Yeremia 30 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Yeremia 30:1-24

Wogye Israel Si Hɔ

1Asɛm a efi Awurade nkyɛn baa Yeremia hɔ ni: 2“Sɛɛ na Awurade, Israel Nyankopɔn, se: ‘Kyerɛw nsɛm a maka akyerɛ wo nyinaa gu nhoma mu. 3Nna bi reba,’ sɛnea Awurade se, ‘a mede me nkurɔfo Israelfo ne Yudafo befi nnommum mu asan aba na mede wɔn aba asase a mede maa wɔn agyanom sɛ wɔmfa ntena so no so,’ Awurade na ose.”

4Eyi ne nsɛm a Awurade ka faa Israel ne Yuda ho: 5“Nea Awurade se ni:

“ ‘Akomatu nteɛteɛmu na mete,

mete basabasayɛ, na ɛnyɛ asomdwoe.

6Mummisa na munhu:

Ɔbarima betumi awo mma ana?

Afei, adɛn nti na mihu ɔbarima hoɔdenfo biara

sɛ ne nsa gu ne yafunu so te sɛ ɔbea a ɔwɔ awoko mu,

na anim biara ayɛ bosaa saa?

7Sɛnea da no bɛyɛ hu afa!

Da biara renyɛ sɛ ɛno.

Ɛbɛyɛ amanehunu bere ama Yakob,

nanso wobeyi no afi mu.

8“ ‘Saa da no,’ Asafo Awurade na ose,

‘Mebubu konnua no afi wɔn kɔn mu,

na matetew wɔn nkyehama no mu;

ananafo remfa wɔn nyɛ nkoa bio.

9Na mmom wɔbɛsom Awurade, wɔn Nyankopɔn

ne Dawid, wɔn hene,

a mɛpagyaw no ama wɔn.

10“ ‘Enti nsuro, Yakob, me somfo;

mma wʼaba mu mmu, Israel,’

nea Awurade se ni.

‘Nokware, megye wo afi akyirikyiri,

ne wʼasefo afi wɔn nnommum asase so.

Yakob bɛsan anya asomdwoe ne bammɔ

na obiara renhunahuna no bio.

11Me ne wo wɔ hɔ na megye wo nkwa,’

Awurade na ose.

‘Ɛwɔ mu, mesɛe amanaman no nyinaa pasaa,

emu na mebɔ mo ahwete kɔ,

nanso merensɛe mo korakora.

Mɛteɛteɛ mo, nanso mɛyɛ no wɔ trenee kwan so;

meremma mo mfa mo ho nni koraa a merentwe mo aso.’

12“Sɛɛ na Awurade se:

“ ‘Wʼapirakuru ayɛ akisikuru,

na wontumi nsa.

13Obiara nni hɔ a ɔbɛka bi ama wo,

wo kuru no rennya aduru,

na worennya ayaresa.

14Wʼapamfo nyinaa werɛ afi wo;

wo ho biribiara mfa wɔn ho.

Mabɔ wo sɛnea wo tamfo bɛyɛ

na matwe wʼaso sɛnea otirimɔdenfo bɛtwe,

efisɛ wʼafɔdi so dodo

na wʼamumɔyɛ nso dɔɔso.

15Adɛn nti na wusu dennen wɔ wʼapirakuru,

wo yawdi a ano nni aduru no ho?

Wʼafɔdi kɛse ne wʼamumɔyɛ bebrebe nti

na mede saa nneɛma yi ayɛ wo.

16“ ‘Nanso wɔbɛsɛe wɔn a wɔsɛe mo;

mo atamfo nyinaa bɛkɔ nnommum mu.

Wɔn a wɔfow mo no wɔbɛfow wɔn

wɔn a wɔtow hyɛɛ mo so no, mɛtow ahyɛ wɔn so.

17Nanso mɛma wo ahoɔden bio

na masa wʼapirakuru,’

Awurade na ose,

‘efisɛ wɔfrɛ wo nea wɔapam no,

Sion a wo ho nhia obiara.’ ”

18Sɛɛ na Awurade se:

“ ‘Mɛsan de Yakob ntamadan mu ahonyade aba

na manya ayamhyehye ama nʼatenae ahorow no;

wɔbɛkyekye kuropɔn no bio wɔ ne mmubui so,

na ahemfi no besi nea ɛsɛ sɛ esi.

19Wɔn mu na aseda nnwom befi aba

ne ahosɛpɛw nnyigyei.

Mɛma wɔadɔɔso,

na wɔn dodow no so rentew;

mɛhyɛ wɔn anuonyam,

na wɔremmu wɔn abomfiaa.

20Wɔn mma bedi yiye sɛ kan no,

mɛma wɔn asafo atim wɔ mʼanim;

wɔn a wɔhyɛ wɔn so nyinaa mɛtwe wɔn aso.

21Wɔn kannifo bɛyɛ wɔn ankasa nipa;

na wɔn sodifo befi wɔn mu.

Mɛka no abata me ho na wabɛn me,

na hena na ɔde ne ho bɛma

sɛ ɔbɛbɛn me?’ ”

Awurade na ose.

22“ ‘Enti mobɛyɛ me nkurɔfo,

na mayɛ mo Nyankopɔn.’ ”

23Hwɛ, Awurade ahum

betu abufuwhyew mu,

mfɛtɛ bedi kyinhyia wɔ

amumɔyɛfo mpampam.

