Nnwom 143 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 143:1-12

Dwom 143

Dawid dwom.

1Awurade, tie me mpaebɔ,

tie me mmɔborɔsu;

fi wo nokwaredi ne trenee mu

bra bɛboa me.

2Mfa wʼakoa nkɔ atemmu mu,

na ɔteasefo biara nteɛ wɔ wʼanim.

3Ɔtamfo no taa me,

ɔbɔ me hwe fam;

ɔma me tena sum mu

te sɛ wɔn a wowuwuu dedaada.

4Ɛno nti me honhom atɔ beraw wɔ me mu;

na me koma di yaw wɔ me mu.

5Mekae tete nna no;

midwinnwen wo nnwuma

ne nea wo nsa ayɛ nyinaa ho.

6Mema me nsa so kyerɛ wo;

wo ho sukɔm de me kra sɛ asase kesee.

7Awurade, gye me so ntɛm;

me honhom tɔ piti.

Mfa wʼanim nhintaw me

anyɛ saa a mɛyɛ sɛ wɔn a wɔkɔ amoa mu no.

8Ma mente wʼadɔe a ɛnsa da no ho asɛm daa anɔpa,

na mede me ho ato wo so.

Kyerɛ me ɔkwan a memfa so,

na wo na mema me kra so kyerɛ.

9Awurade gye me fi mʼatamfo nsam,

na wo mu na mede me ho hintaw.

10Kyerɛ me na menyɛ wʼapɛde,

na wo ne me Nyankopɔn;

ma wo honhom pa no

nkogya me asasetaw so.

11Awurade, wo din nti, kyɛe me nkwa so;

wo trenee mu, yi me fi ɔhaw mu.

12Fi wʼadɔe a ɛnsa da no mu mua mʼatamfo ano;

na sɛe wɔn a wokyi me no nyinaa,

na meyɛ wo somfo.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 143:1-12

Salimo 143

Salimo la Davide.

1Yehova imvani pemphero langa,

mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo;

mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu

bwerani kudzandithandiza.

2Musazenge mlandu mtumiki wanu,

pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.

3Mdani akundithamangitsa,

iye wandipondereza pansi;

wachititsa kuti ndikhale mu mdima

ngati munthu amene anafa kale.

4Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga;

mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.

5Ndimakumbukira masiku amakedzana;

ndimalingalira za ntchito yanu yonse,

ndimaganizira zimene manja anu anachita.

6Ndatambalitsa manja anga kwa Inu;

moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma.

Sela

7Yehova ndiyankheni msanga;

mzimu wanga ukufowoka.

Musandibisire nkhope yanu,

mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.

8Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika,

pakuti ine ndimadalira Inu.

Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo,

pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.

9Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova,

pakuti ndimabisala mwa Inu.

10Phunzitseni kuchita chifuniro chanu,

popeza ndinu Mulungu wanga;

Mzimu wanu wabwino unditsogolere

pa njira yanu yosalala.

11Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu;

mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.

12Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga;

wonongani adani anga,

pakuti ndine mtumiki wanu.