启示录 10 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

启示录 10:1-11

天使与小书卷

1我看见另一位大力天使从天而降。他身披云霞,头顶彩虹,脸如太阳,双腿如火柱, 2手中拿着一卷打开了的小书卷,右脚踏在海中,左脚踏在地上。 3他大喊的时候,声如狮吼,之后有七声雷鸣。 4我正要将雷鸣的意思记录下来,就听见天上有声音说:“你要封住七声雷鸣所说的事,别写下来。”

5我刚才所见的那位脚踏海洋和陆地的天使向天举起右手, 6凭着活到永永远远、创造天地海洋和其中一切的上帝起誓说:“必不再耽延了。 7等第七位天使吹响号角时,上帝奥秘的计划就实现了,正如上帝向祂的奴仆——众先知所宣告的。”

8先前从天上对我说话的声音又吩咐我:“你去,从那位脚踏海洋陆地的天使手中把展开的小书卷拿来。”

9于是,我走到那天使面前,请他将小书卷给我。他对我说:“拿去,把它吃了。你的腹中会感到苦涩,可是你口中会觉得甘甜如蜜。” 10我就从天使手中接过小书卷,将它吃了,我口中果然甘甜如蜜,之后腹中觉得苦涩。 11那天使又对我说:“你必要再对许多民族、国家、语言族群、君王说预言。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 10:1-11

Mngelo ndi Kabuku

1Kenaka ndinaona mngelo wina wamphamvu akutsika kuchokera kumwamba. Anavala mtambo ndipo anali ndi utawaleza pamutu pake. Nkhope yake inali ngati dzuwa, ndipo miyendo yake inali ngati mizati yamoto. 2Mʼdzanja lake munali kabuku kakangʼono kotsekulidwa. Phazi lake lamanja linaponda mʼnyanja ndipo phazi lake lamanzere linaponda pa mtunda. 3Mngeloyo anafuwula kwambiri ngati kubangula kwa mkango. Atangofuwula, kunamveka kugunda kwa mabingu asanu ndi awiri. 4Mabingu asanu ndi awiriwo atangogunda, ine ndinkati ndizilemba; koma ndinamva mawu kuchokera kumwamba kuti, “Zisunge mu mtima zimene mabingu asanu ndi awiriwo anena ndipo usazilembe.”

5Kenaka mngelo amene ndinamuona ataponda mʼnyanja ndi ku mtunda uja, anakweza dzanja lake lamanja kumwamba. 6Mngeloyo analumbira mʼdzina la Iye wokhala ndi moyo mpaka muyaya, amene analenga kumwamba ndi zonse zili kumeneko, dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo, nati, “Pasakhalenso zochedwa tsopano! 7Koma patsala pangʼono kuti mngelo wachisanu ndi chiwiri uja awombe lipenga lake, chinsinsi cha Mulungu chidzachitika monga momwe analengezera kwa atumiki ake, aneneri.”

8Pamenepo mawu amene ndinamva kuchokera kumwamba aja, anandiyankhulanso, anati, “Pita katenge buku lotsekulidwalo mʼdzanja la mngelo amene waponda pa nyanja ndi pa mtundayo.”

9Choncho ndinapita kwa mngeloyo ndipo ndinamupempha kuti andipatse kabukuko. Iye anati, “Tenga, idya. Mʼmimba mwako kaziwawa koma mʼkamwa mwako kazizuna ngati uchi.” 10Ndinatenga kabukuko mʼdzanja la mngeloyo ndipo ndinadyadi. Mʼkamwa mwanga kankazuna ngati uchi, koma nditakameza, mʼmimbamu munkawawa. 11Ndipo anandiwuza kuti, “Iwe uyenera kulalikiranso za mitundu yambiri ya anthu, za mayiko, ziyankhulo ndi za mafumu.”