Hiob 21 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Hiob 21:1-34

1Na Hiob buae se,

2Muntie me nsɛm no yiye.

Momma eyi nyɛ awerɛkyekye a mode ma me.

3Munnya ntoboase mma me bere a merekasa,

na sɛ mekasa wie a, monkɔ so nni fɛw.

4“Minwiinwii hyɛ onipa ana?

Adɛn nti na ɛsɛ sɛ minya ntoboase?

5Monhwɛ me, na mo ho nnwiriw mo;

momfa mo nsa nkata mo ano.

6Sɛ midwen eyi ho a, mebɔ hu;

na me ho popo.

7Adɛn nti na amumɔyɛfo tena nkwa mu?

Wonyin kyɛ na wɔkɔ so di tumi.

8Wohu wɔn mma a atwa wɔn ho ahyia no nkɔso,

wohu wɔn nenanom.

9Ɔhaw nni wɔn afi mu, na ehu nni hɔ;

Onyankopɔn asotwe mma wɔn so.

10Wɔn anantwinini nnyɛ asaadwe;

na wɔn anantwibere nwo a wɔmpɔn.

11Wɔka wɔn mma bɔ mu te sɛ nguankuw;

na emu mmotafowa no huruhuruw.

12Wɔto nnwom wɔ akasae ne sanku so;

na wɔde atɛntɛbɛn nnyigyei gye wɔn ani.

13Wodi yiye wɔn nkwanna mu

na wɔkɔ ɔdae mu asomdwoe mu.

14Nanso wɔka kyerɛ Onyankopɔn se, ‘Fi yɛn so!

Yɛmpɛ sɛ yehu wʼakwan.

15Hena ne otumfo no a ɛsɛ sɛ yɛsom no?

Sɛ yɛbɔ no mpae a mfaso bɛn na yebenya?’

16Nanso wɔn nkɔso no nni wɔn nsam,

enti metwe me ho fi amumɔyɛfo afotu ho.

17“Nanso mpɛn ahe na wodum amumɔyɛfo kanea?

Mpɛn ahe na amanehunu ba wɔn so,

nea Onyankopɔn fi nʼabufuw mu de ba no?

18Mpɛn ahe na wɔyɛ sɛ sare wɔ mframa ano,

te sɛ ntɛtɛ a mframaden bi apra wɔn?

19Wɔka se, ‘Onyankopɔn kora onipa asotwe so de twɛn ne mma.’

Ɛsɛ sɛ ɔtwe onipa no ankasa aso ma ohu.

20Ma ɔno ankasa ani nhu ne sɛe;

ma Otumfo abufuwhyew no nka nʼani.

21Dɛn na ɛfa wɔn ho fa wɔn abusuafo a woagyaw wɔn akyi no ho

bere a asram a wɔatwa ama no aba awiei no?

22“Obi betumi akyerɛ Onyankopɔn nyansa,

wɔ bere a obu atitiriw mpo atɛn?

23Obi wu wɔ bere a ɔwɔ ahoɔden

ne ho tɔ no na nʼaso mu adwo no,

24na ne nipadua ayɛ frɔmfrɔm,

na hon ahyɛ ne nnompe ma.

25Ɔfoforo nso de ɔkra mu yawdi wu,

a wanka asetena pa anhwɛ da.

26Wosie wɔn nyinaa wɔ mfutuma koro mu,

ma asunson nnunu wɔn nyinaa.

27“Mahu mo adwene,

ɔkwan a mobɛfa so afom me.

28Moka se, ‘Onipa kɛse no fi wɔ he,

ntamadan a omumɔyɛfo no tenaa mu no?’

29So mummmisaa wɔn a wotu kwan no asɛm da?

Wɔn amanneɛbɔ mu nsɛm ho nhiaa mo

30sɛ onipa bɔne nya ne ti didi mu amanehunu da,

na wogye wɔn abufuwhyew da no ana?

31Hena na ɔde ne suban si nʼanim?

Hena na otua no nea wayɛ so ka?

32Wɔsoa no kɔ ɔda mu,

na wɔwɛn nʼaboda.

33Obon mu dɔte yɛ no dɛ;

nnipa nyinaa di nʼakyi,

na dɔm a wontumi nkan wɔn di nʼanim.

34“Enti ɛbɛyɛ dɛn na mode mo nsɛnhunu bɛkyekye me werɛ?

Mo mmuae nyɛ hwee sɛ atoro!”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 21:1-34

Mawu a Yobu

1Pamenepo Yobu anayankha kuti,

2“Mvetserani bwino mawu anga;

ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.

3Ndiloleni ndiyankhule

ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.

4“Kodi ine ndikudandaulira munthu?

Tsono ndilekerenji kupsa mtima?

5Ndipenyeni ndipo mudabwe;

mugwire dzanja pakamwa.

6Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri;

thupi langa limanjenjemera.

7Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo,

amakalamba ndi kusanduka amphamvu?

8Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo,

zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.

9Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha;

mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.

10Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa;

ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.

11Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa;

makanda awo amavinavina pabwalo.

12Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze;

amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.

13Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero

ndipo amatsikira ku manda mwamtendere.

14Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’

Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.

15Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire?

Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?

16Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo,

koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.

17“Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa?

Nʼkangati kamene tsoka limawagwera?

Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?

18Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo,

ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?

19Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’

Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.

20Mulole kuti adzionere yekha chilango chake,

kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.

21Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo,

pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?

22“Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru,

poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?

23Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse,

ali pa mtendere ndi pa mpumulo,

24thupi lake lili lonenepa,

mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.

25Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima,

wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.

26Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda

ndipo onse amatuluka mphutsi.

27“Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza,

ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.

28Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti,

matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’

29Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo?

Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?

30Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka,

kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?

31Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo?

Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?

32Iye amanyamulidwa kupita ku manda

ndipo anthu amachezera pa manda ake.

33Dothi la ku chigwa limamukomera;

anthu onse amatsatira mtembo wake,

ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.

34“Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo

palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”