24Awurade abufuw rennwo

kosi sɛ obewie

ne koma mu nhyehyɛe nyinaa.

Nna a ɛreba no mu no

mobɛte eyi ase.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 30:1-24

Kubwezeretsedwa kwa Israeli

1Yehova anawuza Yeremiya kuti, 2“Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Lemba mʼbuku mawu onse amene ndakuwuza. 3Nthawi ikubwera pamene ndidzachotse anthu anga, Israeli ndi Yuda kuchokera ku ukapolo ndi kuwabwezera dziko limene ndinapatsa makolo awo,’ akutero Yehova.”

4Nawa mawu amene Yehova anayankhula ndi anthu a ku Israeli ndi Yuda: 5“Yehova akuti:

“Ndamva kulira chifukwa cha nkhawa,

ndamva kulira kwa mantha popeza palibe mtendere.

6Tsono khalani pansi ndi kudzifunsa kuti:

Kodi munthu wamwamuna angathe kubereka mwana?

Nanga nʼchifukwa chiyani ndikuona munthu aliyense wamwamuna

atagwira manja ake pa mimba pake ngati mayi pa nthawi yake yochira?

Chifukwa chiyani nkhope iliyonse ili yakugwa?

7Mayo ine! Tsiku limeneli ndi lalikulu kwambiri!

Sipadzakhala lina lofanana nalo.

Idzakhala nthawi ya masautso kwa Yakobo,

koma adzapulumuka ku masautsowo.”

8Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pa tsiku limenelo,

ndidzathyola goli la ukapolo mʼkhosi mwawo

ndipo ndidzadula zingwe zowamanga;

Aisraeli sadzakhalanso akapolo a alendo.

9Mʼmalo mwake, adzatumikira Yehova Mulungu wawo

ndiponso Davide mfumu yawo,

amene ndidzawasankhira.

10“ ‘Tsono usachite mantha, iwe mtumiki wanga Yakobo;

usade nkhawa, iwe Israeli,’

akutero Yehova.

‘Ndithu ndidzakupulumutsa kuchokera ku dziko lakutali,

zidzukulu zako kuchokera ku dziko la ukapolo wawo.

Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala modekha pa mtendere,

ndipo palibe amene adzamuchititsa mantha.

11Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani,’

akutero Yehova.

‘Ngakhale ndidzawononga kotheratu mitundu yonse ya anthu

kumene ndinakubalalitsirani,

koma inu sindidzakuwonongani kotheratu.

Sindidzakulekani kuti mukhale osalangidwa.

Koma ndidzakulangani mwachilungamo.’ ”

12Yehova akuti,

“Chilonda chanu nʼchosachizika,

bala lanu ndi lonyeka.

13Palibe amene angathe kukutetezani pa mlandu wanu,

palibe chiyembekezo choti inu nʼkuchira,

palibe mankhwala ochiritsa inu.

14Abwenzi anu onse akuyiwalani;

sasamalanso za inu.

Ndakukanthani ngati mmene mdani akanachitira.

Ndipo ndakulangani mwa nkhanza,

chifukwa machimo anu ndi ambiri,

ndipo kulakwa kwanu ndi kwakukulu.

15Chifukwa chiyani mukulira nacho chilonda chanu?

Bala lanu silingapole ayi.

Ine ndakuchitani zimenezi chifukwa machimo anu ndi ambiri

ndipo kulakwa kwanu nʼkwakukulu.

16“Tsono onse amene anakuwonongani, nawonso adzawonongedwa;

adani anu onse adzapita ku ukapolo.

Iwo amene anafunkha zinthu zanu, zinthu zawo zidzafunkhidwanso;

onse amene anakusakazani nawonso adzasakazidwa.

17Ndidzachiza matenda anu

ndi kupoletsa zilonda zanu,

akutero Yehova,

‘chifukwa mukutchedwa anthu otayika.

Amati, ndi anthu a ku Ziyoni awa amene alibe wowasamala.’ ”

18Yehova akuti,

“Ndidzabwera nalo banja la Yakobo ku dziko lawo

ndipo ndidzachitira chifundo malo ake okhalamo;

mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso pa bwinja pake,

nyumba yaufumu idzamangidwanso pa malo pake penipeni.

19Anthuwo adzayimba nyimbo zoyamika Yehova

ndipo kudzamveka phokoso lachisangalalo.

Ndidzawachulukitsa,

ndipo chiwerengero chawo sichidzatsika;

ndidzawapatsa ulemerero,

ndipo sadzanyozedwanso.

20Ana awo adzakhalanso monga mmene analili kale,

ndipo gulu lawo ndidzalikhazikitsa pamaso panga;

ndidzalanga onse owazunza.

21Mtsogoleri wawo adzakhala mmodzi mwa iwo.

Wodzawalamulira adzachokera pakati pawo.

Choncho ndidzawakokera kufupi ndi Ine ndipo iye adzandiyandikira.

Ndani angalimbe mtima payekha kuyandikana nane

popanda kuyitanidwa?”

akutero Yehova.

22“Choncho inu mudzakhala anthu anga,

ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu.”

23Taonani ukali wa Yehova wowomba

ngati mphepo ya mkuntho.

Mphepo ya namondwe

ikuwomba pa mitu ya anthu oyipa.

24Mkwiyo woopsa wa Yehova sudzachoka

mpaka atakwaniritsa zolinga

za mu mtima mwake.

Mudzamvetsa zimenezi

masiku akubwerawo.