撒母耳记上 2 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

撒母耳记上 2:1-36

哈娜的祷告

1哈娜祷告说:

“我的心因耶和华而欢喜,

我的力量因耶和华而倍增,

我的口向敌人夸耀,

我因耶和华的拯救而快乐。

2“耶和华圣洁无比,

独一无二,

没有磐石像我们的上帝。

3不要再骄横傲慢、口出狂言,

因为耶和华鉴察万事,

祂会按着人的行为施行审判。

4勇士的弓被折断,

软弱的变为刚强。

5素来丰衣足食的为糊口而当雇工,

本来食不果腹的却不再挨饿。

不育的妇人现在生了七个孩子,

儿女成群的妇人却子女尽失。

6耶和华掌管生死,

祂使人进入坟墓,也使人起死回生。

7贫穷富足在于祂,

卑微高贵也在于祂。

8祂从灰尘中提拔穷苦的人,

从粪堆里擢升贫贱的人,

使他们与王子同坐,

得享尊荣。

大地的根基属于耶和华,

祂在上面建立了世界。

9祂保护祂的圣民,

使恶人在黑暗中灭亡,

因为得胜不是靠人的勇力。

10跟耶和华对抗的人必被击溃,

祂必从天上用雷击打他。

祂必审判天下,

赐力量给祂所立的君王,

使祂所膏立的人大有权柄。”

11以利加拿返回了拉玛,小撒母耳却留在了示罗,在祭司以利的带领下事奉耶和华。

以利的恶子

12以利的两个儿子为人邪恶,不敬畏耶和华, 13对民众不守自己做祭司的职分。每当民众来献祭,还在煮祭肉的时候,他们的仆人便拿着三齿叉来, 14从罐里、鼎里、釜里或锅里插肉,把插上来的祭肉据为己有。他们这样对待所有到示罗来的以色列人。 15甚至在焚烧脂肪之前,祭司的仆人就来对献祭的人说:“把肉给祭司烤吧!他不要煮过的,只要生的。” 16如果献祭的人答道:“要先焚烧脂肪,之后你可以随便拿。”仆人便会说:“不,你现在就给我,不然我就要抢了。” 17在耶和华的眼中,这两个青年罪恶深重,因为他们轻视献给耶和华的祭物。

18那时年少的撒母耳穿着细麻布的以弗得,在耶和华面前事奉。 19他母亲每年都为他缝一件小外衣,在她和丈夫来献年祭时带给他。 20以利祝福以利加拿和他妻子,对他说:“愿耶和华让你妻子再给你生儿育女,代替她求来并献给耶和华的孩子。”他们就回家去了。 21耶和华眷顾哈娜,她又生了三个儿子和两个女儿。年少的撒母耳在耶和华面前渐渐长大。

22以利年事已高,他听说两个儿子对待以色列人的恶行,以及他们与在会幕门口供职的妇女行淫的事后, 23就对他们说:“你们为什么做这样的事?我从百姓口中听说了有关你们的恶行。 24我儿啊,不可这样,我听到在耶和华的子民中流传着你们的坏名声。 25人若得罪了别人,有上帝为他们调解。但人若得罪了耶和华,谁能为他调解呢?”然而,他们不肯听从父亲的话,因为耶和华决意要杀他们。

26撒母耳渐渐长大,深受耶和华和民众的喜爱。

预言以利家的遭祸

27有一个上帝的仆人来见以利,对他说:“耶和华说,‘你的祖先在埃及被法老奴役的时候,我向他们显现。 28我在以色列各支派中选出你的先祖做我的祭司,在我的祭坛上献祭烧香,穿着以弗得事奉我。我把以色列人献的火祭都赐给你先祖家。 29你们为什么蔑视献给我的祭物和供品?你为什么把你的儿子看得比我还重要,拿我以色列子民所献的上好祭物来养肥自己?’

