Yesaia 61 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Yesaia 61:1-11

Awurade Adom Afe

1Otumfo Awurade Honhom wɔ me so,

efisɛ, wɔafrɛ me

sɛ memmɛka asɛmpa nkyerɛ ahiafo.

Wasoma me se, menkɔkyekye wɔn a wɔn koma abubu werɛ,

se mempae mu nka ahofadi nkyerɛ nnommum

na wonyi nneduafo mfi sum mu,

2se mempae mu nka Awurade adom no ho asɛm,

ne yɛn Nyankopɔn aweretɔ da.

Wasoma me se, menkyekye wɔn a wodi awerɛhow nyinaa werɛ,

3na memma wɔn a wodi awerɛhow wɔ Sion no nea wohia,

na menhyɛ wɔn ahenkyɛw fɛfɛ

nsi nsõ anan mu,

anigye ngo

nsi awerɛhowdi anan mu,

ayeyi atade

nsi abasamtu honhom anan mu.

Wɔbɛfrɛ wɔn trenee adum

nea Awurade adua

de ada nʼanuonyam adi.

4Wobesi tete mmubui no bio,

na wɔasiesie mmeaemmeae a asɛe dedaada no;

wɔbɛyɛ nkuropɔn a asɛe no foforo

nea asɛe awo ntoatoaso bebree no.

5Ananafo bɛhwɛ mo nguankuw;

ahɔho bɛyɛ adwuma wɔ mo mfuw ne bobeturo mu.

6Na wɔbɛfrɛ mo Awurade asɔfo,

wɔbɛto mo din sɛ yɛn Nyankopɔn asomfo.

Amanaman no ahonya no na mubedi

na wɔn ahode na mode bɛhoahoa mo ho.

7Wɔn animguase anan mu

me nkurɔfo benya anuonyam mmɔho,

na ahohora anan mu

wɔbɛsɛpɛw wɔn ho wɔ wɔn adedi mu;

ne saa nti wɔn asase no so kyɛfa bɛyɛ mmɔho,

na anigye a enni awiei bɛyɛ wɔn dea.

8“Na me Awurade, mepɛ atɛntrenee.

Mikyi korɔn ne nnebɔne.

Me nokware mu, mɛbɔ wɔn aba so

na me ne wɔn ayɛ apam a ɛbɛtena hɔ daa.

9Wɔn asefo begye din wɔ amanaman no mu

ne wɔn mma wɔ nkurɔfo no mu.

Wɔn a wohu wɔn nyinaa begye ato mu sɛ

wɔyɛ nnipa a Awurade ahyira wɔn.”

10Awurade mu na me ho sɛpɛw me mmoroso,

me Nyankopɔn mu na me kra di ahurusi.

Efisɛ, ɔde nkwagye ntama afura me

na ɔde trenee atade yuu awura me,

sɛnea ayeforokunu siesie me ti so sɛ ɔsɔfo,

ne sɛnea ayeforo de nnwinne hyehyɛ ne ho no.

11Na sɛnea asase ma afifide pue

na turo nso ma aba nyin no,

saa ara na Otumfo Awurade bɛma trenee ne ayeyi

apue wɔ amanaman anim.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 61:1-11

Uthenga Wabwino wa Yehova

1Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine,

chifukwa Yehova wandidzoza

kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka.

Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima,

ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu

ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.

2Wandituma kuti ndikalengeze nthawi imene Yehova adzapulumutsa anthu ake;

za tsiku limene Yehova adzalanga adani a anthu ake.

Wandituma kuti ndikatonthoze olira.

3Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni,

nkhata ya maluwa yokongola

mʼmalo mwa phulusa,

ndiwapatse mafuta achikondwerero

mʼmalo mwa kulira.

Ndiwapatse chovala cha matamando

mʼmalo mwa mtima wopsinjika.

Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo,

yoyidzala Yehova

kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.

4Adzamanganso mabwinja akale a mzinda

ndipo malo amene anawonongeka kalekale aja adzakonzanso.

Adzakonzanso mizinda imene inapasuka,

imene yakhala yowonongeka kwa nthawi yayitali kwambiri.

5Anthu achilendo adzakutumikirani; adzazidyetsa ziweto zanu;

iwo adzagwira ntchito mʼminda yanu ya mpesa.

6Ndipo inu mudzatchedwa ansembe a Yehova,

adzakutchulani kuti ndinu atumiki a Mulungu wathu.

Mudzadyerera chuma cha mitundu ya anthu,

ndipo mudzanyadira ulemu umene mwalandira.

7Chifukwa manyazi awo anali owirikiza;

ndi kuti munalandira

chitonzo ndi kutukwana,

adzakondwera ndi cholowa chawo,

tsono adzalandira cholowa chawo cha chigawo cha dziko mowirikiza,

ndipo chimwemwe chamuyaya chidzakhala chawo.

8“Pakuti Ine Yehova, ndimakonda chilungamo;

ndimadana ndi zakuba ndi zoyipa.

Anthu anga ndidzawapatsa mphotho mokhulupirika

ndikupangana nawo pangano losatha.

9Ana awo adzakhala odziwika pakati pa mitundu ya anthu

ndipo adzukulu awo adzakhala otchuka pakati pa anthu a mitundu ina.

Aliyense wowaona adzazindikira

kuti ndi anthu amene Yehova wawadalitsa.”

10Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova;

moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga.

Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso,

ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo.

Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake,

ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.

11Monga momwe nthaka imameretsa mbewu

ndiponso monga munda umakulitsa mbewu zimene anadzala,

momwemonso Ambuye Yehova adzaonetsa chilungamo ndi matamando

pamaso pa mitundu yonse ya anthu.