Dwom 142
Dawid de. Bere a na ɔwɔ ɔbodan mu no. Mpaebɔ.
1Meteɛ mu su frɛ Awurade;
mema me nne so su frɛ Awurade sɛ onhu me mmɔbɔ.
2Mihwie mʼahiasɛm gu nʼanim;
meka me haw kyerɛ no.
3Sɛ me kra tɔ beraw wɔ me mu a,
ɛyɛ wo na wunim me kwan.
Ɔkwan a menam so no
nnipa asum me afiri.
4Hwɛ na hu, obiara nni me nifa so;
mʼasɛm mfa obiara ho;
minni guankɔbea bi;
me nkwa mfa obiara ho.
5Awurade, misu frɛ wo;
mise, “Wone me guankɔbea,
me kyɛfa wɔ ateasefo asase so.”
6Tie me sufrɛ,
na mewɔ ahohia kɛse mu;
gye me fi mʼataafo nsam,
efisɛ wɔn ho yɛ den sen me.
7Yi me fi mʼafiase,
na makamfo wo din.
Afei atreneefo betwa me ho ahyia
esiane wo papa a woayɛ me no nti.
Salimo 142
Ndakatulo ya Davide, pamene iyeyo anali mʼphanga. Pemphero.
1Ndikulirira Yehova mofuwula;
ndikukweza mawu anga kwa Yehova kupempha chifundo.
2Ndikukhuthula madandawulo anga pamaso pake;
ndikufotokoza za masautso anga pamaso pake.
3Pamene mzimu wanga walefuka mʼkati mwanga,
ndinu amene mudziwa njira yanga.
Mʼnjira imene ndimayendamo
anthu anditchera msampha mobisa.
4Yangʼanani kumanja kwanga ndipo onani;
palibe amene akukhudzika nane.
Ndilibe pothawira;
palibe amene amasamala za moyo wanga.
5Ndilirira Inu Yehova;
ndikuti, “Ndinu pothawirapo panga,
gawo langa mʼdziko la anthu amoyo.”
6Mverani kulira kwanga
pakuti ndathedwa nzeru;
pulumutseni kwa amene akundithamangitsa
pakuti ndi amphamvu kuposa ine.
7Tulutseni mʼndende yanga
kuti nditamande dzina lanu.
Ndipo anthu olungama adzandizungulira
chifukwa cha zabwino zanu pa ine.