创世记 10 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

创世记 10:1-32

挪亚三个儿子的后代

1洪水以后,挪亚的儿子雅弗都生养了儿女,以下是他们的后代。

2雅弗的儿子是歌篾玛各玛代雅完土巴米设提拉3歌篾的儿子是亚实基拿利法陀迦玛4雅完的儿子是以利沙他施基提多单5雅弗的这些后裔按宗族、语言和民族分散在各海岛。

6的儿子是古实麦西10:6 麦西”希伯来文是Mizraim,就是“埃及”,13节亦同。迦南7古实的儿子是西巴哈腓拉撒弗他拉玛撒弗提迦拉玛的儿子是示巴底但

8古实也是宁录之父,宁录是世上第一位勇士, 9在耶和华眼中是个孔武有力的猎人,因此有俗话说:“要像宁录那样在耶和华眼中是个孔武有力的猎人。” 10他首先在示拿地区的巴别以力亚甲甲尼各地建国, 11后来扩展到亚述,在那里建立了尼尼微利河伯迦拉各城, 12又在尼尼微迦拉之间建立了利鲜大城。

13麦西的后代有路低人、亚拿米人、利哈比人、拿弗土希人、 14帕斯鲁细人、迦斯路希人和迦斐托人。非利士人是迦斐托人的后代。

15迦南生长子西顿和次子16他的后代还有耶布斯人、亚摩利人、革迦撒人、 17希未人、亚基人、西尼人、 18亚瓦底人、洗玛利人和哈马人。后来迦南各宗族散居在各地。 19迦南的疆域从西顿基拉耳延伸,远至迦萨,再向所多玛蛾摩拉押玛洗扁延伸,远至拉沙20以上记载的都是的子孙,他们根据自己的宗族、语言、地域和民族散居各处。

21雅弗的哥哥希伯子孙的祖先。 22的儿子是以拦亚述亚法撒路德亚兰23亚兰的儿子是乌斯户勒基帖玛施24亚法撒沙拉沙拉希伯25希伯有两个儿子,一个名叫法勒,意思是分开,因为那时人们分地而居。法勒的兄弟叫约坍26约坍亚摩答沙列哈萨玛非耶拉27哈多兰乌萨德拉28俄巴路亚比玛利示巴29阿斐哈腓拉约巴。这些都是约坍的儿子。 30他们居住的地方,从米沙直到东边的西发山区。 31以上记载的都是的子孙,他们按着自己的宗族、语言、地域和民族散居各处。

32这些人都是洪水以后挪亚三个儿子所生的子孙,他们按着自己的族系散居在各地,后来成为地上不同的民族。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 10:1-32

Mndandanda wa Mitundu ya Anthu

1Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.

Banja la Yafeti

2Ana aamuna a Yafeti anali:

Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.

3Ana aamuna a Gomeri anali:

Asikenazi, Rifati ndi Togarima.

4Ana aamuna a Yavani anali:

Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu. 5(Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).

Banja la Hamu

6Ana aamuna a Hamu anali:

Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.

7Ana aamuna a Kusi anali:

Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka.

Ana aamuna a Raama anali:

Seba ndi Dedani.

8Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi. 9Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.” 10Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara. 11Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala, 12ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.

13Igupto ndiye kholo la

Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu, 14Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).

15Kanaani anabereka mwana wake wachisamba,

Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti; 16Ayebusi, Aamori, Agirigasi; 17Ahivi, Aariki, Asini, 18Aaravadi, Azemari ndi Ahamati.

Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse, 19mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.

20Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.

Banja la Semu

21Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.

22Ana aamuna a Semu anali:

Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.

23Ana aamuna a Aramu anali:

Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.

24Aripakisadi anabereka Sela,

ndipo Selayo anabereka Eberi.

25A Eberi anabereka ana aamuna awiri:

Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.

26Yokitani anabereka

Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera, 27Hadoramu, Uzali, Dikila, 28Obali, Abimaeli, Seba, 29Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.

30Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.

31Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.

32Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.