列王纪上 5 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

列王纪上 5:1-18

预备建造圣殿

1泰尔希兰素来与大卫修好,他听说以色列人膏立了所罗门继承大卫的王位,就遣使者来见所罗门2所罗门也派人去见希兰,说: 3“你知道,我父大卫因周围战事连连,未能为他的上帝耶和华建殿,要等到耶和华使仇敌伏在他脚下后再建。 4现在我的上帝耶和华使我四境太平,内外无忧, 5我想为我的上帝耶和华建殿,因为耶和华曾对我父大卫说,‘我必使你的儿子继承你的王位,他必为我的名建殿。’ 6请你命人为我砍伐黎巴嫩的香柏木。我会派人帮助你的人,并按你的要求付你的人工钱。因为你知道,我们没有人像西顿人那样善于砍伐树木。”

7希兰听了所罗门的话后,非常高兴,说:“今天当赞美耶和华!祂赐给大卫一个有智慧的儿子治理这伟大的民族。” 8他派人回复所罗门说:“我已收到你派人带来的口信。我一定会照你的心愿提供香柏木和松木。 9我的工人会将这些木料从黎巴嫩扎成木筏,经海道运到你指定的地点。木筏拆散以后,你就可以点收了。你也要成全我的心愿,供应我家食粮。” 10于是,希兰供应所罗门需用的香柏木和松木, 11所罗门每年供应希兰四百四十万升麦子和四千四百升橄榄油。 12耶和华照着应许赐给所罗门智慧。他跟希兰修好,缔结盟约。

13所罗门王从以色列征集了三万劳工, 14派他们每月轮班到黎巴嫩工作,每班一万人,在黎巴嫩一个月,在家两个月。亚多尼兰做他们的总管。 15所罗门又征用了七万名搬运工,八万名在山上凿石的匠人。 16此外,他还派了三千三百名监工,监督工人做工。 17他们按照王的命令在山上凿出珍贵的巨石,用来作殿的根基。 18于是,所罗门希兰的工匠及迦巴勒人凿好石头,备好木料,准备建殿。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 5:1-18

Kukonzekera Kumanga Nyumba ya Mulungu

1Hiramu mfumu ya ku Turo atamva kuti Solomoni wadzozedwa kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo ake Davide, anatumiza akazembe ake kwa Solomoni, chifukwa mfumu Hiramu inali pa ubale wabwino ndi Davide nthawi zonse. 2Solomoni anabweza mawu awa kwa Hiramu:

3“Inu mukudziwa kuti chifukwa cha nkhondo zimene zinkachokera ku mbali zonse kulimbana ndi abambo anga, iwo sanathe kumangira Nyumba Yehova Mulungu wawo, mpaka Yehova atawayika adani awo pansi pa ulamuliro wawo. 4Koma tsopano Yehova Mulungu wanga wandipatsa mtendere mbali zonse za dziko ndipo ndilibe mdani kapena chovuta chilichonse. 5Choncho ine ndikufuna kumangira nyumba Yehova Mulungu wanga, monga momwe Iye anawuzira abambo anga Davide kuti, ‘Mwana wako amene ndidzamukhazike pa mpando waufumu mʼmalo mwako ndiye adzandimangire Nyumba.’

6“Choncho lamulani kuti andidulire mikungudza ya ku Lebanoni. Anthu anga adzagwira ntchito imeneyo pamodzi ndi anthu anuwo, ndipo ine ndidzalipira anthu anuwo malipiro amene inu mungakhazikitse. Inu mukudziwa kuti ife tilibe anthu aluso locheka matabwa monga Asidoni.”

7Hiramu anakondwa kwambiri atamva uthenga wa Solomoni ndipo anati, “Lero Yehova atamandike chifukwa wapatsa Davide mwana wanzeru kuti alamulire mtundu waukuluwu.”

8Tsono Hiramu anabweza mawu awa kwa Solomoni:

“Ndalandira uthenga umene mwanditumizira ndipo ine ndidzachita zonse zimene mukufuna pokupatsani mitengo ya mkungudza ndi payini. 9Anthu anga adzatsika nayo kuchokera ku Lebanoni mpaka ku nyanja, ndipo adzayiyandamitsa pa nyanja mpaka ku malo amene munene. Kumeneko ndidzayimasula ndipo mudzayitenga. Ndipo inu mudzakwaniritsa chokhumba changa pondipatsa chakudya cha banja langa laufumu.”

10Motero Hiramu anapereka kwa Solomoni mitengo yonse ya mkungudza ndi payini imene ankayifuna, 11ndipo Solomoni anamupatsa Hiramu mitanga ya tirigu 20,000 ngati chakudya cha pa nyumba yake, kuwonjezera pa migolo ya mafuta a olivi yokwana 20,000. Solomoni anapitiriza kupereka zimenezi chaka ndi chaka. 12Yehova anamupatsa Solomoni nzeru monga momwe analonjezera. Panali ubale wa mtendere pakati pa Solomoni ndi Hiramu, ndipo awiriwa anachita pangano.

13Mfumu Solomoni inasonkhanitsa anthu ogwira ntchito ya thangata mʼdziko lonse la Israeli ndipo anthu athangatawo analipo 30,000. 14Iye ankatumiza anthu 10,000 ku Lebanoni pa mwezi mosinthanasinthana, kotero kuti ankakhala ku Lebanoniko mwezi umodzi ndipo kwawo ankakhalako miyezi iwiri. Adoniramu ndiye ankayangʼanira ogwira ntchito yathangatayo. 15Solomoni anali ndi anthu amtengatenga 70,000, anthu 80,000 osema miyala ku mapiri, 16ndi akapitawo 33,000 amene ankayangʼanira ntchitoyi ndiponso anthu ogwira ntchito zina. 17Molamulidwa ndi mfumu, anakumba ndi kusema miyala ikuluikulu kwambiri yoti akamangire maziko a Nyumba ya Mulungu. 18Amisiri a Solomoni ndi a Hiramu ndiponso anthu a ku Gebala anasema miyala ndi kukonza matabwa ndi miyala yomangira Nyumba ya Mulungu.