Nnwom 2 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 2:1-12

Dwom 2

1Adɛn nti na amanaman no hyehyɛ bɔne ho

na nnipa no bɔ pɔw hunu yi?

2Asase so ahemfo sɔre gyina

na sodifo ka wɔn ho bɔ mu

tia Awurade ne Nea Wɔasra no no.

3Wɔka se,

“Momma yemmubu wɔn nkɔnsɔnkɔnsɔn

na yɛntow wɔn mpokyerɛ ngu.”

4Nea ɔte agua so wɔ ɔsoro no serew;

Awurade di wɔn ho fɛw.

5Afei ɔka wɔn anim wɔ nʼabufuw mu,

hunahuna wɔn wɔ nʼabufuwhyew mu, ka se,

6“Masi me Hene

wɔ Sion, me bepɔw kronkron no so.”

7Mɛpae mu aka Awurade ahyɛde:

Ɔka kyerɛɛ me se, “Woyɛ me Ba;

nnɛ mayɛ wʼAgya.

8Bisa me,

na mede amanaman nyinaa bɛyɛ wʼagyapade,

asase ano nyinaa bɛyɛ wo de.

9Wode dade ahempema bedi wɔn so;

na woabobɔ wɔn sɛ ɔnwemfo ahina.”

10Enti mo ahemfo, munsua nyansa;

monkae kɔkɔbɔ yi, mo asase sodifo.

11Momfa osuro nsom Awurade

na monsɛpɛw mo ho ahopopo mu.

12Mumfew Ɔba no ano, na ne bo amfuw

na mo akwan de mo bɛkɔ ɔsɛe mu,

efisɛ nʼabufuwhyew tumi sɔre mpofirim.

Nhyira ne wɔn a woguan toa no nyinaa.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 2:1-12

Salimo 2

1Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu?

Akonzekeranji zopanda pake anthu?

2Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo;

ndipo olamulira asonkhana pamodzi

kulimbana ndi Ambuye

ndi wodzozedwa wakeyo.

3Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo

ndipo titaye zingwe zawo.”

4Wokhala mmwamba akuseka;

Ambuye akuwanyoza iwowo.

5Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake

ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,

6“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga

pa Ziyoni, phiri langa loyera.”

7Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula:

Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga;

lero Ine ndakhala Atate ako.

8Tandipempha,

ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako;

malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.

9Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo;

udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”

10Kotero, inu mafumu, chenjerani;

chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.

11Tumikirani Yehova mwa mantha

ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.

12Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye;

kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu,

pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa.

Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.