30“所以,以色列的上帝耶和华宣告说,‘我曾经应许让你们家族永远做我的祭司。’但现在耶和华宣布,‘这绝不可能了。尊重我的,我必尊重他;藐视我的,必遭藐视。 31看啊,时候将到,我要终结你和你家族的力量,你们家族必没有一个老人。 32你必以羡慕的眼光看着我赐福以色列人,你家中却永远没有一个老人。 33我不会把你家中的人从我坛前灭绝,但留下来的人必使你哭瞎双眼、伤心欲绝。你的子孙必中年夭亡。 34你的两个儿子何弗尼非尼哈必死在同一天,这就是我言出必行的记号。 35我要为自己立一位忠心的祭司,他必照我的心意行事。我要赐福给他的后代,他必永远服侍我膏立的王。 36那时,你家存留下来的人要在他面前下拜,乞讨银子和饼,并恳求说,请给我一个祭司的职位以便糊口!’”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 2:1-36

Pemphero la Hana

1Ndipo Hana anapemphera nati,

“Moyo wanga ukukondwera mwa Yehova;

Ndiyenda mwa tukumutukumu chifukwa cha Yehova.

Pakamwa panga pakula ndi kuseka adani anga mowanyogodola.

Ndikukondwa chifukwa mwandipulumutsa.

2“Palibe wina woyera ngati Yehova,

palibe wina koma inu nokha,

palibe thanthwe lofanana ndi Mulungu wathu.

3“Musandiyankhulenso modzitama,

pakamwa panu pasatuluke zonyada,

pakuti Yehova ndi Mulungu wanzeru,

ndipo ndiye amene amayesa ntchito za anthu onse.

4“Mauta a anthu ankhondo athyoka

koma anthu ofowoka avala dzilimbe.

5Amene kale anali okhuta tsopano akukagula chakudya,

koma iwo amene anali ndi njala sakumvanso njala.

Amene anali wosabereka, wabereka ana aamuna asanu ndi awiri,

koma iye wobereka ana ambiri watsala yekha.

6“Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo,

amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso.

7Yehova amasaukitsa ndipo amalemeretsa,

amatsitsa ndipo amakweza.

8Iye amakweza osauka kuwachotsa pa fumbi,

ndipo amachotsa anthu osowa pa dzala.

Iye amawakhazika pamodzi ndi ana a mafumu,

amawapatsa mpando waulemu.

“Pakuti nsanamira za dziko lapansi ndi za Yehova,

anakhazika dziko lapansi pa nsanamirazo.

9Iye adzateteza moyo wa anthu okhulupirika

koma anthu oyipa adzawonongedwa mu mdima.

“Pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.

10Yehova adzaphwanya omutsutsa.

Adzawaopsa ndi bingu kuchokera kumwamba;

Yehova adzaweruza mathero a dziko lapansi.

“Koma adzapereka mphamvu kwa mfumu yake,

adzakuza mphamvu za odzozedwa wake.”

11Tsono Elikana anapita ku mudzi kwawo ku Rama, koma mnyamatayo amatumikira Yehova pansi pa ulamuliro wa wansembe Eli.

Kuyipa kwa Ana a Eli

12Ana a Eli anali ana achabechabe pakuti samasamala za Yehova. 13Ndipo chizolowezi cha ansembe pakati pa anthu chinali motere kuti pamene munthu aliyense ankapereka nsembe ndipo nyama ija ikuwira pa moto, mtumiki wa wansembe ankabwera ndi chifoloko cha mano atatu mʼdzanja lake. 14Iye ankachipisa mu mʼphikamo, ndipo wansembeyo amatenga chilichonse chimene folokoyo yabaya. Umu ndi mmene ansembewo amachitira ndi Aisraeli onse amene amabwera ku Silo. 15Ndipo ngakhale mafuta asanatenthedwe, mtumiki wansembe amabwera ndi kunena kwa munthu amene akupereka nsembeyo kuti, “Ndipatse nyama kuti ndiwotche, pakuti Yehova salandira nyama yophika koma yayiwisi.”

16Ngati munthuyo anena kuti, “Apseretu mafuta poyamba, ndipo kenaka mutenge mmene mufunira,” mtumikiyo amayankha kuti, “Ayi ndipatse tsopano lino. Ngati sutero, ine nditenga molanda.”

17Tchimo la ana a Eli linali lalikulu kwambiri pamaso pa Yehova pakuti iwo amanyoza nsembe za Yehova.

