使徒行传 17 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

使徒行传 17:1-34

保罗在帖撒罗尼迦传道

1保罗西拉经过暗非坡里亚波罗尼亚,到了帖撒罗尼迦。那里有犹太人的会堂。 2保罗照以往的习惯进入会堂,一连三个安息日引用圣经与当地人讨论, 3解释、证明基督必须受害,然后从死里复活,又说:“我向你们宣讲的这位耶稣就是基督。” 4不少人被说服,成为保罗西拉的同道,其中有许多是敬畏上帝的希腊人和有地位的妇女。

5那些不信主的犹太人却妒火中烧,他们召集了一群市井无赖,在城里引发骚乱,闯进耶孙的家企图把保罗西拉揪出来示众。 6他们找不到保罗西拉,就把耶孙和几个弟兄拉到当地官员面前,高喊:“那些搅乱天下的人到我们这里来了, 7耶孙接待了他们。他们违抗凯撒的命令,说另有一个王叫耶稣。” 8百姓和当地官长听后,深感不安。 9于是,官长命耶孙等人缴纳保释金,然后释放了他们。

庇哩亚人接受福音

10弟兄姊妹在夜间把保罗西拉送往庇哩亚。他们二人一到,就进了犹太会堂。 11当地的人比帖撒罗尼迦人通情达理,非常乐意接受真道,还天天查考圣经,研究这道是否正确。 12结果有很多人信了,包括不少有名望的希腊妇女和男子。 13可是,帖撒罗尼迦犹太人听到保罗庇哩亚宣扬上帝的道,就赶来怂恿、煽动众人。 14庇哩亚的弟兄姊妹立刻送保罗到海边,西拉提摩太仍然留在庇哩亚15护送保罗的人一直把他送到雅典,然后带着保罗的口信回庇哩亚,交代西拉提摩太尽快赶去雅典保罗会合。

保罗在雅典传道

16保罗雅典等候他们的时候,看见满城都是偶像,心里非常着急。 17于是,他在会堂跟犹太人和虔诚的外族人辩论,每天在广场上跟遇见的人辩论。 18还有一些伊壁鸠鲁斯多亚学派的哲学家和保罗争论,有人嘲笑他说:“这人在胡说八道些什么呀?”还有人说:“他好像在宣扬外国的神明。”他们这样说是因为保罗在传讲耶稣和祂复活的福音。 19他们带保罗到一个称为亚略·巴古的论坛,问他:“我们可以知道你所教导的这个新道理吗? 20你的言论确实稀奇,我们很想知道个究竟。”

21这些雅典人和侨居在那里的人没有别的嗜好,只喜欢谈论和打听一些新奇的事。

22保罗亚略·巴古论坛中站起来说:“各位雅典人,我看得出你们在各方面都非常虔诚。 23我在街上走的时候,观察了你们所敬拜的对象,发现一座祭坛上面写着‘献给未知之神’。这位你们不认识却在敬拜的神明,我现在介绍给你们。

24“这位创造宇宙万物的上帝是天地的主宰,并不住在人手建造的庙宇里, 25也不需要人的侍奉,因为祂一无所缺。祂将生命、气息和万物赐给世人。 26祂从一人造出万族,让他们散居世界各地,又预先定下他们的期限和居住的疆界, 27以便他们在其间寻求祂,或许他们可以摸索着找到祂。祂原本就离我们各人不远, 28我们的生活、行动和存在都靠祂,你们的诗人也说过,‘我们是祂的子孙。’ 29我们既然是上帝的子孙,就不该认为上帝是人凭手艺和想象用金、银、石头所雕刻的样子。

30“上帝以往不鉴察世人的无知,现在则命令世上所有的人都要悔改。 31因为祂已经定了日子,要借祂所设立的人按公义审判这个世界。祂叫那人从死里复活,给了全人类可信的凭据。”

32听见保罗提到死人复活的事,有些人就嘲笑他,还有些人说:“我们改天再听你讲这个。” 33于是保罗离开了他们。 34不过,也有人跟随保罗,信了耶稣,其中有亚略·巴古的会员丢尼修和一位名叫戴玛丽的妇人及其他人。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 17:1-34

Paulo ku Tesalonika

1Atadutsa ku Amfipoli ndi Apoloniya, anafika ku Tesalonika, kumene kunali sunagoge ya Ayuda. 2Paulo, monga mwachizolowezi chake, analowa mʼsunagoge, ndipo anakambirana nawo Mawu a Mulungu kwa masabata atatu, 3kuwafotokozera ndi kuwatsimikizira kuti Khristu anayenera kufa ndi kuuka. Iye anati, “Yesu amene ndikukulalikirani ndiye Khristu.” 4Ena mwa Ayuda anakopeka mtima ndipo anatsatira Paulo ndi Sila, monganso linachitira gulu lalikulu la Agriki woopa Mulungu, pamodzi ndi amayi odziwika ambiri.

5Koma Ayuda ena anachita nsanje; kotero anasonkhanitsa anthu akhalidwe loyipa ochokera pa msika ndipo napanga gulu nayambitsa chipolowe mu mzindawo. Anathamangira ku nyumba ya Yasoni kukafuna Paulo ndi Sila kuti awabweretse pa gulu la anthu. 6Koma atalephera kuwapeza, anakokera Yasoniyo ndi abale ena ku bwalo la akulu a mzindawo akufuwula kuti, “Anthu awa, Paulo ndi Sila, amene akhala akusokoneza dziko lonse lapansi, tsopano afikanso kuno. 7Yasoni ndiye anawalandira mʼnyumba mwake. Onsewa akuchita zotsutsana ndi malamulo a Kaisara pomanena kuti palinso mfumu ina, yotchedwa Yesu.” 8Atamva zimenezi, gulu la anthu ndi akulu a mzinda anavutika mu mtima. 9Iwo analipiritsa Yasoni ndi anzakewo ndipo anawamasula.

