启示录 11 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

启示录 11:1-19

两位见证人

1有一根杆子赐给我当量尺,同时有声音吩咐我说:“起来,量一量上帝的殿和祭坛,并数点在殿里敬拜的人。 2你不用量圣殿的外院,因为这部分已经给了外族人,他们要践踏圣城四十二个月。 3我要赐权柄给我的两个见证人,他们将身穿麻衣,传道一千二百六十天。”

4这两位见证人就是竖立在世界之主面前的那两棵橄榄树和两座灯台。 5若有人要伤害他们,他们便从口中喷出火焰,烧灭敌人;若有人企图加害他们,必定会这样被杀。 6他们拥有权能,在传道期间可以关闭天空使雨不降在地上,又有权使水变成血,并随时用各样的灾祸击打世界。

7当他们做完见证以后,从无底坑上来的兽要和他们交战,并战胜他们,把他们杀掉。 8他们便陈尸在大城的街上,这大城按寓意名叫所多玛,又名埃及,是他们的主被钉在十字架上的地方。 9三天半之久,他们的尸体不得埋葬,各民族、各部落、各语言族群、各国家的人都观看他们的尸体。 10地上万民便兴高采烈,互相送礼道贺,因为这两位先知曾使地上的人受苦。

11三天半过后,上帝的生命之气进入二人里面,他们便站立起来。看见的人都害怕极了! 12接着天上有大声音呼唤他们说:“上这里来!”他们就在敌人的注视下驾云升上天去。 13就在那一刻,发生了强烈的地震,那座城的十分之一倒塌了,因地震死亡的共七千人,生还者都在恐惧中将荣耀归给天上的上帝。

14第二样灾难过去了,第三样灾难又接踵而来!

第七位天使吹号

15第七位天使吹响号角的时候,天上有大声音说:“世上的国度现在已经属于我们的主和祂所立的基督了。祂要做王,直到永永远远。” 16在上帝面前,坐在自己座位上的二十四位长老都一同俯伏敬拜上帝,说:

17“主啊!昔在、今在的全能上帝啊!

我们感谢你,

因你已施展大能做王了。

18世上的列国曾向你发怒,

现在是你向他们发烈怒的日子了。

时候已到,你要审判死人,

你要赏赐你的奴仆、先知、圣徒

和一切不论尊卑敬畏你名的人,

你要毁灭那些毁坏世界的人。”

19那时,天上上帝的圣殿敞开了,殿内的约柜清晰可见,又有闪电、巨响、雷鸣、地震和大冰雹。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 11:1-19

Mboni Ziwiri

1Ndinapatsidwa bango longa ndodo yoyezera ndipo ndinawuzidwa kuti, “Pita, kayeze Nyumba ya Mulungu ndi guwa lansembe, ndipo ukawerenge anthu opembedza mʼNyumbamo. 2Koma bwalo lakunja ulisiye, usaliyeze chifukwa linaperekedwa kwa a mitundu ina. Iwo adzawupondereza mzinda woyerawo kwa miyezi 42. 3Ndipo ndidzapereka mphamvu kwa mboni zanga ziwiri, zitavala ziguduli, ndipo kwa masiku 1,260 zidzakhala zikulalikira.” 4Mboni ziwirizo ndi mitengo iwiri ya olivi ndi zoyikapo nyale ziwiri zija zimene zili pamaso pa Ambuye wa dziko lapansi. 5Ngati wina atafuna kuzipweteka mbonizo, moto umatuluka mʼkamwa mwawo ndikuwononga adani awo. 6Mbonizo zili ndi mphamvu yomanga mvula kuti isagwe pa nthawi imene akulalikirayo; ndipo zili ndi mphamvu yosanduliza madzi kukhala magazi ndi yokantha dziko lapansi ndi miliri ya mitundumitundu nthawi iliyonse imene zingafune.

7Tsono zikadzatsiriza umboni wawowo, chirombo chotuluka mʼChidzenje chakuya chija chidzachita nawo nkhondo nʼkuzigonjetsa mpaka kuzipha. 8Mitembo yawo idzakhala ili gone pabwalo la mu mzinda waukulu umene mozimbayitsa umatchedwa Sodomu ndi Igupto, kumenenso Ambuye wawo anapachikidwako. 9Kwa masiku atatu ndi theka, anthu ochokera ku mtundu uliwonse, fuko lililonse, chiyankhulo chilichonse ndi dziko lililonse, azidzayangʼanitsitsa mitembo yawoyo koma adzakana kuyikwirira. 10Anthu okhala pa dziko lapansi adzasangalala nazo zimenezi. Adzachita chikondwerero ndi kutumizirana mphatso, chifukwa aneneri awiri amenewa ankasautsa anthu okhala pa dziko lapansi.

11Koma patapita masiku atatu ndi theka aja, mpweya wopatsa moyo wochoka kwa Mulungu unalowa mwa aneneriwo, ndipo anayimirira, ndipo amene anawaona anachita mantha aakulu. 12Kenaka aneneri aja anamva mawu ofuwula ochokera kumwamba owawuza kuti, “Bwerani kuno.” Ndipo anapitadi kumwamba mu mtambo adani awo aja akuwaona.

13Nthawi yomweyo panachitika chivomerezi choopsa mwakuti chigawo chimodzi cha magawo khumi a mzinda chinagwa. Anthu 7,000 anaphedwa ndi chivomerezicho, ndipo opulumukawo anachita mantha kwambiri nayamba kutamanda Mulungu wakumwamba.

14Tsoka lachiwiri lapita; koma tsoka lachitatu likubwera posachedwapa.

Lipenga Lachisanu ndi Chiwiri

15Mngelo wachisanu ndi chiwiri anawomba lipenga lake, ndipo kumwamba kunamveka mawu ofuwula amene anati,

“Ufumu wa dziko lapansi uli

mʼmanja mwa Ambuye athu ndi Khristu wake uja,

ndipo adzalamulira mpaka muyaya.”

16Ndipo akuluakulu 24 aja okhala pa mipando yawo yaufumu pamaso pa Mulungu, anadzigwetsa chafufumimba napembedza Mulungu 17Iwo anati,

“Ife tikuyamika Inu Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse,

amene mulipo ndipo munalipo,

chifukwa mwaonetsa mphamvu yanu yayikulu,

ndipo mwayamba kulamulira.

18A mitundu ina anapsa mtima;

koma yafika nthawi yoonetsa mkwiyo.

Nthawi yakwana yoweruza anthu akufa,

yopereka mphotho kwa atumiki anu, aneneri,

anthu oyera mtima anu ndi amene amaopa dzina lanu,

wamngʼono pamodzi ndi wamkulu yemwe.

Yafika nthawi yowononga amene awononga dziko lapansi.”

19Pamenepo anatsekula Nyumba ya Mulungu kumwamba ndipo mʼkati mwake munaoneka Bokosi la Chipangano. Kenaka kunachita mphenzi, phokoso, mabingu, chivomerezi ndipo kunachita mkuntho wamatalala akuluakulu.