Velsignelsen ved at gøre Guds vilje
1Gud velsigner de mennesker,
som ikke går efter gudløses råd,
står bag syndige handlinger,
eller sidder og håner Herren,
2men som ønsker at gøre hans vilje,
og har hans ord i tanke både dag og nat.
3De er som træer, der vokser ved vandløb
og bærer frugt hver eneste høst,
og hvis blade altid er grønne.
Alt, hvad de gør, lykkes for dem.
4Anderledes er det med de gudløse.
De er som avner, vinden blæser bort.
5På dommens dag står de straf skyldige,
de hører ikke hjemme blandt Guds folk.
6Herren hjælper dem, der gør hans vilje,
men de gudløses vej ender i afgrunden.
BUKU LOYAMBA
Masalimo 1–41
Salimo 1
1Wodala munthu
amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa,
kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa,
kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
2Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova
ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
3Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,
umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake
ndipo masamba ake safota.
Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
4Sizitero ndi anthu oyipa!
Iwo ali ngati mungu
umene umawuluzidwa ndi mphepo.
5Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo,
kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
6Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama,
koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.