Ku Bereya

10Mdima utagwa, abale anatumiza Paulo ndi Sila ku Bereya. Atafika kumeneko anapita ku sunagoge ya Ayuda. 11Tsopano anthu a ku Bereya anali akhalidwe labwino kusiyana ndi Atesalonika, pakuti iwo analandira mawu ndi chidwi chachikulu ndipo ankasanthula Malemba tsiku ndi tsiku kuti aone ngati zimene ankanena Paulozo zinali zoona. 12Ayuda ambiri anakhulupirira, monga anachitiranso amayi ndi amuna ambiri odziwika a Chigriki.

13Ayuda a ku Tesalonika atadziwa kuti Paulo akulalikira Mawu a Mulungu ku Bereya, anapitanso kumeneko, ndi kuwutsa mitima ya anthu nayambitsa chisokonezo. 14Nthawi yomweyo abale anatumiza Paulo ku nyanja koma Sila ndi Timoteyo anatsalira ku Bereya. 15Anthu amene anamuperekeza Paulo nafika naye ku Atene, ndipo anabwerera ku Bereya atawuzidwa kuti Sila ndi Timoteyo amutsatire msanga.

Ku Atene

16Paulo akudikira Timoteyo ndi Sila ku Atene, anavutika mu mtima kwambiri poona kuti mzindawo unali odzaza ndi mafano. 17Tsono anakambirana ndi Ayuda ndi Agriki amene amaopa Mulungu mʼsunagoge, komanso anthu amene amapezeka pa msika tsiku ndi tsiku ndi ena amene amakumana nawo. 18Gulu la Aepikureya ndi Astoiki, anthu anzeru, anayamba kutsutsana naye. Ena a iwo anafunsa kuti, “Kodi wolongololayu akufuna kunena chiyani?” Enanso anati, “Akuoneka ngati akulalikira milungu yachilendo.” Iwo ananena zimenezi chifukwa Paulo amalalikira Uthenga Wabwino wa Yesu ndi kuuka kwa akufa. 19Kenaka iwo anamutenga nafika naye ku bwalo la Areopagi kumene anamufunsa kuti, “Kodi tingadziweko chiphunzitso chatsopano chimene ukuchifotokozachi? 20Iwe ukubweretsa zinthu zina zachilendo mʼmakutu mwathu, ndipo ife tikufuna tidziwe tanthauzo lake.” 21Atene onse ndi alendo amene amakhala kumeneko samachita kanthu kena koma kufotokoza ndi kumvera fundo zatsopano.

22Paulo anayimirira mʼbwalo la Areopagi nati: “Inu anthu a ku Atene! Ine ndikuona kuti mʼnjira zonse ndinu opembedza kwambiri. 23Pakuti pamene ndimayenda ndi kuona zinthu zimene mumazipembedza, ndapezanso guwa lansembe lolembedwapo kuti, kwa mulungu wosadziwika. Tsopano chimene mumachipembedza osachidziwa ndi chimene ndikuchilalikira.

24“Mulungu amene analenga dziko lapansi ndiponso zonse zili mʼmenemo ndiye Ambuye wakumwamba ndi dziko lapansi ndipo sakhala mʼnyumba zachipembedzo zomangidwa ndi manja. 25Ndipo satumikiridwa ndi manja a anthu ngati kuti Iye amasowa kanthu, chifukwa Iye ndiye amapereka moyo ndi mpweya kwa anthu onse ndi zina zonse. 26Kuchoka kwa munthu mmodzi Iye analenga mtundu uliwonse wa anthu, kuti akakhale pa dziko lonse lapansi; ndipo Iye anakonzeratu nthawi yawo ndiponso malo enieni kumene adzakhale. 27Mulungu anachita izi kuti anthu amufunefune, ndikuti pomufunafunapo amupeze ngakhale kuti Iye sali kutali ndi aliyense wa ife. 28‘Pakuti timakhala mwa Iye, kuyenda mwa Iye ndi kukhala moyo mwa Iye.’ Monga olemba ndakatulo anu ena akuti, ‘Ife ndi zidzukulu zake.’

29“Tsono popeza ndife ana a Mulungu, tisaganize kuti umulungu wake ndi wofanana ndi ndalama zagolide, zasiliva, mwala, kapenanso fanizo lopangidwa mwaluso la nzeru za anthu. 30Nthawi imene anthu sankadziwa, Mulungu anawalekerera koma tsopano akulamulira kuti anthu onse, kulikonse atembenuke mtima. 31Pakuti Iye wayika tsiku limene adzaweruze dziko lapansi mwa chilungamo kudzera mwa Munthu amene anamusankha. Iye watsimikizira anthu onse zimenezi pomuukitsa.”

32Atamva za kuuka kwa akufa, ena a iwo anaseka, koma enanso anati, “Ife tikufuna tidzamvenso zimenezi tsiku lina.” 33Ndipo Paulo anatuluka mʼBwalolo. 34Anthu ena ochepa anamutsatira Paulo ndipo anakhulupirira. Pakati pawo panali Dionisiyo mmodzi wa bwalo la Areopagi ndi mayi wina wotchedwa Damalisi ndi enanso.