Hiob 20 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Hiob 20:1-29

Sofar Mmuae A Ɛto So Abien

1Na Naamani Sofar buae se,

2Me tirim mu ntew me, na ɛhyɛ me sɛ mimmua

efisɛ me ho yeraw me yiye.

3Mate animka bi a egu me ho fi,

na ntease a minya no hyɛ me sɛ mimmua.

4“Ampa ara wunim sɛnea nneɛma te fi tete,

efi bere a wɔde nnipa duaa asase so no,

5sɛ amumɔyɛfo ani gye bere tiaa bi mu,

na wɔn a wonsuro nyame nso anigye nkyɛ.

6Ɛwɔ mu sɛ nʼahohoahoa kodu ɔsoro,

na ne ti kɔpem omununkum koraa a,

7ɔbɛyera afebɔɔ te sɛ nʼankasa nʼagyanan;

na wɔn a wohuu no no bebisa se, ‘Ɔwɔ he?’

8Otu kɔ te sɛ ɔdae, na wɔrenhu no bio,

wɔn werɛ fi te sɛ anadwo mu anisoadehu.

9Ani a ehuu no no renhu no bio;

na ne sibea nso renhu no bio.

10Ne mma bɛpata ahiafo;

ɛsɛ sɛ nʼankasa de nʼahonya san ma.

11Ne mmerantebere mu ahoɔden a ahyɛ ne nnompe ma no

ne no bɛkɔ mfutuma mu.

12“Ɛwɔ mu sɛ bɔne yɛ nʼanom dɛ

na ɔde sie ne tɛkrɛma ase,

13ɛwɔ mu sɛ ontumi nnyaa mu

na ɔma ɛka ne dudom,

14nanso, nʼaduan bɛyɛ nwen wɔ ne yafunu mu;

ɛbɛyɛ ɔwɔ ano bɔre wɔ ne mu.

15Ɔbɛfe ahonyade a ɔmenee no;

Onyankopɔn bɛma ne yafunu apuw agu.

16Ɔbɛfefe awɔ bɔre;

Ɔnanka se bekum no.

17Ɔrennya nsuwansuwa no nnom

nsubɔnten a nufusu ne ɛwo sen wɔ mu no.

18Ɔbɛdan nea ɔbrɛ nyae no aba a ɔrenni bi;

ɔremfa nʼaguadi mu mfaso nnye nʼani.

19Efisɛ ɔhyɛɛ ahiafo so ma wodii ohia buruburoo;

ɔde ne nsa ato afi a ɛnyɛ ɔno na osii so.

20“Ampa ara ɔrennya ahomegye mfi nea wapere anya no mu;

ɔrentumi mfa nʼademude nnye ne ho nkwa.

21Wafom nneɛma nyinaa awie;

ne nkɔso nnu baabiara.

22Nʼadedodow nyinaa mu no, ɔbɛkɔ ɔhaw mu;

na amanehunu a emu yɛ den bɛto no.

23Bere a nʼafuru ayɛ ma no,

Onyankopɔn bɛtɔ nʼabufuw gya agu ne so

na wabobɔ no basabasa.

24Ɛwɔ mu sɛ oguan fi dade akode ano

nanso bɛmma a ano yɛ kɔbere mfrafrae bɛwɔ no.

25Ɔtwe bɛmma no fi nʼakyi,

ano hyɛnhyɛn no fi ne brɛbo mu.

Ehu bɛba ne so;

26sum kabii retwɛn nʼademude.

Ogya a ɛnnɛw mu bɛhyew no,

na asɛe nea aka wɔ ne ntamadan mu.

27Ɔsoro bɛda nʼafɔdi adi,

na asase asɔre atia no.

28Nsuyiri bɛtwe ne fi akɔ,

saa ara na asuworo bɛyɛ Onyankopɔn abufuwhyew da no.

29Eyi ne nkrabea a Onyankopɔn de ma amumɔyɛfo,

agyapade a Onyankopɔn de ato hɔ ama wɔn ne no.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 20:1-29

Mawu a Zofari

1Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti

2“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe

chifukwa ndasautsidwa kwambiri.

3Ndikumva kudzudzula kondinyoza,

ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.

4“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale,

kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,

5kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha,

chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.

6Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba

ndipo mutu wake uli nengʼaa,

7iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe;

iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’

8Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso,

adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.

9Diso limene linamuona silidzamuonanso;

sadzapezekanso pamalo pake.

10Ana ake adzabwezera zonse

zimene iyeyo analanda anthu osauka;

11Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake

zidzagona naye limodzi mʼfumbi.

12“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake

ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,

13ngakhale salola kuzilavula,

ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,

14koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake;

chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.

15Adzachisanza chuma chimene anachimeza;

Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.

16Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo

ululu wa mphiri udzamupha.

17Sadzasangalala ndi timitsinje,

mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.

18Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya;

sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.

19Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo;

iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.

20“Chifukwa choti umbombo wake sutha,

sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.

21Palibe chatsala kuti iye adye;

chuma chake sichidzachedwa kutha.

22Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera;

mavuto aakulu adzamugwera.

23Akadya nʼkukhuta,

Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto

ngati mvula yosalekeza.

24Ngakhale athawe mkondo wachitsulo,

muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.

25Muviwo adzawutulutsira ku msana,

songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake.

Adzagwidwa ndi mantha aakulu;

26mdima wandiweyani ukudikira chuma chake.

Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza

ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.

27Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake;

dziko lapansi lidzamuwukira.

28Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake,

katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.

29Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa,

mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”