Yesaia 60 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Yesaia 60:1-22

Sion Anuonyam

1“Sɔre, hyerɛn, na wo hann aba,

na Awurade anuonyam apue wo so.

2Hwɛ, sum akata asase so

na sum kabii akata aman no so,

nanso Awurade apue wo so

na nʼanuonyam ada adi wɔ wo so.

3Amanaman bɛba wo hann no mu,

na Ahemfo bɛba wo adekyee hann no mu.

4“Ma wʼani so na hwɛ wo ho hyia:

wɔn nyinaa aboa wɔn ho ano reba wo nkyɛn;

wo mmabarima fifi akyirikyiri,

na wokura wo mmabea wɔ abasa so.

5Afei wobɛhwɛ na wʼanim atew,

wo koma bɛbɔ na anigye ahyɛ no ma;

ahonya a ɛwɔ po so, wɔde bɛbrɛ wo,

na amanaman no ahode nso bɛba wo nkyɛn.

6Yoma akuwakuw bɛyɛ wʼasase so ma,

yomaforo a wufi Midian ne Efa.

Na wɔn a wofi Seba nyinaa bɛba,

wɔsoso sika kɔkɔɔ ne nnuhuam

na wɔpae mu ka Awurade ayeyi.

7Wɔbɛboaboa Kedar nguankuw nyinaa ano abrɛ wo,

Nebaiot adwennini bɛsom wo;

wobegye wɔn sɛ afɔrebɔde wɔ mʼafɔremuka so,

na mɛhyɛ mʼasɔredan kronkron no anuonyam.

8“Henanom ne eyinom a wotu sɛ omununkum,

te sɛ mmorɔnoma a wɔrekɔ wɔn berebuw mu yi?

9Ampa ara asupɔw no ani da me so;

Tarsis ahyɛn na wodi anim,

wɔde wo mmabarima fifi akyirikyiri reba,

wɔsoso wɔn dwetɛ ne wɔn sikakɔkɔɔ,

de rebɛhyɛ Awurade, wo Nyankopɔn anuonyam,

Israel Kronkronni No,

efisɛ wahyɛ wo anuonyam.

10“Ananafo bɛto wʼafasu no bio,

na wɔn ahemfo bɛsom wo.

Ɛwɔ mu, mede abufuw asɛe wo de,

nanso menam adom so behu wo mmɔbɔ.

11Wo apon ano bɛdeda hɔ bere biara,

wɔrentoto mu awia anaa anadwo,

sɛnea ɛbɛyɛ a nkurɔfo de amanaman no ahonya bɛbrɛ wo,

wɔn ahemfo dii nkonimdi santen no anim.

12Na ɔman anaa ahenni a wɔrensom wo no bɛyera,

wɔbɛsɛe no pasaa.

13“Lebanon anuonyam bɛba wo nkyɛn,

ɔpepaw, ɔsɛsɛ ne kwabɔhɔre bɛbɔ mu,

abesiesie me kronkronbea hɔ;

na mɛhyɛ beae a me nan sisi no anuonyam.

14Wo nhyɛsofo mmabarima bɛba abɛkotow wo;

wɔn a wobu wo animtiaa nyinaa bɛkotow wʼanan ase

na wɔbɛfrɛ wo Awurade Kuropɔn,

Israel Kronkronni, Sion.

15“Ɛwɔ mu, wɔapa wʼakyi atan wo,

a obiara ntu kwan mfa wo mu,

nanso mɛyɛ wo ahohoahoade a ɛte hɔ daa

ne awo ntoatoaso nyinaa anigyede.

16Wobɛnom amanaman nufusu no

na woanum adehye nufu.

Afei wubehu sɛ me Awurade, me ne wo Agyenkwa,

wo gyefo, Yakob Tumfo no.

17Mede sikakɔkɔɔ besi kɔbere anan mu abrɛ wo,

na dwetɛ asi dade anan mu.

Mede kɔbere besi dua anan mu abrɛ wo,

na dade asi abo anan mu.

Mede asomdwoe bɛyɛ wo so amrado

na trenee ayɛ wo sodifo.

18Wɔrente awurukasɛm wɔ wʼasase so bio,

anaa nnwiriwii ne ɔsɛe wɔ wʼahye so

mmom wobɛfrɛ wʼafasu se Nkwagye

ne wʼapon se Ayeyi.

19Owia renyɛ wo hann adekyee mu bio

na ɔsram hann renhyerɛn wo so,

efisɛ Awurade bɛyɛ wo daapem hann,

na wo Nyankopɔn bɛyɛ wo anuonyam.

20Wo wia rentɔ bio,

wo sram rennum bio,

Awurade bɛyɛ wo daapem hann,

na wʼawerɛhownna to betwa.

21Na afei wo nkurɔfo nyinaa bɛyɛ atreneefo

na wɔbɛfa asase no adi so afebɔɔ.

Wɔyɛ ade a madua na afefɛw

me nsa ano adwuma a

ɛbɛda mʼanuonyam adi.

22Mo mu akumaa koraa bɛdɔ ayɛ apem,

na aketewa no ayɛ ɔman kɛse.

Mene Awurade;

na ne bere mu, mɛyɛ eyi ntɛm so.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 60:1-22

Ulemerero wa Ziyoni

1“Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika,

ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.

2Taona, mdima waphimba dziko lapansi

ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina,

koma Yehova adzakuwalira iwe,

ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.

3Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako

ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.

4“Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika.

Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe;

ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali

ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.

5Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri,

mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe;

chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe

chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.

6Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako,

ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai.

Ndipo onse a ku Seba adzabwera

atanyamula golide ndi lubani

uku akutamanda Yehova.

7Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu,

nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani;

zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe,

ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.

8“Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo,

ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?

9Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali;

patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi,

zikubweretsa ana ako ochokera kutali,

pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo,

kudzalemekeza Yehova Mulungu wako,

Woyerayo wa Israeli,

pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.

10“Alendo adzamanganso malinga ako,

ndipo mafumu awo adzakutumikira.

Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya,

koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.

11Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse,

sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku,

kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo,

akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.

12Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe;

adzawonongeka kotheratu.

13“Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini,

mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni

kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika;

ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.

14Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani;

onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu.

Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova;

Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.

15“Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe,

koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya,

ndipo udzakhala malo a chimwemwe

cha anthu amibado yonse.

16Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu

ndi kuleredwa pa maere aufumu,

motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako,

Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.

17Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa,

ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo.

Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa

ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala.

Olamulira ako adzakhala a mtendere.

Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.

18Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako,

bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako,

ndidzakhala malinga ako okuteteza

ndipo udzanditamanda.

19Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire,

kapena mwezi kuti uwunikire usiku,

pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya,

ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.

20Dzuwa lako silidzalowanso,

ndipo mwezi wako sudzazimiriranso;

Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya,

ndipo masiku a mavuto ako adzatha.

21Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama

ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya.

Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala,

ntchito ya manja anga,

kuti aonetse ulemerero wanga.

22Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko,

kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu.

Ine ndine Yehova,

nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”