18Koma Samueli amatumikira pamaso pa Yehova atavala efodi ya nsalu yofewa yosalala. 19Chaka chilichonse amayi ake ankamusokera kamkanjo ndi kukamupatsa akamapita ndi mwamuna wake kukapereka nsembe za pa chaka. 20Tsono Eli amadalitsa Elikana ndi mkazi wake ndi mawu akuti “Yehova akupatseni ana mwa mkazi uyu kulowa mʼmalo mwa amene anapempha ndi kumupereka kwa Yehova.” 21Ndipo Yehova anamukomera mtima Hana. Anakhala ndi pathupi ndi kubereka ana aamuna atatu ndi ana aakazi awiri. Ndipo Samueli ankakula pamaso pa Yehova.

22Tsono Eli anakalamba kwambiri. Iye ankamva zonse zimene ana ake aamuna ankachitira Aisraeli onse, ndiponso kuti ankagona ndi akazi pa chipata cha tenti ya msonkhano. 23Choncho anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuchita zinthu zotere? Ine ndikumva kuchokera kwa anthu onse za zoyipa zanuzo. 24Ayi, ana anga si mbiri yabwino imene ndikumva anthu a Mulungu akufalitsa. 25Ngati munthu alakwira munthu mnzake, mwina Mulungu adzamupepesera, koma ngati munthu achimwira Yehova adzamupepesera ndani?” Koma ana ake sanamvere kudzudzula kwa abambo awo, pakuti chinali cholinga cha Yehova kuti awaphe.

26Ndipo mnyamata Samueli anapitirira kukula mu msinkhu, ndipo ankapeza kuyanja pamaso pa Yehova ndi anthu.

Uneneri Wotsutsa Banja la Eli

27Tsiku lina munthu wa Mulungu anabwera kwa Eli ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi Ine sindinadziwulule ndekha kwa banja la kholo lako pamene iwo anali akapolo a Farao ku Igupto? 28Ndipo ndinamusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti akhale wansembe wanga ndi kuti azipita pa guwa langa la nsembe, kufukiza Lubani ndi kuvala efodi pamaso panga. Ndinapatsa banja la abambo ako gawo la nsembe zonse zopsereza zimene Aisraeli amapereka. 29Nʼchifukwa chiyani ukunyoza nsembe ndi zopereka zanga zimene ndinalamula? Nʼchifukwa chiyani ukupereka ulemu kwa ana ako kuposa Ine podzinenepetsa nokha ndi zopereka zabwino kwambiri za nsembe zimene Aisraeli amapereka?’ ”

30“Paja Ine Yehova Mulungu wa Israeli ‘Ndinalonjeza kuti anthu a pa banja lako ndi a pa banja la abambo ako azidzanditumikira nthawi zonse.’ Koma tsopano ndikuti, ‘Zonsezi zithe!’ Tsopano anthu amene amandilemekeza Inenso ndidzawalemekeza koma iwo amene amandinyoza Ine ndidzawanyoza. 31Nthawi ikubwera imene ndidzachotsa anyamata ako ndi anyamata a pa banja la abambo ako, kotero kuti sipadzakhala munthu wokalamba pa banja lako. 32Pa mavuto ako udzayangʼana ndi maso ansanje zabwino zimene ndidzachitira Aisraeli ena. Mʼbanja lako simudzapezeka munthu wokalamba. 33Komabe pa banja lako mmodzi yekha ndidzamuleka wosamuchotsa kuti azidzanditumikira. Iyeyu azidzakuliritsa ndi kukumvetsa chisoni. Koma ena onse pa banja lako adzafa akanali aangʼono.”

34“ ‘Ndipo chimene chidzachitike kwa ana ako awiriwa, Hofini ndi Finehasi, chidzakhala chizindikiro kwa iwe. Onse awiri adzafa pa tsiku limodzi. 35Pambuyo pake ndidzasankha wansembe wokhulupirika, amene adzachita zimene zili mu mtima ndi mʼmaganizo mwanga. Ndidzakhazikitsa banja lako kolimba ndipo adzatumikira pamaso pa wodzozedwa wanga nthawi zonse. 36Ndipo aliyense wotsala wa banja lako adzabwera ndi kugwada pamaso pake kupempha ndalama kapena chakudya.’ Adzati, ‘Chonde ndiloleni kuti ndizithandizako pa ntchito iliyonse ya unsembe kuti ndipeze chakudya.’ ”