何西阿书 12 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

何西阿书 12:1-14

1以法莲以风为食,

整天追逐东风,

虚谎和暴力日益增多;

他跟亚述结盟,

埃及进贡橄榄油。”

2耶和华指控犹大

要按雅各所行的惩罚他,

雅各所做的报应他。

3雅各在母胎之中曾抓住哥哥的脚跟,

壮年之时曾跟上帝角力。

4他跟天使角力得胜,

向天使哭求福分。

他在伯特利遇见祂,

在那里与祂说话——

5就是万军之上帝耶和华,

耶和华是祂的名。

6所以,你们要归向你们的上帝,

持守仁爱和公义,常常等候祂。

7以法莲是个不诚实的商人,

手里拿着骗人的秤,喜欢压榨人。

8以法莲说:“我发财了,

我依靠自己致富。

没有人能从我的劳碌中找出过错和罪恶。”

9耶和华说:

“从你们在埃及的时候,

我就是你们的上帝耶和华。

我要使你们再次住在帐篷里,

就像从前守节期时一样。

10我曾对先知讲话,赐给他们许多异象,

借他们用比喻警告你们。”

11基列人充满罪恶,终必灭亡。

他们在吉甲用公牛献祭,

他们的祭坛像田间犁沟里的石堆。

12雅各曾逃往亚兰

以色列在那里为娶妻而服侍人,

为得到妻子而替人牧羊。

13耶和华借着先知带领以色列离开埃及

也借着先知保护他。

14以法莲却极大地触怒耶和华,

所以他的主要让他血债血还,

以羞辱还羞辱。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 12:1-14

1Efereimu amadya mpweya;

tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa

ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa.

Amachita mgwirizano ndi Asiriya

ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.

2Yehova akuyimba mlandu Yuda;

Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake,

adzamulanga molingana ndi ntchito zake.

3Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake;

iye atakula analimbana ndi Mulungu.

4Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana;

analira napempha kuti amukomere mtima.

Mulungu anakumana naye ku Beteli

ndipo anayankhula naye kumeneko,

5Yehova Mulungu Wamphamvuzonse,

Yehova ndiye dzina lake lotchuka!

6Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu;

pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama,

ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.

7Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo;

iyeyo amakonda kubera anthu.

8Efereimu amadzitama ponena kuti,

“Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri.

Palibe amene angandiloze chala

chifukwa cha kulemera kwanga.”

9“Ine ndine Yehova Mulungu wako

amene ndinakutulutsa mu Igupto.

Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti,

monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.

10Ndinayankhula ndi aneneri,

ndinawaonetsa masomphenya ambiri,

ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”

11Kodi Giliyadi ndi woyipa?

Anthu ake ndi achabechabe!

Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala?

Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala

mʼmunda molimidwa.

12Yakobo anathawira ku dziko la Aramu,

Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi,

ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.

13Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto;

kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.

14Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri.

Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa.

Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.