐瞒一句,愿上帝重重地惩罚你。”

18撒母耳就一五一十地告诉了他。以利说:“祂是耶和华,祂看怎样好,就怎样行吧。” 19撒母耳渐渐长大,耶和华与他同在,使他所说的话没有一句落空。 20别示巴,全以色列的人都知道撒母耳被立为耶和华的先知。 21耶和华继续在示罗显现,用自己的话启示撒母耳撒母耳把耶和华的话传遍了以色列

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 3:1-21

Yehova Ayitana Samueli

1Samueli ankatumikira Yehova moyangʼaniridwa ndi Eli. Masiku amenewo mawu a Yehova sankamveka pafupipafupi. Kuona zinthu mʼmasomphenya sikunkachitikanso kawirikawiri.

2Tsiku lina Eli, amene maso anali ofowoka ndi kuti sankatha kuona bwino, anagona pa malo ake. 3Nthawiyi nʼkuti nyale ya Mulungu isanazimitsidwe. Samueli anali gone mu Nyumba ya Yehova, kumene kunali Bokosi la Chipangano cha Mulungu. 4Yehova anayitana Samueli.

Iye anayankha kuti, “Wawa.” 5Ndipo iyeyo anathamangira kwa Eli ndipo anati, “Ndabwera ndamva kuyitana.”

Koma Eli anati, “Ine sindinakuyitane, bwerera kagone.” Ndipo iye anapita kukagona.

6Yehova anayitananso, “Samueli!” Ndipo Samueli anadzuka ndi kupita kwa Eli nati, “Ndabwera popeza ndamva mukundiyitana.”

Eli nati, “Mwana wanga, ine sindinakuyitane, bwerera kagone.”

7Nthawiyi nʼkuti Samueli asanadziwe Yehova ndipo Mawu a Yehova nʼkuti asanawululidwe kwa iye.

8Yehova anayitananso Samueli kachitatu ndipo Samueli anadzuka ndikupita kwa Eli ndipo anati, “Ndabwera popeza mwandiyitana ndithu.”

Apo Eli anazindikira kuti Yehova ndiye ankayitana mnyamatayo. 9Tsono Eli anamuwuza Samueli kuti, “Pita ukagone ndipo akakuyitananso ukanene kuti, ‘Yankhulani Yehova, pakuti mtumiki wanu ndikumvetsera.’ ” Choncho Samueli anapita ndi kukagona pamalo pake.

10Yehova anabwera ndi kuyima pomwepo, ndi kuyitana monga nthawi zina zija, “Samueli! Samueli!”

Ndipo Samueli anayankha, “Yankhulani, pakuti mtumiki wanu akumvetsera.”

11Ndipo Yehova anati kwa Samueli, “Taona, patsala pangʼono kuti ndichite chinthu china mu Israeli chimene chidzadabwitsa aliyense amene adzamve. 12Tsiku limenelo ndidzachitadi zonse zimene ndinayankhula zokhudza banja la Eli kuyambira poyamba mpaka pomaliza. 13Pakuti ndinamudziwitsa kuti Ine ndikhoza kulanga banja lake kwamuyaya chifukwa cha zoyipa zimene ana ake ankadziyipitsa nazo. Iye ankadziwa zimenezi koma osawaletsa. 14Nʼchifukwa chake ndinalumbira kuti, ‘Zoyipa zimene banja la Eli linandichita sizidzafafanizidwa mpaka muyaya ngakhale adzapereke nsembe kapena zopereka zina.’ ”

15Samueli anagona mpaka mmawa. Atadzuka anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova. Iye anachita mantha kumuwuza Eli za masomphenya ake. 16Koma Eli anamuyitana nati, “Samueli mwana wanga.”

Samueli anayankha kuti, “Wawa.”

17Tsono Eli anafunsa kuti, “Yehova wakuwuza chiyani? Usandibisire. Mulungu akulange ndithu ngati undibisira chilichonse cha zimene wakuwuza.” 18Choncho Samueli anamuwuza zonse, sanamubisire kalikonse. Ndipo Eli anati, “Iye ndi Yehova, mulekeni achite chimene chamukomera.”

19Yehova anali ndi Samueli pamene amakula, ndipo zonse zimene ankayankhula zinkachitikadi. 20Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dera la Dani mpaka ku Beeriseba anazindikira kuti Yehova analozadi chala pa Samueli kuti akhale mneneri wake. 21Yehova anapitiriza kuoneka ku Silo, ndipo kumeneko anadziwulula yekha kwa Samueli mwa mawu ake.