ملاكی 4 – PCB & CCL

Persian Contemporary Bible

ملاكی 4:1-6

فرا رسيدن روز داوری خداوند

1خداوند قادر متعال می‌فرمايد: «روز داوری مثل تنوری شعله‌ور فرا می‌رسد و همهٔ اشخاص مغرور و بدكار را مانند كاه می‌سوزاند. آنها مانند درخت تا ريشه خواهند سوخت و خاكستر خواهند شد.

2«اما برای شما كه ترس مرا در دل داريد، آفتاب عدالت با پرتو شفابخش خود طلوع خواهد كرد، و شما شاد و سبكبال مثل گوساله‌هايی كه به چراگاه می‌روند، جست و خيز خواهيد نمود. 3در آن روزی كه من تعيين كرده‌ام، بدكاران را مثل خاكستر زير پای خود له خواهيد كرد.

4«دستورات و قوانينی را كه بر كوه سينا توسط خدمتگزار خود موسی به همهٔ قوم اسرائيل دادم به ياد داشته باشيد و از آن اطاعت كنيد.

5«پيش از فرا رسيدن روز بزرگ و هولناک داوری خداوند، من رسولی شبيه ايليای نبی برای شما می‌فرستم. 6او دلهای پدران و فرزندان را دوباره به هم نزديک خواهد كرد و اين باعث خواهد شد كه من سرزمين شما را ويران نكنم.»

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Malaki 4:1-6

Tsiku la Yehova

1Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndithu tsiku likubwera; lidzayaka ngati ngʼanjo. Anthu onse odzikuza, ndi aliyense ochita zoyipa adzapsa ngati chiputu, ndipo pa tsiku limene likubweralo adzapserera ndi moto. Sipadzatsalira muzu kapena nthambi. 2Koma inu amene mumaopa dzina langa, dzuwa lachilungamo lidzakutulukirani lili ndi kuwala kokuchiritsani. Ndipo inu mudzatuluka ndi kulumphalumpha ngati ana angʼombe amene atulutsidwa mʼkhola. 3Tsiku limenelo inu mudzapondereza anthu oyipa; adzakhala phulusa ku mapazi anu pa tsiku limene Ine ndidzachite zinthu zimenezi,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

4Kumbukirani zophunzitsa za mtumiki wanga Mose, malamulo ndi malangizo amene ndinamupatsa pa Horebu kuti awuze Aisraeli onse.

5“Taonani, ndidzakutumizirani mneneri Eliya lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Yehova. 6Iye adzabweza mitima ya makolo kwa ana awo, ndi mitima ya ana kwa makolo awo. Kupanda kutero ndidzabwera kudzakantha dziko lanu ndi temberero.”